Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 76

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo la Asafu.

76 Mulungu amadziwika mu Yuda;
    dzina lake ndi lotchuka mu Israeli.
Tenti yake ili mu Salemu,
    malo ake okhalamo mu Ziyoni.
Kumeneko Iye anathyola mivi yowuluka,
    zishango ndi malupanga, zida zankhondo.
            Sela

Wolemekezeka ndinu,
    wamphamvu kuposa mapiri amene ali ndi nyama zambiri.
Anthu owuma mtima amagona atalandidwa chuma,
    Iwowo amagona tulo tawo totsiriza;
palibe mmodzi wamphamvu
    amene angatukule manja ake.
Pa kudzudzula kwanu, Inu Mulungu wa Yakobo,
    kavalo pamodzi ndi galeta zimakhala chete zitagona pansi.
Inu nokha ndiye muyenera kuopedwa.
    Angathe kuyima pamaso panu ndani mukakwiya?
Kuchokera kumwamba Inu munalengeza chiweruzo,
    ndipo dziko linaopa ndi kukhala chete,
pamene Inu Mulungu munadzuka kuti muweruze,
    kupulumutsa onse osautsidwa mʼdziko.
            Sela
10 Zoonadi, ukali wanu pa anthu umakubweretserani matamando
    ndipo opulumuka ku ukali wanu mumawasunga pafupi nanu.

11 Chitani malumbiro kwa Yehova Mulungu wanu ndipo muwakwaniritse;
    anthu onse omuzungulira abweretse mphatso
    kwa Iye amene ayenera kuopedwa.
12 Iye amaswa mzimu wa olamulira;
    amaopedwa ndi mafumu a dziko lapansi.

Yesaya 66:1-13

Chiweruzo ndi Chiyembekezo

66 Yehova akuti,

“Kumwamba ndi mpando wanga waufumu
    ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga.
Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire,
    ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?
Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi,
    motero zonsezi ndi zanga?”
            Akutero Yehova.

“Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu:
    amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima,
    ndipo amamvera mawu anga.
Koma aliyense amene amapereka nsembe ngʼombe yayimuna
    amaphanso munthu,
ndipo aliyense amene amapereka mwana wankhosa,
    amaphanso galu.
Aliyense amene amapereka nsembe chopereka cha chakudya
    amaperekanso magazi a nkhumba.
Ndipo amene amafukiza lubani pa guwa lansembe la chikumbutso
    amapembedzanso fano.
Popeza iwo asankha njira zawozawo,
    ndiponso kusangalatsidwa ndi zonyansa zawo.
Inenso ndawasankhira chilango chowawa
    ndipo ndidzabweretsa pa iwo zimene amaziopa zija.
Pakuti pamene ndinawayitana palibe amene anayankha,
    pamene ndinayankhula palibe amene anatchera khutu.
Anachita zoyipa pamaso panga
    ndi kusankha kuchita zimene zimandinyansa zija.”

Imvani mawu a Yehova,
    inu amene mumanjenjemera ndi mawu ake:
“Abale anu amene amakudani,
    ndi kukuchotsani pakati pawo chifukwa cha dzina langa, amanena kuti,
‘Yehova alemekezeke
    kuti ife tione chimwemwe chanu!’
    Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.
Imvani mfuwu mu mzinda,
    imvani phokoso mʼNyumba ya Mulungu!
Limenelo ndi liwu la Yehova,
    kulanga adani ake onse.

“Mzinda uli ngati amayi apakati amene asanayambe kumva zowawa
    wachira kale;
asanayambe kumva ululu,
    wabala kale mwana wamwamuna.
Ndani anamvapo zinthu zoterezi?
    Ndani anazionapo zinthu zoterezi?
Kodi dziko nʼkupangika tsiku limodzi,
    kapena mtundu wa anthu nʼkubadwa tsiku limodzi?
Komatu Ziyoni atangoyamba kumva zowawa
    nthawi yomweyo anabereka ana ake.
Kodi Ine ndingangofikitsa amayi apakati mpaka nthawi yake yochira,
    koma osalola kuti abaledi mwana?” akutero Yehova.
“Kodi ndingatseke mimba
    pa nthawi yoti abeleke?” akutero Mulungu wako.
10 “Kondwera nayeni Yerusalemu ndipo musangalale chifukwa cha Iye,
    inu nonse amene mumakonda Yerusalemu,
kondwera nayeni kwambiri,
    nonse amene mumamulira.
11 Pakuti mudzagawana naye ulemerero wake
    ngati kuyamwa ndi kukhuta mkaka wambiri
wa mʼmawere
    a chitonthozo chake.”

12 Yehova akuti,

“Ndidzamupatsa mtendere ngati mtsinje wa madzi,
    ndiponso chuma cha anthu a mitundu ina ngati mtsinje wosefukira.
Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene amayi ake amunyamulira pambalipa,
    kapena kumufungata pa miyendo yake.
13 Monga momwe amayi amasangalatsira mwana wawo,
    moteronso Ine ndidzakusangalatsani;
    ndipo mudzasangalala chifukwa cha Yerusalemu.”

1 Akorinto 10:23-11:1

Ufulu wa Munthu Wokhulupirira

23 Mutha kunena kuti, “Zinthu zonse nʼzololedwa,” komatu si zonse zili za phindu. “Zinthu zonse nʼzololedwa,” komatu si zonse zimathandiza. 24 Munthu aliyense asafunefune zokomera iye yekha, koma zokomeranso ena.

25 Idyani nyama iliyonse imene amagulitsa pa msika, osafunsa mafunso okhudzana ndi chikumbumtima chanu. 26 Popeza kuti, “Dziko lapansi ndi la Ambuye ndi zonse za mʼmenemo ndi zake.”

27 Ngati wosakhulupirira akuyitanani kuti mukadye naye, inuyo ndi kuvomera kupitako, mukadye chilichonse chimene akakupatseni ndipo musakafunse mafunso okhudzana ndi chikumbumtima chanu. 28 Koma ngati wina akuwuzani kuti, “Izi zaperekedwa nsembe,” musadye zimenezo, pofuna kuthandiza amene wakuwuzaniyo komanso chifukwa cha chikumbumtima. 29 Ndikunena za chikumbumtima cha winayo osati chanu. Tsono mungafunse kuti, nʼchifukwa chiyani ufulu wanga ukuphwanyidwa chifukwa cha chikumbumtima cha munthu wina? 30 Ngati ndikuyamika Mulungu chifukwa cha chakudya, nanga munthu angandinyoze bwanji pa zinthu zomwe ndayamikira nazo Mulungu?

31 Nʼchifukwa chake chilichonse mungadye kapena kumwa, kapena chimene mungachite, chitani zonse ku ulemerero wa Mulungu. 32 Musakhumudwitse aliyense, kaya ndi Myuda, Mgriki, kapena mpingo wa Mulungu. 33 Mu zonse ndikuyesetsa kukondweretsa aliyense mʼnjira iliyonse. Popeza sindikufunafuna zokondweretsa ine ndekha koma zokomera ambiri kuti apulumutsidwe.

11 Tsatirani chitsanzo changa, monga inenso nditsatira chitsanzo cha Khristu.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.