Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 74

Ndakatulo ya Asafu.

74 Nʼchifukwa chiyani mwatitaya ife kwamuyaya, Inu Mulungu?
    Chifukwa chiyani mkwiyo wanu ukutukutira pa nkhosa za busa lanu?
Kumbukirani anthu amene munawagula kalekale,
    fuko la cholowa chanu, limene Inu munaliwombola,
    phiri la Ziyoni, kumene inuyo mumakhala.
Tembenuzani mapazi kuloza ku mabwinja awa amuyaya
    chiwonongeko ichi chonse mdani wabweretsa pa malo opatulika.

Adani anu anabangula pa malo pamene Inu munkakumana nafe;
    anayimika mbendera zawo monga zizindikiro zachigonjetso.
Iwo anachita ngati anthu oti anyamula mbendera zawo
    kuti adule mitengo mʼnkhalango.
Kenaka anaphwanya ndi nkhwangwa ndi akasemasema awo
    zonse zimene tinapachika.
Iwo anatentha malo anu opatulika mpaka kuwagwetsa pansi;
    anadetsa malo okhalamo dzina lanu.
Ndipo anati mʼmitima yawo, “Tawatha kwathunthu.”
    Anatentha malo aliwonse amene Mulungu amapembedzedwerako mʼdzikomo.
Ife sitinapatsidwe chizindikiro chodabwitsa;
    palibe aneneri amene atsala
    ndipo palibe aliyense wa ife akudziwa kuti izi zidzatenga nthawi yayitali bwanji.

10 Kodi mpaka liti, mdani adzanyoze Inu Mulungu?
    Kodi amaliwongowa adzapeputsa dzina lanu kwamuyaya?
11 Chifukwa chiyani mukubweza dzanja lanu lamanja?
    Litulutseni kuchoka pachifuwa chanu ndipo muwawononge!

12 Koma Inu Mulungu, ndinu Mfumu yanga kuyambira kalekale;
    Mumabweretsa chipulumutso pa dziko lapansi.
13 Ndinu amene munagawa nyanja ndi mphamvu yanu;
    munathyola mitu ya zirombo za mʼmadzi.
14 Ndinu amene munaphwanya mitu ya Leviyatani
    ndi kuyipereka ngati chakudya cha zirombo za mʼchipululu.
15 Ndinu amene munatsekula akasupe ndi mitsinje,
    munawumitsa mitsinje imene siphwa nthawi zonse.
16 Masana ndi anu ndipo usiku ndi wanunso;
    Inuyo munakhazikitsa dzuwa ndi mwezi.
17 Ndinu amene munakhazikitsa malire onse a dziko lapansi;
    munakhazikitsa chilimwe ndi dzinja.

18 Kumbukirani momwe mdani wakunyozerani Inu Yehova,
    momwe anthu opusa apeputsira dzina lanu.
19 Musapereke moyo wa nkhunda yanu ku zirombo zakuthengo;
    nthawi zonse musayiwale miyoyo ya anthu anu osautsidwa.
20 Mukumbukire pangano lanu, pakuti malo obisika a mʼdziko
    asanduka mochitira zachiwawa zochuluka.
21 Musalole kuti osautsidwa abwerere mwamanyazi;
    osauka ndi osowa atamande dzina lanu.

22 Dzukani Inu Mulungu ndipo dzitetezeni pa mlandu;
    kumbukirani momwe opusa akukunyozerani tsiku lonse.
23 Musalekerere phokoso la otsutsana nanu,
    chiwawa cha adani anu, chimene chikumveka kosalekeza.

Yesaya 5:8-23

Tsoka ndi Chiweruzo

Tsoka kwa inu amene mumangokhalira kulumikiza nyumba,
    ndipo mumangokhalira kuwonjezera minda,
mpaka mutalanda malo onse
    kuti muzikhalamo nokha mʼdzikomo.

Yehova Wamphamvuzonse wayankhula ine ndikumva kuti,

“Ndithudi nyumba zambirizo zidzasanduka mabwinja,
    nyumba zazikulu zokongolazo zidzakhala zopanda anthu.
10 Munda wamphesa wa maekala khumi udzatulutsa vinyo wodzaza mbiya imodzi,
    kufesa madengu khumi a mbewu, zokolola zake zidzangodzaza dengu limodzi.”

11 Tsoka kwa iwo amene amadzuka mmamawa
    nathamangira chakumwa choledzeretsa,
amene amamwa mpaka usiku
    kufikira ataledzera kotheratu.
12 Pa maphwando awo pamakhala azeze, apangwe,
    matambolini, zitoliro ndi vinyo,
ndipo sasamala ntchito za Yehova,
    salemekeza ntchito za manja ake.
13 Motero anthu anga adzatengedwa ukapolo
    chifukwa cha kusamvetsa zinthu;
atsogoleri awo olemekezeka adzafa ndi njala,
    ndipo anthu wamba ochuluka adzafa ndi ludzu.
14 Nʼchifukwa chake ku manda sikukhuta
    ndipo kwayasama kwambiri kukamwa kwake;
mʼmandamo mudzagweranso anthu otchuka a mu Yerusalemu pamodzi ndi anthu wamba ochuluka;
    adzagweramo ali wowowo, nʼkuledzera kwawoko.
15 Ndipo munthu aliyense adzatsitsidwa,
    anthu onse adzachepetsedwa,
    anthu odzikuza adzachita manyazi.
16 Koma Yehova Wamphamvuzonse adzalemekezedwa chifukwa cha chiweruzo chake cholungama.
    Ndipo Mulungu woyera adzadzionetsa kuti ndi woyera pochita chilungamo chake.
17 Tsono nkhosa zidzadya pamenepo ngati pabusa pawo;
    ana ankhosa adzadya mʼmabwinja a anthu olemera.

18 Tsoka kwa amene amadzikokera tchimo ndi zingwe zachinyengo,
    ndipo amadzikokera zoyipa ndi zingwe zokokera ngolo,
19 amene amanena kuti, “Yehova afulumire,
    agwire ntchito yake mwamsanga
    kuti ntchitoyo tiyione.
Ntchito zionekere,
    zimene Woyerayo wa Israeli akufuna kuchita,
    zichitike kuti tizione.”

20 Tsoka kwa amene zoyipa amaziyesa zabwino
    ndipo zabwino amaziyesa zoyipa,
amene mdima amawuyesa kuwala
    ndipo kuwala amakuyesa mdima,
amene zowawasa amaziyesa zotsekemera
    ndipo zotsekemera amaziyesa zowawasa.

21 Tsoka kwa amene amadziona ngati anzeru
    ndipo amadziyesa ochenjera.

22 Tsoka kwa zidakwa zimene zimayika mtima pa vinyo
    ndipo ndi akatswiri posakaniza zakumwa,
23 amene amamasula olakwa chifukwa cha chiphuphu
    koma amayipitsa mlandu wa munthu wosalakwa.

1 Yohane 4:1-6

Kuyesa Mizimu

Anzanga okondedwa, musakhulupirire mzimu uliwonse, koma yesani mizimu ngati ikuchokera kwa Mulungu, chifukwa aneneri onama ambiri afalikira mʼdziko lapansi. Mungathe kuzindikira Mzimu wa Mulungu motere: Mzimu uliwonse umene umavomereza kuti Yesu Khristu anabwera mʼthupi, ndi wochokera kwa Mulungu, koma mzimu uliwonse umene suvomereza Yesu, siwochokera kwa Mulungu. Uwu ndi mzimu wa wokana Khristu umene munawumva kuti ukubwera ndipo ngakhale tsopano wabwera kale mʼdziko lapansi.

Inu ana okondedwa, ndinu ochokera kwa Mulungu ndipo mwawagonjetsa aneneri onyengawa, chifukwa Iye amene ali mwa inu ndi wamkulu kuposa amene ali mʼdziko lapansi. Aneneri onyengawa ndi ochokera mʼdziko lapansi, nʼchifukwa chake amayankhula za dziko lapansi, ndipo dziko lapansi limawamvera. Ife ndi ochokera kwa Mulungu, ndipo aliyense amene amadziwa Mulungu amamvera zimene timayankhula. Koma aliyense amene sachokera kwa Mulungu samvera zimene timayankhula. Mmenemu ndiye mmene timasiyanitsira pakati pa mzimu wachoonadi ndi Mzimu wachinyengo.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.