Add parallel Print Page Options

Kupambana kwa Chikondi

13 Ngakhale nditamayankhula mʼmalilime a anthu ndi a angelo, koma ngati ndilibe chikondi, ndili ngati chinganga chaphokoso kapena ngati chitsulo chosokosera. Ngati ndili ndi mphatso ya uneneri, nʼkumazindikira zinsinsi ndi kudziwa zonse, ndipo ngati ndili ndi chikhulupiriro chosuntha mapiri, koma wopanda chikondi, ine sindili kanthu. Ngati ndipereka zanga zonse kwa osauka ndi kupereka thupi langa kuti alitenthe, koma ngati ndilibe chikondi, ine sindipindula kanthu.

Chikondi nʼcholeza mtima, chikondi nʼchokoma mtima, chilibe nsanje, sichidzikuza, sichidzitamandira. Chikondi chilibe mwano, sichodzikonda, sichipsa mtima msanga, sichisunga mangawa. Chikondi sichikondwera ndi zoyipa koma chimakondwera ndi choonadi. Chimatchinjiriza nthawi zonse, chimakhulupirika nthawi zonse, chimakhala ndi chiyembekezo nthawi zonse, chimapirira nthawi zonse.

Chikondi ndi chosatha. Koma mphatso ya uneneri idzatha, pamene pali kuyankhula malilime adzatha, pamene pali chidziwitso chidzatha. Pakuti timadziwa zinthu pangʼono chabe ndipo timanenera pangʼono chabe. 10 Koma changwiro chikadzaoneka ndipo chopereweracho chidzatha. 11 Pamene ndinali mwana ndinkayankhula ngati mwana, ndinkaganiza ngati mwana, ndinkalingalira ngati mwana. Koma nditakula, zonse zachibwana ndinazisiya. 12 Pakuti tsopano tiona zinthu mosaoneka bwino ngati mʼgalasi loonera; kenaka tidzaziona maso ndi maso. Tsopano ndidziwa mosakwanira koma kenaka ndidzadziwa mokwanira, monga mmene Mulungu akundidziwira ine.

13 Ndipo tsopano zatsala zinthu zitatu: chikhulupiriro, chiyembekezo ndi chikondi. Koma chachikulu pa zonsezi ndi chikondi.

13 If I speak in the tongues[a](A) of men or of angels, but do not have love, I am only a resounding gong or a clanging cymbal. If I have the gift of prophecy(B) and can fathom all mysteries(C) and all knowledge,(D) and if I have a faith(E) that can move mountains,(F) but do not have love, I am nothing. If I give all I possess to the poor(G) and give over my body to hardship that I may boast,[b](H) but do not have love, I gain nothing.

Love is patient,(I) love is kind. It does not envy, it does not boast, it is not proud.(J) It does not dishonor others, it is not self-seeking,(K) it is not easily angered,(L) it keeps no record of wrongs.(M) Love does not delight in evil(N) but rejoices with the truth.(O) It always protects, always trusts, always hopes, always perseveres.(P)

Love never fails. But where there are prophecies,(Q) they will cease; where there are tongues,(R) they will be stilled; where there is knowledge, it will pass away. For we know in part(S) and we prophesy in part, 10 but when completeness comes,(T) what is in part disappears. 11 When I was a child, I talked like a child, I thought like a child, I reasoned like a child. When I became a man, I put the ways of childhood(U) behind me. 12 For now we see only a reflection as in a mirror;(V) then we shall see face to face.(W) Now I know in part; then I shall know fully, even as I am fully known.(X)

13 And now these three remain: faith, hope and love.(Y) But the greatest of these is love.(Z)

Footnotes

  1. 1 Corinthians 13:1 Or languages
  2. 1 Corinthians 13:3 Some manuscripts body to the flames