Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Yoweli 2:23-32

23 Inu anthu a ku Ziyoni sangalalani,
    kondwerani mwa Yehova Mulungu wanu,
pakuti wakupatsani
    mvula yoyambirira mwachilungamo chake.
Iye wakutumizirani mivumbi yochuluka,
    mvula yoyambirira ndi mvula ya nthawi ya mphukira, monga poyamba paja.
24 Pa malo opunthira padzaza tirigu;
    mʼmitsuko mudzasefukira vinyo watsopano ndi mafuta.

25 “Ine ndidzakubwezerani zonse zimene zinawonongedwa ndi dzombe,
    dzombe lalikulu ndi dzombe lalingʼono,
    dzombe lopanda mapiko ndi dzombe lowuluka;
gulu langa lalikulu la nkhondo limene ndinalitumiza pakati panu.
26 Mudzakhala ndi chakudya chambiri, mpaka mudzakhuta,
    ndipo mudzatamanda dzina la Yehova Mulungu wanu,
    amene wakuchitirani zodabwitsa;
ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
27 Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndili mu Israeli,
    kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu,
    ndi kuti palibenso wina;
ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.

Tsiku la Yehova

28 “Ndipo patapita nthawi,
    ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse.
Ana anu aamuna ndi ana anu aakazi adzanenera,
    nkhalamba zanu zidzalota maloto,
    anyamata anu adzaona masomphenya.
29 Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi
    ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo.
30 Ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga
    ndi pa dziko lapansi,
    ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.
31 Dzuwa lidzadetsedwa
    ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi
    lisanafike tsiku lalikulu ndi loopsa la Ambuye.
32 Ndipo aliyense amene adzayitana
    pa dzina la Ambuye adzapulumuka;
pakuti chipulumutso chidzakhala pa Phiri la Ziyoni
    ndi mu Yerusalemu,
    monga Yehova wanenera,
pakati pa otsala
    amene Yehova wawayitana.

Masalimo 65

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Nyimbo.

65 Matamando akudikira Inu Mulungu mu Ziyoni;
    kwa inu malumbiro athu adzakwaniritsidwa.
Inu amene mumamva pemphero,
    kwa inu anthu onse adzafika.
Pamene tinathedwa nzeru ndi machimo,
    Inu munakhululukira mphulupulu zathu.
Odala iwo amene inu muwasankha
    ndi kuwabweretsa pafupi kukhala mʼmabwalo anu!
Ife tadzazidwa ndi zinthu zabwino za mʼNyumba mwanu,
    za mʼNyumba yanu yoyera.

Mumatiyankha ife ndi ntchito zodabwitsa zachilungamo,
    Inu Mulungu Mpulumutsi wathu,
chiyembekezo cha mathero onse a dziko lapansi
    ndi cha nyanja zomwe zili kutali kwambiri,
amene munapanga mapiri ndi mphamvu zanu,
    mutadziveka nokha ndi mphamvu.
Amene munakhalitsa bata nyanja
    kukokoma kwa mafunde ake,
    ndi phokoso la anthu a mitundu ina.
Iwo amene akukhala kutali amaopa zizindikiro zozizwitsa zanu;
    kumene dzuwa limatulukira ndi kumene dzuwa limalowera.
    Inu mumafuna nyimbo zachimwemwe.

Inu mumasamalira dziko lapansi ndi kulithirira;
    Inuyo mumalilemeretsa kwambiri.
Mtsinje wa Mulungu ndi wodzaza ndi madzi
    kuti upereke tirigu kwa anthu,
    pakuti Inu munakhazikitsa zimenezi.
10 Mwadzaza nthaka yake ndi madzi ndi kusalaza migula yake,
    mwayifewetsa ndi mvula yamawawa ndi kudalitsa mbewu zake.
11 Inu mumaveka chaka ndi zinthu zochuluka,
    ndipo ngolo zanu zimasefukira ndi zinthu zochuluka.
12 Malo a udzu a mʼchipululu amasefukira;
    mapiri avekedwa ndi chisangalalo.
13 Madambo akutidwa ndi zoweta
    ndi zigwa zavekedwa ndi tirigu;
    izo pamodzi zikufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe.

2 Timoteyo 4:6-8

Pakuti moyo wanga wayamba kale kuthiridwa ngati nsembe, ndipo nthawi yakwana yoti ndinyamuke ulendo wanga. Ndamenya nkhondo yabwino, ndatsiriza bwino mpikisano wa liwiro ndipo ndasunga chikhulupiriro. Tsopano mphotho yanga ikundidikira imene ndi chipewa cha chilungamo, imene Ambuye, woweruza wolungama, adzandipatsa pa tsiku lijalo, osati ine ndekha komanso onse amene akufunitsitsa kubwera kwake.

2 Timoteyo 4:16-18

16 Podziteteza koyamba pa mlandu wanga, panalibe ndi mmodzi yemwe amene anandithandiza, koma aliyense anandithawa. Mulungu awakhululukire. 17 Koma Ambuye anayima nane limodzi, ndipo anandipatsa mphamvu, kuti kudzera mwa ine, uthenga ulalikidwe kwambiri, ndikuti anthu a mitundu ina amve. Ndipo ndinalanditsidwa mʼkamwa mwa mkango. 18 Ambuye adzandilanditsa ku chilichonse chofuna kundichita choyipa ndipo adzandisamalira bwino mpaka kundilowetsa chonse mu ufumu wake wakumwamba. Kwa Iye kukhale ulemerero mpaka muyaya.

Luka 18:9-14

Fanizo la Mfarisi ndi Wolandira Msonkho

Yesu ananena fanizoli kwa amene amadzikhulupirira mwa iwo okha kuti anali wolungama nanyoza ena onse. 10 “Anthu awiri anapita ku Nyumba ya Mulungu kukapemphera, wina Mfarisi ndi winayo wolandira msonkho. 11 Mfarisiyo anayimirira ndipo anapemphera za iye mwini kuti, ‘Mulungu, ine ndikuyamika kuti sindili ngati anthu ena onse, achifwamba, ochita zoyipa, achigololo, sindilinso ngati wolandira msonkhoyu. 12 Ine ndimasala kudya kawiri pa Sabata ndipo ndimapereka chakhumi pa zonse ndimapeza.’

13 “Koma wolandira msonkhoyo ali chiyimire potero, sanathe nʼkomwe kuyangʼana kumwamba; koma anadziguguda pachifuwa ndipo anati, ‘Mulungu, chitireni chifundo, ine wochimwa.’

14 “Ine ndikukuwuzani kuti munthu wolandira msonkhoyu, osati Mfarisiyu, anapita kwawo atalungamitsidwa pamaso pa Mulungu. Chifukwa chake, aliyense wodzikweza adzachepetsedwa, ndipo wodzichepetsa adzakwezedwa.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.