Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
19 Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala,
zili ngati zowawa ndi ndulu.
20 Ine ndikuzikumbukira bwino izi,
ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.
21 Komabe ndimakumbukira zimenezi,
nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.
22 Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu,
ndi chifundo chake ndi chosatha.
23 Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse;
kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.
24 Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse;
motero ndimamuyembekezera.”
25 Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye,
kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;
26 nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha
Yehova modekha.
7 Pa masiku a masautso ndi kuzunzika kwake,
Yerusalemu amakumbukira chuma chonse
chimene mʼmasiku amakedzana chinali chake.
Anthu ake atagwidwa ndi adani ake,
panalibe aliyense womuthandiza.
Adani ake ankamuyangʼana
ndi kumuseka chifukwa cha kuwonongeka kwake.
8 Yerusalemu wachimwa kwambiri
ndipo potero wakhala wodetsedwa.
Onse amene ankamulemekeza pano akumunyoza,
chifukwa aona umaliseche wake.
Iye mwini akubuwula
ndipo akubisa nkhope yake.
9 Uve wake umaonekera pa zovala zake;
iye sanaganizire za tsogolo lake.
Nʼchifukwa chake kugwa kwake kunali kwakukulu;
ndipo analibe womutonthoza.
“Inu Yehova, taonani masautso anga,
pakuti mdani wapambana.”
10 Adani amulanda
chuma chake chonse;
iye anaona mitundu ya anthu achikunja ikulowa mʼmalo ake opatulika,
amene Inu Mulungu munawaletsa
kulowa mu msonkhano wanu.
11 Anthu ake onse akubuwula
pamene akufunafuna chakudya;
asinthanitsa chuma chawo ndi chakudya
kuti akhale ndi moyo.
“Inu Yehova, taonani ndipo ganizirani,
chifukwa ine ndanyozeka.”
12 “Kodi zimenezi mukuziyesa zachabe, inu nonse mukudutsa?
Yangʼanani ndipo muone.
Kodi pali mavuto ofanana ndi
amene andigwerawa,
amene Ambuye anandibweretsera
pa tsiku la ukali wake?
13 “Anatumiza moto kuchokera kumwamba,
unalowa mpaka mʼmafupa anga.
Anayala ukonde kuti ukole mapazi anga
ndipo anandibweza.
Anandisiya wopanda chilichonse,
wolefuka tsiku lonse.
14 “Wazindikira machimo anga onse
ndipo ndi manja ake anawaluka pamodzi.
Machimowa afika pakhosi panga,
ndipo Ambuye wandithetsa mphamvu.
Iye wandipereka
kwa anthu amene sindingalimbane nawo.
15 “Ambuye wakana
anthu anga onse amphamvu omwe ankakhala nane:
wasonkhanitsa gulu lankhondo kuti lilimbane nane,
kuti litekedze anyamata anga;
mʼmalo ofinyira mphesa Ambuye wapondereza
anamwali a Yuda.
Yesu Achiritsa Anthu Awiri Osaona
29 Pamene Yesu ndi ophunzira ake ankachoka ku Yeriko, gulu lalikulu la anthu linawatsata. 30 Amuna awiri osaona anakhala mʼmbali mwa msewu, ndipo pamene anamva kuti Yesu akudutsa anafuwula kuti, “Ambuye, Mwana wa Davide, tichitireni chifundo!”
31 Gulu la anthulo linawadzudzula iwo ndi kuwawuza kuti akhale chete, koma anafuwulitsabe kuti, “Ambuye, Mwana wa Davide, tichitireni chifundo!”
32 Yesu anayima ndi kuwayitana ndipo anawafunsa kuti, “Mukufuna ndikuchitireni chiyani?”
33 Anamuyankha nati, “Ambuye, tikufuna tione!”
34 Yesu anamva nawo chifundo ndipo anakhudza maso awo. Nthawi yomweyo anaona namutsata Iye.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.