Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
68 “Alemekezeke Ambuye, Mulungu wa Israeli
chifukwa wabwera ndi kuwombola anthu ake.
69 Iye wakweza nyanga yachipulumutso kwa ife
mu nyumba ya mtumiki wake Davide.
70 (Monga mmene ananenera kudzera mwa aneneri oyera),
71 chipulumutso kuchoka kwa adani athu
ndi kuchoka mʼdzanja la onse otida,
72 kuonetsa chifundo kwa makolo athu
ndi kukumbukira pangano lake loyera,
73 lumbiro limene analumbira kwa kholo lathu Abrahamu:
74 kutilanditsa ife mʼdzanja la adani athu,
ndi kutipanga ife timutumikire Iye mopanda mantha,
75 mʼchiyero ndi mʼchilungamo masiku athu onse.
76 “Ndipo iwe mwana wanga udzatchedwa mneneri wa Wammwambamwamba;
pakuti udzapita patsogolo pa Ambuye kukonza njira yake,
77 kupatsa anthu ake chidziwitso cha chipulumutso
kudzera mwa chikhululukiro cha machimo awo,
78 chifukwa cha chifundo chachikulu cha Mulungu wathu,
ndipo kuwala kwa dzuwa kudzafikira ife kuchokera kumwamba,
79 kuwalira iwo okhala mu mdima
ndi mu mthunzi wa imfa,
kutsogolera mapazi athu mu njira yamtendere.”
18 Nʼchifukwa chake Yehova ponena za Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda akuti,
“Anthu sadzamulira maliro kapena kunena kuti,
‘Kalanga ine, mʼbale wanga! Kalanga ine mlongo wanga!
Anthu ake sadzamulira maliro kuti,
Kalanga ine, mbuye wathu! Taonani ulemerero wake wapita!’
19 Adzayikidwa ngati bulu,
kuchita kumuguguza ndi kukamutaya
kunja kwa zipata za Yerusalemu.”
20 “Tsono inu anthu a ku Yerusalemu, pitani ku mapiri a Lebanoni kuti mukalire mofuwula kumeneko,
mawu anu akamveke mpaka ku Basani.
Mulire mofuwula muli ku Abarimu
chifukwa abwenzi ako onse awonongeka.
21 Ndinakuchenjezani pamene munali pa mtendere.
Koma inu munati, ‘Sindidzamvera.’
Umu ndi mmene mwakhala mukuchitira kuyambira mukali aangʼono.
Simunandimvere Ine.
22 Mphepo idzakuchotserani abusa anu onse,
ndipo abwenzi anu adzatengedwa ku ukapolo.
Pamenepo mudzachita manyazi ndi kunyozedwa
chifukwa cha zoyipa zanu zonse.
23 Inu amene mumakhala mʼnyumba ya ku Lebanoni,
amene munamanga nyumba zanu pakati pa mikungudza,
mudzabuwula kwambiri pamene zowawa zidzakugwerani,
zonga za mkazi pa nthawi yake yochira!
24 “Pali Ine wamoyo, akutero Yehova, ngakhale iwe, Yehoyakini mwana wa Yehoyakimu mfumu ya ku Yuda, ukanakhala ngati mphete ya ku dzanja langa lamanja, ndikanakuvula nʼkukutaya. 25 Ndidzakupereka kwa amene akufuna kukupha, amene iwe umawaopa. Ndidzakupereka kwa Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni ndi anthu ake. 26 Iwe pamodzi ndi amayi ako amene anakubereka ndidzakupititsani ku dziko lachilendo. Ngakhale inu simunabadwire kumeneko, komabe mudzafera komweko. 27 Simudzabwereranso ku dziko limene mudzafuna kubwerera.”
28 Kodi Yehoyakini wakhala ngati mbiya yonyozeka,
yosweka imene anthu sakuyifunanso?
Kodi nʼchifukwa chake iye pamodzi ndi ana ake,
achotsedwa nʼkutayidwa ku dziko limene iwo sakulidziwa?
29 Iwe dziko, dziko, dziko,
Imva mawu a Yehova!
30 Yehova akuti,
“Munthu ameneyu mumutenge ngati wopanda ana,
munthu amene sadzakhala wochita bwino pamoyo wake wonse,
pakuti palibe ndi mmodzi yemwe mwa zidzukulu zake zomwe zidzachita bwino.
Palibe amene adzathe kukhala pa mpando waufumu wa Davide
ndi kulamulira Yuda.”
Yesu Adalitsa Ana Aangʼono
15 Anthu amabweretsanso ana aangʼono kwa Yesu kuti awadalitse. Ophunzira ataona izi, anawadzudzula. 16 Koma Yesu anayitana anawo kuti abwere kwa Iye nati, “Lolani ana abwere kwa Ine ndipo musawatsekereze, pakuti ufumu wa Mulungu uli wa anthu otere. 17 Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene salandira ufumu wa Mulungu ngati mwana wamngʼono, sadzalowamo.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.