Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide.
58 Kodi inu olamulira mumayankhuladi molungama?
Kodi mumaweruza mwachilungamo pakati pa anthu?
2 Ayi, mʼmitima mwanu mumakonzekera zosalungama,
ndipo manja anu amatulutsa zachiwawa pa dziko lapansi.
3 Ngakhale kuchokera tsiku lawo lobadwa oyipa amasochera;
kuchokera mʼmimba ya amayi awo, iwo ndi otayika ndipo amayankhula mabodza.
4 Ululu wawo uli ngati ululu wa njoka,
ngati uja wa mphiri imene yatseka mʼmakutu mwake.
5 Imene simva liwu la munthu wamatsenga,
ngakhale akhale wa luso lotani munthu wamatsengayo.
6 Gululani mano mʼkamwa mwawo, Inu Mulungu,
Yehova khadzulani mano a mikango!
7 Mulole kuti asowe ngati madzi oyenda
pamene iwo akoka uta mulole kuti mivi yawo ikhale yosathwa.
8 Akhale ngati nkhono imene imasungunuka pamene ikuyenda;
ngati mwana wakufa asanabadwe, iwo asaone dzuwa.
9 Miphika yanu isanagwire moto waminga ya mkandankhuku,
kaya iyo ndi yobiriwira kapena yowuma, oyipa adzachotsedwa.
10 Olungama adzasangalala poona kubwezera chilango,
pamene adzasambitsa mapazi awo mʼmagazi a anthu oyipa.
11 Ndipo anthu adzanena kuti,
“Zoonadi, olungama amalandirabe mphotho;
zoonadi kuli Mulungu amene amaweruza dziko lapansi.”
15 Ndipo ndidzakupatsani abusa a pamtima panga amene adzakutsogolerani mwanzeru ndi mwaluntha. 16 Masiku amenewo mukadzachulukana kwambiri mʼdzikomo, anthu sadzanenanso za ‘Bokosi la Chipangano la Yehova’ kapena kuliganizira. Sadzalikumbukiranso kapena kulifuna, ndipo sadzapanganso lina,”
akutero Yehova.
17 Nthawi imeneyo adzatcha Yerusalemu Mpando Waufumu wa Yehova, ndipo mitundu yonse ya anthu idzasonkhana mu Yerusalemu pamaso pa Yehova. Sadzawumiriranso kutsata mitima yawo yoyipa. 18 Masiku amenewo fuko la Yuda lidzaphatikizana ndi fuko la Israeli, onse pamodzi adzachokera ku dziko la kumpoto kupita ku dziko limene ndinapatsa makolo awo, kuti likhale cholowa.
19 “Ine mwini ndinati,
“ ‘Ndikanakonda bwanji kukukhazikani pakati pa ana anga
ndikukupatsani dziko labwino kwambiri,
cholowa chokongola kwambiri kuposa cha mitundu ina ya anthu.’
Ndinaganiza kuti mudzanditcha Ine ‘Atate’
ndi kuti simudzaleka kunditsata.
20 Koma monga mkazi wosakhulupirika amasiya mwamuna wake,
momwemonso inu mwakhala osakhulupirika kwa Ine, inu fuko la Israeli,”
akutero Yehova.
21 Mawu akumveka pa magomo,
Aisraeli akulira ndi kupempha chifundo
chifukwa anatsata njira zoyipa
ndi kuyiwala Yehova Mulungu wawo.
22 Inu mukuti, “Bwererani, anthu osakhulupirika;
ndidzachiritsa kubwerera mʼmbuyo kwanu.”
“Inde, tidzabwerera kwa Inu
pakuti ndinu Yehova Mulungu wathu.
23 Ndithu kupembedza pa magomo
komanso kuchita maphwando pa mapiri zilibe phindu.
Zoonadi chipulumutso cha Israeli
chili mwa Yehova Mulungu wathu basi.
24 Kuyambira pa ubwana wathu milungu yochititsa manyazi ija yakhala ikutiwonongetsa phindu
la ntchito za makolo athu,
nkhosa ndi ngʼombe zawo,
ana awo aamuna ndi aakazi.
25 Tilekeni tigone pansi mwa manyazi,
ndipo kunyozeka kwathu kutiphimbe.
Paja tachimwira Yehova Mulungu wathu,
ife pamodzi ndi makolo athu
kuyambira nthawi ya ubwana wathu mpaka lero lino
sitinamvere Yehova Mulungu wathu.”
Fanizo la Phwando Lalikulu
15 Mmodzi mwa amene amadya naye atamva izi, anati kwa Yesu, “Ndi wodala munthu amene adzadye nawo mu ufumu wa Mulungu.”
16 Yesu anayankha kuti, “Munthu wina ankakonza phwando lalikulu ndipo anayitana alendo ambiri. 17 Nthawi yaphwando itakwana anatuma wantchito wake kuti akawuze onse amene anayitanidwa kuti, ‘Bwerani, pakuti zonse zakonzeka.’
18 “Koma onse anayamba kupereka zifukwa mofanana. Woyamba anati, ‘Ine ndangogula kumene munda, ndipo ndikuyenera kupita kuti ndikawuone. Pepani mundikhululukire.’
19 “Wina anati, ‘Ndangogula kumene ngʼombe khumi zokoka ngolo ndipo kupita kukaziyesa. Pepani mundikhululukire.’
20 “Wina anatinso, ‘Ine ndangokwatira kumene, choncho sinditha kubwera.’
21 “Wantchitoyo anabwera ndikudzamuwuza bwana wakeyo zimenezi. Pamenepo mphwandoyo anapsa mtima ndipo analamula wantchito wakeyo kuti, ‘Pita msangamsanga kunja mʼmisewu ndi mʼmakwalala a mu mzinda ndipo ukabweretse osauka, ofa ziwalo, osaona ndi olumala.’
22 “Wantchitoyo anati, ‘Bwana, zimene munanena zachitika koma malo akanalipobe.’
23 “Ndipo mbuye uja anawuza wantchito wake kuti, ‘Pita kunja ku misewu ikuluikulu ndi kunja kwa mpanda ndipo ukawawuze kuti alowe, kuti nyumba yanga idzaze. 24 Ine ndikukuwuzani inu kuti palibe ndi mmodzi yemwe mwa anthu amene anayitanidwa adzalawa phwandolo.’ ”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.