Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a gititi. Salimo la Asafu.
81 Imbani mwachimwemwe kwa Mulungu mphamvu yathu;
Fuwulani mokweza kwa Mulungu wa Yakobo!
10 Ine ndine Yehova Mulungu wanu,
amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto.
Yasamani kukamwa kwanu ndipo ndidzakudyetsani.
11 “Koma anthu anga sanandimvere;
Israeli sanandigonjere.
12 Kotero ndinawasiya ndi mitima yawo yosamverayo
kuti atsate zimene ankafuna.
13 “Anthu anga akanangondimvera,
Israeli akanatsatira njira zanga,
14 nʼkanafulumira motani kuti ndigonjetse adani awo
ndi kutembenuza mkono wanga kulimbana ndi amaliwongo!
15 Iwo amene amadana ndi Yehova akanakhwinyata pamaso pake,
ndipo chilango chawo chinakakhala mpaka kalekale.
16 Koma inu mukanadyetsedwa tirigu wabwino kwambiri;
ndikanakukhutitsani ndi uchi wochokera pa thanthwe.”
Madandawulo a Yeremiya
12 Yehova, Inu mumakhala wokhoza nthawi zonse
ndikati nditsutsane nanu.
Komabe ndikufuna kuyankhula nanu za mlandu wanga.
Chifukwa chiyani anthu oyipa zinthu zimawayendera bwino?
Chifukwa chiyani anthu achinyengo amakhala pabwino?
2 Inu munawadzala ndipo anamera mizu;
amakula ndi kubereka zipatso.
Dzina lanu limakhala pakamwa pawo nthawi zonse,
koma mitima yawo imakhala kutali ndi Inu.
3 Koma Inu Yehova, ine mumandidziwa;
mumandiona ndipo mumayesa zolingalira zanga.
Akokeni anthu oyipawo ngati nkhosa zokaphedwa!
Ayikeni padera mpaka tsiku loti akaphedwe!
4 Kodi dziko lidzakhala likulirabe mpaka liti
ndipo udzu mʼmunda uliwonse udzakhalabe ofota mpaka liti?
Nyama ndi mbalame kulibiretu
chifukwa anthu amene amakhalamo ndi oyipa.
Iwo amati:
“Yehova sangathe kuona ntchito zathu.”
Yankho la Mulungu
5 Yehova anayankha kuti, “Ngati kukutopetsa kuthamanga pamodzi ndi anthu
nanga ungapikisane bwanji ndi akavalo?
Ngati ukupunthwa ndi kugwa pa malo abwino,
udzatha bwanji kuthamanga mʼnkhalango
za ku Yorodani?
6 Ngakhale abale ako
ndi anansi akuwukira,
onsewo amvana zokuyimba mlandu.
Usawakhulupirire,
ngakhale ayankhule zabwino ndi iwe.
7 “Ine ndawasiya anthu anga;
anthu amene ndinawasankha ndawataya.
Ndapereka okondedwa anga
mʼmanja mwa adani awo.
8 Anthu amene ndinawasankha
asanduka ngati mkango wa mʼnkhalango.
Akundibangulira mwaukali;
nʼchifukwa chake Ine ndikudana nawo.
9 Anthu anga amene ndinawasankha
asanduka ngati mbalame yolusa yamawangamawanga
imene akabawi ayizinga.
Pitani, kasonkhanitseni nyama zakuthengo.
Mubwere nazo kuti zidzadye mbalameyo.
10 Abusa ambiri anawononga munda wanga wa mpesa,
anapondereza munda wanga;
munda wanga wabwino uja
anawusandutsa chipululu.
11 Unawusandutsadi chipululu.
Ukanali wokhawokha chomwecho ukundilirira Ine.
Dziko lonse lasanduka chipululu
chifukwa palibe wolisamalira.
12 Anthu onse owononga abalalikira
ku zitunda zonse za mʼchipululu.
Yehova watuma ankhondo ake
kudzawatha kuyambira kumalire ena a dziko mpaka ku malire enanso a dziko,
ndipo palibe amene adzakhale pa mtendere.
13 Anthu anafesa tirigu koma anatuta minga;
anadzitopetsa kugwira ntchito koma osapeza phindu lililonse.
Choncho mudzachita manyazi ndi zokolola zanu
chifukwa cha mkwiyo wa Yehova.”
7 Chimaliziro cha zinthu zonse chili pafupi. Choncho khalani maso ndi odziletsa kuti muthe kupemphera. 8 Koposa zonse muzikondana wina ndi mnzake kwambiri, chifukwa chikondi chimaphimba machimo ambiri. 9 Muzisamalirana wina ndi mnzake osamanyinyirika. 10 Aliyense agwiritse ntchito mokhulupirika mphatso iliyonse imene anayilandira potumikira ena ngati adindo ogwiritsa bwino ntchito mphatso za Mulungu za mitundumitundu. 11 Ngati wina ayankhula, ayankhuledi mawu enieni a Mulungu. Ngati wina atumikira, atumikire ndi mphamvu imene Mulungu amapereka, kuti pa zonse Mulungu alemekezedwe mwa Yesu Khristu. Kwa Iye kukhale ulemerero ndi mphamvu mpaka muyaya, Ameni.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.