Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Yesaya 35

Chimwemwe cha Opulumutsidwa

35 Chipululu ndi dziko lopanda madzi zidzasangalala;
    dziko lowuma lidzakondwa
ndi kuchita maluwa. Dzikolo lidzakhala ndi maluwa ochuluka
    lidzasangalala kwambiri ndi kufuwula mwachimwemwe.
Lidzakhala ndi ulemerero monga wa ku mapiri a ku Lebanoni,
    maonekedwe ake wokongola adzakhala ngati a ku Karimeli ndi a ku Saroni.

Aliyense adzaona ulemerero wa Yehova,
    ukulu wa Mulungu wathu.
Limbitsani manja ofowoka,
    limbitsani mawondo agwedegwede;
nenani kwa a mitima yamantha kuti;
    “Limbani mtima, musachite mantha;
Mulungu wanu akubwera,
    akubwera kudzalipsira;
ndi kudzabwezera chilango adani anu;
    akubwera kudzakupulumutsani.”

Pamenepo maso a anthu osaona adzapenyanso
    ndipo makutu a anthu osamva adzatsekuka.
Anthu olumala adzalumpha ngati mbawala,
    ndipo osayankhula adzayimba mokondwera.
Akasupe adzatumphuka mʼchipululu
    ndipo mitsinje idzayenda mʼdziko lowuma,
mchenga wotentha udzasanduka dziwe,
    nthaka yowuma idzasanduka ya akasupe.
Pamene panali mbuto ya ankhandwe
    padzamera udzu ndi bango.

Ndipo kumeneko kudzakhala msewu waukulu;
    ndipo udzatchedwa Msewu Wopatulika.
Anthu odetsedwa
    sadzayendamo mʼmenemo;
    zitsiru sizidzasochera mʼmenemo.
Kumeneko sikudzakhala mkango,
    ngakhale nyama yolusa sidzafikako;
    sidzapezeka konse kumeneko.
Koma okhawo amene Yehova anawapulumutsa adzayenda mu msewu umenewu.
10     Iwo amene Yehova anawawombola adzabwerera.
Adzalowa mu mzinda wa Ziyoni akuyimba;
    kumeneko adzakondwa mpaka muyaya.
Adzakutidwa ndi chisangalalo ndi chimwemwe,
    ndipo chisoni ndi kudandaula zidzatheratu.

Masalimo 146:5-10

Wodala ndi amene thandizo lake ndi
    Mulungu wa Yakobo.
Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi,
    nyanja ndi zonse zili mʼmenemo;
    Yehova, amene ndi wokhulupirika kwamuyaya.
Iye amachitira chilungamo anthu oponderezedwa
    ndipo amapereka chakudya kwa anthu anjala.
Yehova amamasula amʼndende,
    Yehova amatsekula maso anthu osaona,
Yehova amadzutsa onse amene awerama pansi,
    Yehova amakonda anthu olungama.
Yehova amasamalira alendo
    ndipo amathandiza ana ndi akazi amasiye,
    koma amasokoneza njira za anthu oyipa.

10 Yehova ndiye Mfumu mpaka muyaya,
    Mulungu wako iwe Ziyoni, pa mibado yonse.

Tamandani Yehova.

Luka 1:46-55

Nyimbo ya Mariya

46 Ndipo Mariya anati:

“Moyo wanga ulemekeza Ambuye.
47     Ndipo mzimu wanga ukondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga,
48 pakuti wakumbukira
    kudzichepetsa kwa mtumiki wake.
Kuyambira tsopano mibado yonse idzanditcha wodala,
49     pakuti Wamkuluyo wandichitira ine zinthu zazikulu,
    dzina lake ndi loyera.
50 Chifundo chake chifikira kwa iwo amene amuopa Iye
    kufikira mibadomibado.
51 Iye wachita zamphamvu ndi dzanja lake;
    Iye anabalalitsa iwo amene ali onyada mʼmaganizo awo.
52 Iye anachotsa olamulira pa mipando yawo yaufumu,
    koma wakweza odzichepetsa.
53 Iye wakhutitsa a njala ndi zinthu zabwino
    koma anachotsa olemera wopanda kanthu.
54 Iye anathandiza mtumiki wake Israeli,
    pokumbukira chifundo chake.
55 Kwa Abrahamu ndi zidzukulu zake ku nthawi zonse
    monga ananena kwa makolo athu.”

Yakobo 5:7-10

Kupirira Mʼmasautso

Tsono abale, pirirani mpaka kubwera kwa Ambuye. Onani mmene amachitira mlimi. Amadikirira kuti zipatso zabwino zioneke mʼmunda mwake. Amayembekezera mokhazikika mtima kuyambira nthawi ya mvula yoyamba mpaka yotsiriza. Inunso mukhale owugwira mtima ndi osasinthika chifukwa Ambuye ali pafupi kubwera. Abale, musamanenezane zoyipa kuopa kuti mungadzaweruzidwe. Woweruza ali pa khomo!

10 Abale, tengerani chitsanzo cha aneneri amene anayankhula mʼdzina la Ambuye. Iwowo anakumana ndi zovuta koma anapirira.

Mateyu 11:2-11

Yohane ali mʼndende anamva zimene Khristu ankachita, ndipo anatumiza ophunzira ake kukamufunsa Iye. Anamufunsa kuti, “Kodi Inu ndinu uja ankanena kuti mudzabwerayu kapena tidikire wina?”

Yesu anayankha kuti, “Bwererani ndi kukamuwuza Yohane zimene mwamva ndi kuona. Osaona akuona, olumala akuyenda, akhate akuchiritsidwa, osamva akumva, akufa akuukitsidwa ndipo Uthenga Wabwino ukulalikidwa kwa osauka. Odala ndi munthu amene sakhumudwa chifukwa cha Ine.”

Pamene ophunzira a Yohane ankachoka, Yesu anayamba kuyankhula kwa gulu la anthu za Yohane kuti, “Kodi munkapita ku chipululu kuti mukaone chiyani? Kodi bango logwedezeka ndi mphepo? Nanga munkapita kukaona chiyani, munthu wovala zokongola? Ayi, wovala zokongola amakhala mʼnyumba za mafumu. Nanga munkapita kukaona chiyani? Mneneri kodi? Inde ndikuwuzani kuti munkakaona woposa mneneri. 10 Uyu ndi amene malemba akunena za iye kuti,

“Ine ndidzatuma mthenga wanga patsogolo panu
    amene adzakonza njira yanu.

11 Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti pakati pa obadwa ndi mkazi sipanaoneke wina aliyense wamkulu woposa Yohane Mʼbatizi; komatu amene ndi wamngʼono kwambiri mu ufumu wakumwamba ndi wamkulu koposa iye.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.