Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Nyimbo za Mayamiko
12 Tsiku limenelo aliyense wa inu adzati:
“Ndikukuyamikani, Inu Yehova;
chifukwa ngakhale munandipsera mtima,
mkwiyo wanu wachoka,
ndipo mwanditonthoza.
2 Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga;
ndidzamudalira ndipo sindidzachita mantha.
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;
Iye wakhala chipulumutso changa.”
3 Mudzakondwera popeza Yehova
ali ngati chitsime cha chipulumutso chanu.
4 Tsiku limenelo mudzati:
“Yamikani Yehova, tamandani dzina lake;
mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu,
ndipo mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.
5 Imbirani Yehova, pakuti wachita ntchito zazikulu;
zimenezi zidziwike pa dziko lonse lapansi.
6 Fuwulani ndi kuyimba mwachimwemwe, inu anthu a ku Ziyoni;
pakuti Woyerayo wa Israeli ndi wamkulu pakati panu.”
Mpumulo kwa Anthu Osweka Mtima
14 Ndipo panamveka mawu akuti,
“Undani, undani, konzani msewu!
Chotsani zotchinga pa njira yoyendamo anthu anga.”
15 Pakuti Iye amene ali Wamkulu ndi Wopambanazonse,
amene alipo nthawi zonse, amene dzina lake ndi Woyerayo,
akunena kuti, “Ndimakhala pamalo aulemu ndi opatulika,
koma ndimakhalanso ndi munthu wodzichepetsa ndi wosweka mtima
kuti odzichepetsawo ndiwalimbitse
ndi kuwachotsa mantha osweka mtima.
16 Sindidzawatsutsa anthu mpaka muyaya
kapena kuwapsera mtima nthawi zonse,
popeza kuti ndinalenga anthu anga
ndi kuwapatsa mpweya wamoyo.
17 Ine ndinakwiya kwambiri chifukwa cha tchimo lawo ladyera;
ndinawalanga ndi kuwafulatira mokwiya,
koma iwo anapitirirabe kuchita ntchito zawo zoyipa.
18 Ndaona zochita zawo, komabe ndidzawachiritsa;
kuwapumulitsa ndi kuwapatsa mtendere,
19 anthu olira a mu Israeli adzanditamanda ndi milomo yawo.
Anthu amene ali kutali ndi apafupi pomwe ndidzawapatsa mtendere,”
“Ndipo ndidzawachiritsa.”
Akutero Yehova.
20 Koma anthu oyipa ali ngati nyanja yowinduka,
yosatha kukhala bata,
mafunde ake amaponya matope ndi ndere.
21 “Palibe mtendere kwa oyipa,” akutero Mulungu wanga.
Mkwiyo wa Mulungu pa Mtundu wa Anthu
18 Mkwiyo wa Mulungu ukuonekera kuchokera kumwamba. Ukutsutsana ndi kusapembedza konse ndi kuyipa kwa anthu amene amapondereza choonadi mwa chikhalidwe chawo choyipa. 19 Za Mulungu zimene zingathe kudziwika, ndi zomveka bwino kwa iwo pakuti Mulungu anazionetsera kwa iwo. 20 Pakuti kuyambira pamene dziko lapansi linalengedwa, zinthu zosaoneka za Mulungu, mphamvu zake zosatha ndi chikhalidwe cha umulungu, zakhala zikuoneka bwinobwino. Akhala akuzindikira poona zimene Mulungu analenga, kotero kuti anthu sangathe kuwiringula.
21 Ngakhale iwo anadziwa Mulungu, sanamulemekeze ngati Mulungu kapena kumuthokoza, koma maganizo awo anasanduka wopanda pake ndipo mʼmitima yawo yopusa munadzaza mdima. 22 Ngakhale ankadzitama kuti ndi anzeru, anasanduka opusa. 23 Iwo anasinthanitsa ulemerero wa Mulungu wosafa ndi mafano opangidwa ndi manja wooneka ngati munthu amene amafa, kapena ngati mbalame, ndi nyama kapena zokwawa.
24 Nʼchifukwa chake Mulungu anawasiya kuti azingochita zilakolako zochititsa manyazi zauchimo zomwe mitima yawo inkafuna. Zotsatira zake anachita za chiwerewere wina ndi mnzake kunyazitsa matupi awo. 25 Iwo anasinthanitsa choonadi cha Mulungu ndi bodza ndipo anapembedza ndi kutumikira zinthu zolengedwa mʼmalo mwa Mlengi amene ali woyenera kutamandidwa mpaka muyaya. Ameni.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.