Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
40 Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake
ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
41 Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina,
ndipo adani awo anawalamulira.
42 Adani awo anawazunza
ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
43 Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri,
koma iwo ankatsimikiza za kuwukira
ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
44 Koma Iye anaona kuzunzika kwawo
pamene anamva kulira kwawo;
45 Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake
ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
46 Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo
awamvere chisoni.
47 Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu,
ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina
kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera
ndi kunyadira mʼmatamando anu.
48 Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli,
Kuyambira muyaya mpaka muyaya.
Anthu onse anene kuti, “Ameni!”
Tamandani Yehova.
Mulungu ndi Mafano
10 Inu Aisraeli, imvani zimene Yehova akunena. 2 Yehova akuti,
“Musatsatire makhalidwe a anthu a mitundu ina
kapena kuchita mantha ndi zizindikiro zamlengalenga,
ngakhale anthu a mitundu ina amachita nazo mantha.
3 Pakuti miyambo ya mitundu inayo ndiyachabechabe.
Iwo amakadula mtengo ku nkhalango
ndipo mmisiri amawusema ndi sompho.
4 Amakongoletsa chosemacho ndi siliva ndi golide;
kenaka amachikhomerera ndi misomali
kuti chisagwedezeke.
5 Mafano awo ali ngati mtengo wakanjedza woopsezera mbalame mʼmunda wa minkhaka.
Mafanowo sangathe nʼkuyankhula komwe
ndipo ayenera kunyamulidwa
popeza sangathe nʼkuyenda komwe.
Musachite nawo mantha
popeza sangathe kukuchitani choyipa
ndiponso alibe mphamvu yochitira chabwino chilichonse.”
6 Palibe wofanana nanu, Inu Yehova;
Inu ndinu wamkulu,
ndipo dzina lanu lili ndi mphamvu yayikulu.
7 Ndani amene angaleke kukuopani,
inu Mfumu ya mitundu ya anthu?
Chimenechi ndicho chokuyenerani.
Pakati pa anthu anzeru onse komanso mafumu onse
a mitundu ya anthu,
palibe wina wofanana nanu.
8 Onsewo ndi opusa ndi opanda nzeru;
malangizo awo amawatenga kuchokera kwa mafano achabechabe opanga ndi mitengo.
9 Siliva wosula amabwera naye kuchokera ku Tarisisi
ndipo golide amachokera naye ku Ufazi.
Mafanowo ndi ntchito ya anthu aluso ndi odziwa kuzokota golide.
Tsono mafanowo amawaveka zovala za mtundu wamtambo ndi pepo.
Yonseyo ndi ntchito ya anthu a luso.
10 Koma Yehova ndiye Mulungu woona;
Iyeyo ndiye Mulungu wamoyo, Mfumu yamuyaya.
Akakwiya, dziko limagwedezeka;
anthu a mitundu ina sangathe kupirira ukali wakewo.
11 “Awuze anthu awa kuti, ‘Milungu iyi, imene sinalenge dziko lakumwamba ndi dziko lapansi, idzawonongeka pa dziko lapansi ndi pansi pa thambo.’ ”
12 Koma Mulungu analenga dziko lapansi ndi mphamvu zake;
Iye anapanga dziko lonse ndi nzeru zake
ndipo anayala thambo mwaluso lake.
13 Iye akayankhula, kumamveka mkokomo wamadzi akumwamba;
Iyeyo amabweretsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi.
Amabweretsa mphenzi pamodzi ndi mvula
ndi kutulutsa mphepo yamkuntho kumalo kumene osungirako.
14 Anthu onse ndi opusa ndiponso opanda nzeru;
mmisiri aliyense wosula golide akuchita manyazi ndi mafano ake.
Mafano akewo ndi abodza;
alibe moyo mʼkati mwawo.
15 Mafanowo ndi achabechabe, zinthu zosekedwa nazo.
Pamene anthuwo azidzaweruzidwa, mafanowo adzawonongedwa.
16 Koma Yehova amene ndi Cholowa cha Yakobo sali ngati mafanowo.
Iyeyu ndi Mlengi wa zinthu zonse
kuphatikizapo Israeli, mtundu umene anawusankha kuti ukhale anthu ake.
Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Ufulu wa Paulo
19 Ngakhale ndine mfulu ndipo sindine kapolo wa munthu, ndimadzisandutsa kapolo wa aliyense kuti ndikope ambiri mmene ndingathere. 20 Kwa Ayuda ndimakhala ngati Myuda kuti ndikope Ayuda. Kwa olamulidwa ndi Malamulo ndimakhala ngati wolamulidwa nawo (ngakhale kuti sindine wolamulidwa ndi Malamulowo) kuti ndikope amene amalamulidwa ndi Malamulo. 21 Kwa amene alibe Malamulo ndimakhala wopanda Malamulo (ngakhale kuti sindine wopanda Malamulo a Mulungu koma ndili pansi pa ulamuliro wa Khristu) kuti ndikope wopanda Malamulo. 22 Kwa ofowoka ndimakhala wofowoka, kuti ndikope ofowoka. Ndimachita zinthu zilizonse kwa anthu onse kuti mwanjira ina iliyonse ndipulumutse ena. 23 Ndimachita zonsezi chifukwa cha Uthenga Wabwino, kuti ndigawane nawo madalitso ake.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.