Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 137

137 Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira
    pamene tinakumbukira Ziyoni.
Kumeneko, pa mitengo ya misondozi
    tinapachika apangwe athu,
pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo.
    Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo;
    iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”

Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova
    mʼdziko lachilendo?
Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu,
    dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.
Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga
    ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu,
ngati sindiyesa iwe
    chimwemwe changa chachikulu.

Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita
    pa tsiku limene Yerusalemu anagonja.
Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi
    mpaka pa maziko ake!”

Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa,
    wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera
    pa zimene watichitira.
Amene adzagwira makanda ako
    ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.

Maliro 1:16-22

16 “Chifukwa cha zimenezi ndikulira
    ndipo maso anga adzaza ndi misozi.
Palibe aliyense pafupi woti anditonthoze,
    palibe aliyense wondilimbitsa mtima.
Ana anga ali okhaokha
    chifukwa mdani watigonjetsa.

17 “Ziyoni wakweza manja ake,
    koma palibe aliyense womutonthoza.
Yehova walamula kuti abale ake
    a Yakobo akhale adani ake;
Yerusalemu wasanduka
    chinthu chodetsedwa pakati pawo.

18 “Yehova ndi wolungama,
    koma ndine ndinawukira malamulo ake.
Imvani inu anthu a mitundu yonse;
    onani masautso anga.
Anyamata ndi anamwali anga
    agwidwa ukapolo.

19 “Ndinayitana abwenzi anga
    koma anandinyenga.
Ansembe ndi akuluakulu anga
    anafa mu mzinda
pamene ankafunafuna chakudya
    kuti akhale ndi moyo.

20 “Inu Yehova, onani mmene ine ndavutikira!
    Ndikuzunzika mʼkati mwanga,
ndipo mu mtima mwanga ndasautsidwa
    chifukwa ndakhala osamvera.
Mʼmisewu anthu akuphedwa,
    ndipo ku mudzi kuli imfa yokhayokha.

21 “Anthu amva kubuwula kwanga,
    koma palibe wonditonthoza.
Adani anga onse amva masautso anga;
    iwo akusangalala pa zimene Inu mwachita.
Lifikitseni tsiku limene munalonjeza lija
    kuti iwonso adzakhale ngati ine.

22 “Lolani kuti ntchito zawo zoyipa zifike pamaso panu;
    muwalange
ngati mmene mwandilangira ine
    chifukwa cha machimo anga onse.
Ndikubuwula kwambiri
    ndipo mtima wanga walefuka.”

Yakobo 1:2-11

Masautso ndi Mayesero

Abale, muchiyese ngati chimwemwe chenicheni nthawi zonse pamene mukukumana ndi mayesero amitundumitundu. Inu mukudziwa kuti kuyesedwa kwa chikhulupiriro chanu kumabweretsa chipiriro. Chipiriro chiyenera kugwira ntchito yake kuti mukhale okhwima ndi angwiro, osasowa kanthu kalikonse. Ngati wina pakati panu akusowa nzeru, apemphe kwa Mulungu amene amapereka kwa onse mwaulere ndi mosatonzera, ndipo adzapatsidwa. Koma pamene mupempha, muyenera kukhulupirira osakayika, chifukwa amene amakayika ali ngati mafunde pa nyanja amene amawinduka nakankhika ndi mphepo. Munthu wotere asayembekezere kulandira kalikonse kuchokera kwa Ambuye. Iyeyu ndi munthu wa mitima iwiri, wosakhazikika pa zimene akuchita.

Abale omwe ndi anthu wamba anyadire pamene akwezedwa. 10 Koma olemera anyadire pamene atsitsidwa, chifukwa adzatha ngati duwa lakuthengo. 11 Pakuti dzuwa limatuluka nʼkutentha kwake, ndipo limafotetsa zomera. Duwa lake limathothoka ndipo kukongola kwake kumatheratu. Momwemonso munthu wachuma adzazimirira ngakhale atamachitabe malonda ake.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.