Readings for Celebrating Advent
6 Chifukwa mwana watibadwira,
mwana wamwamuna wapatsidwa kwa ife,
ndipo ulamuliro udzakhala pa phewa lake.
Ndipo adzamutcha dzina lake lakuti
Phungu Wodabwitsa, Mulungu Wamphamvu,
Atate Amuyaya, ndi Mfumu ya Mtendere.
7 Ulamuliro ndi mtendere wake
zidzakhala zopanda malire.
Iye adzalamulira ufumu wake ali pa
mpando waufumu wa Davide,
ndipo adzawukhazikitsa ndi kuwuchirikiza
mwa chiweruzo cholungama ndi pochita zachilungamo
kuyambira nthawi imeneyo mpaka muyaya.
Ndi mtima wake wonse, Yehova Wamphamvuzonse
watsimikiza kuchita zimenezi.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.