Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 58

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide.

58 Kodi inu olamulira mumayankhuladi molungama?
    Kodi mumaweruza mwachilungamo pakati pa anthu?
Ayi, mʼmitima mwanu mumakonzekera zosalungama,
    ndipo manja anu amatulutsa zachiwawa pa dziko lapansi.
Ngakhale kuchokera tsiku lawo lobadwa oyipa amasochera;
    kuchokera mʼmimba ya amayi awo, iwo ndi otayika ndipo amayankhula mabodza.
Ululu wawo uli ngati ululu wa njoka,
    ngati uja wa mphiri imene yatseka mʼmakutu mwake.
Imene simva liwu la munthu wamatsenga,
    ngakhale akhale wa luso lotani munthu wamatsengayo.

Gululani mano mʼkamwa mwawo, Inu Mulungu,
    Yehova khadzulani mano a mikango!
Mulole kuti asowe ngati madzi oyenda
    pamene iwo akoka uta mulole kuti mivi yawo ikhale yosathwa.
Akhale ngati nkhono imene imasungunuka pamene ikuyenda;
    ngati mwana wakufa asanabadwe, iwo asaone dzuwa.

Miphika yanu isanagwire moto waminga ya mkandankhuku,
    kaya iyo ndi yobiriwira kapena yowuma, oyipa adzachotsedwa.
10 Olungama adzasangalala poona kubwezera chilango,
    pamene adzasambitsa mapazi awo mʼmagazi a anthu oyipa.
11 Ndipo anthu adzanena kuti,
    “Zoonadi, olungama amalandirabe mphotho;
    zoonadi kuli Mulungu amene amaweruza dziko lapansi.”

Yeremiya 2:23-37

23 “Iwe ukunena bwanji kuti, ‘Ine sindinadziyipitse;
    sindinatsatire Abaala’?
Takumbukira mmene unkandichimwira mʼchigwa muja;
    zindikira bwino zomwe wachita.
Iwe uli ngati ngamira yayikazi yaliwiro
    yomangothamanga uku ndi uku,
24 wakhala ngati mbidzi yozolowera mʼchipululu,
    yonka ninunkhiza pa nthawi yachisika.
    Ndani angayiretse chilakolako chakecho?
Mphongo iliyonse yoyikhumba sidzavutika.
    Pa nthawi yachisika chakecho mphongoyo idzayipeza.
25 Iwe usathamange, nsapato zingakuthere kuphazi
    ndi kukhosi kwako kuwuma ndi ludzu.
Koma unati, ‘Zamkutu!
    Ine ndimakonda milungu yachilendo,
    ndipo ndidzayitsatira.’

26 “Monga momwe mbala imachitira manyazi pamene yagwidwa,
    moteronso nyumba ya Israeli idzachita manyazi;
Aisraeliwo, mafumu ndi akuluakulu awo,
    ansembe ndi aneneri awo.
27 Iwo amawuza mtengo kuti, ‘Iwe ndiwe abambo athu,’
    ndipo amawuza mwala kuti, ‘Iwe ndiye amene unatibala.’
Iwo andifulatira Ine,
    ndipo safuna kundiyangʼana;
Koma akakhala pa mavuto amati,
    ‘Bwerani mudzatipulumutse!’
28 Nanga ili kuti milungu yanu imene munadzipangira nokha?
    Ibweretu ngati ingathe kukupulumutsani
    pamene muli pamavuto!
Inu anthu a ku Yuda,
    milungu yanu ndi yambiri kuchuluka kwake ngati mizinda yanu.

29 “Kodi mukundizengeranji mlandu?
    Nonse mwandiwukira,”
            akutero Yehova.
30 “Ine ndinalanga anthu ako popanda phindu;
    iwo sanaphunzirepo kanthu.
Monga mkango wolusa,
    lupanga lanu lapha aneneri anu.

31 “Inu anthu a mʼbado uno, ganizirani bwino mawu a Yehova:

“Kodi Ine ndinakhalapo ngati chipululu kwa Israeli
    kapena ngati dziko la mdima wandiweyani?
Chifukwa chiyani anthu anga akunena kuti, ‘Ife tili ndi ufulu omayendayenda;
    sitidzabweranso kwa Inu’?
32 Kodi namwali amayiwala zokongoletsera zake,
    kapena kuyiwala zovala zake za ukwati?
Komatu anthu anga andiyiwala
    masiku osawerengeka.
33 Mumadziwa bwino njira zopezera zibwenzi!
    Choncho ngakhale akazi oyipa omwe mumawaphunzitsa njira zanu.
34 Ngakhale pa zovala zako anthu amapezapo
    magazi a anthu osauka osalakwa.
    Anthuwo simunawapeze akuthyola nyumba.
Komabe ngakhale zinthu zili chomwechi,
35     inu mukunena kuti, ‘Ndife osalakwa,
    sadzatikwiyira.’
Ndidzakuyimbani mlandu
    chifukwa mukunena kuti, ‘Ife sitinachimwe.’
36 Chifukwa chiyani
    mukunkabe nimusinthasintha njira zanu?
Aigupto adzakukhumudwitsani
    monga momwe Asiriya anakuchititsani manyazi.
37 Mudzachokanso kumeneko
    manja ali kunkhongo.
Popeza Ine Yehova ndawakana anthu amene munkawadalira,
    choncho sadzakuthandizani konse.

Ahebri 13:7-21

Muzikumbukira atsogoleri anu, amene amakulalikirani Mawu a Mulungu. Ganizirani zamoyo wawo ndipo tsatirani chikhulupiriro chawo. Yesu Khristu ndi yemweyo dzulo, lero ndi kunthawi zonse.

Musasocheretsedwe ndi ziphunzitso zosiyanasiyana zachilendo. Nʼkwabwino kuti mitima yathu ilimbikitsidwe ndi chisomo osati ndi chakudya, chimene sichipindulitsa iwo amene amachidya. 10 Ife tili ndi guwa lansembe, ndipo ansembe otumikira mʼtenti cha Ayuda, saloledwa kudya zochokera pamenepo.

11 Mkulu wa ansembe amatenga magazi kukapereka nsembe chifukwa cha machimo, koma nyamayo imawotchedwa kunja kwa msasa. 12 Nʼchifukwa chakenso Yesu anafera kunja kwa mzinda kuti ayeretse anthu ake kudzera mʼmagazi ake. 13 Tiyeni tsono, tipite kwa iye kunja kwa msasa, titasenza chitonzo chake. 14 Pakuti ife tilibe mzinda wokhazikika koma tikudikira mzinda umene ukubwera.

15 Tsono, tiyeni kudzera mwa Yesu tipereke nsembe zachiyamiko kwa Mulungu osalekeza, chipatso cha milomo imene imavomereza dzina lake. 16 Ndipo musayiwale kumachita zabwino ndi kuthandiza ena, pakuti Mulungu amakondwera ndi nsembe zotere. 17 Muzimvera atsogoleri anu ndi kugonjera ulamuliro wawo, iwo amakuyangʼanirani monga anthu amene adzayenera kufotokoza za ntchito yawo pamaso pa Mulungu. Muziwamvera kuti agwire ntchito yawo ndi chimwemwe osati molemedwa pakuti izi sizingakupindulireni.

18 Mutipempherere ifenso. Pakuti tikutsimikiza kuti tili ndi chikumbumtima changwiro ndipo timafuna kuchita zinthu zonse mwaulemu. 19 Ine ndikukupemphani kuti mundipempherere kuti Mulungu andibwezere kwa inu msanga.

20 Mulungu wamtendere, amene kudzera mʼmagazi a pangano lamuyaya anaukitsa Ambuye athu Yesu kwa akufa, amene ndi Mʼbusa wamkulu, 21 akupatseni chilichonse chabwino kuti muchite chifuniro chake ndipo Mulungu achite mwa ife, chimene chingamukomere kudzera mwa Yesu Khristu. Kwa Iye kukhale ulemerero ku nthawi zanthawi, Ameni.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.