Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 80:1-2

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Salimo la Asafu.

80 Tcherani khutu Inu mʼbusa wa Israeli,
    Inu amene mumatsogolera Yosefe monga nkhosa;
Inu amene mumakhala pa mpando waufumu pakati pa akerubi, walani
    kwa Efereimu, Benjamini ndi Manase.
Utsani mphamvu yanu;
    bwerani ndi kutipulumutsa.

Masalimo 80:8-19

Munatulutsa mpesa kuchoka ku Igupto;
    munathamangitsa anthu a mitundu ina ndi kuwudzala mpesawo.
Munawulimira munda wamphesawo,
    ndipo unamera ndi kudzaza dziko.
10 Mapiri anaphimbidwa ndi mthunzi wake,
    mikungudza yamphamvu ndi nthambi zake.
11 Unatambalitsa nthambi zake mpaka ku nyanja,
    mphukira zake mpaka ku mtsinje.

12 Chifukwa chiyani mwagwetsa makoma ake
    kuti onse amene akudutsa athyole mphesa zake?
13 Nguluwe zochokera mʼnkhalango zikuwononga
    ndipo zirombo za mthengo zimawudya.
14 Bweraninso kwa ife Inu Mulungu Wamphamvuzonse!
    Yangʼanani pansi muli kumwambako ndipo muone!
Uyangʼanireni mpesa umenewu,
15     muzu umene dzanja lanu lamanja ladzala,
    mwana amene inu munamukuza nokha.

16 Mpesa wanu wadulidwa ndi kutenthedwa ndi moto;
    pakudzudzula kwanu anthu anu awonongeka.
17 Dzanja lanu likhale pa munthu amene ali ku dzanja lanu lamanja,
    mwana wa munthu amene mwalera nokha.
18 Ndipo ife sitidzatembenukira kumbali kuchoka kwa Inu;
    titsitsimutseni ndipo tidzayitana pa dzina lanu.

19 Tibwezereni mwakale Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse
    nkhope yanu itiwalire
    kuti tipulumutsidwe.

Yesaya 3:1-17

Chiweruzo pa Yerusalemu ndi Yuda

Taonani tsopano, Ambuye
    Yehova Wamphamvuzonse,
ali pafupi kuchotsa mu Yerusalemu ndi mu Yuda
    zinthu pamodzi ndi thandizo;
adzachotsa chakudya chonse ndi madzi onse,
    anthu amphamvu ndi asilikali ankhondo,
oweruza ndi aneneri,
    anthu olosera ndi akuluakulu,
atsogoleri a ankhondo makumi asanu ndi anthu olemekezeka,
    aphungu ndi anthu amatsenga ndi akatswiri pa za kulosera.

Ndidzawayikira anyamata kuti akhale mafumu awo;
    ana akhanda ndiwo adzawalamulire.
Anthu adzazunzana,
    munthu ndi munthu mnzake, mnansi ndi mnansi wake.
Anthu wamba adzanyoza
    akuluakulu.

Munthu adzagwira mʼbale wake
    mʼnyumba ya abambo awo, ndipo adzati,
“Iwe uli nawo mwinjiro, ndiye ukhale mtsogoleri wathu;
    lamulira malo opasuka ano!”
Koma tsiku limenelo mʼbale wakeyo adzafuwula kuti,
    “Ayi, mavuto oterewa ndilibe mankhwala ake.
Ndilibe chakudya kapena chovala mʼnyumba mwanga;
    musasankhe ine kukhala mtsogoleri wa anthu.”

Yerusalemu akudzandira,
    Yuda akugwa;
zokamba zawo ndi ntchito zawo nʼzotsutsana ndi Yehova,
    sakulabadira ulemerero wa Mulungu.
Maonekedwe a nkhope zawo amawatsutsa;
    amaonetsera poyera tchimo lawo ngati Sodomu;
    salibisa tchimo lawolo.
Tsoka kwa iwo
    odziputira okha mavuto.

10 Nena kwa olungama kuti zonse zidzawayendera bwino,
    pakuti adzakondwera ndi phindu la ntchito zawo.
11 Tsoka kwa anthu oyipa! Mavuto ali pa iwo!
Adzalandira malipiro a zimene manja awo anachita.

12 Achinyamata akupondereza anthu anga,
    ndipo amene akuwalamulira ndi akazi.
Aa, anthu anga, atsogoleri anu akukusocheretsani;
    akukuchotsani pa njira yanu.

13 Yehova wakhala pamalo pake mʼbwalo la milandu;
    wakonzeka kuti aweruze anthu ake.
14 Yehova akuwazenga milandu
    akuluakulu ndi atsogoleri a anthu ake:
“Ndinu amene mwawononga munda wanga wa mpesa;
    nyumba zanu zadzaza ndi zolanda kwa amphawi.
15 Nʼchifukwa chiyani inu mukupsinja anthu anga,
    nʼkudyera masuku pamutu amphawi?”
            Akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.

16 Yehova akunena kuti,
    “Akazi a ku Ziyoni ngodzikuza kwambiri,
akuyenda atakweza makosi awo,
    akukopa amuna ndi maso awo
akuyenda monyangʼama
    akuliza zigwinjiri za mʼmiyendo yawo
17 Nʼchifukwa chake Ambuye, adzatulutsa zipere pa mitu ya akazi a ku Ziyoniwo;
    Yehova adzachititsa dazi mitu yawo.”

Ahebri 10:32-39

32 Kumbukirani masiku akale aja mutangowunikiridwa chatsopano, pa nthawi imeneyi munapirira zowawa zambiri. 33 Nthawi zina ankakunyozani pagulu ndi kukuzunzani. Nthawi zina munkamva zowawa pamodzi ndi amene ankasautsidwa chotere. 34 Munkawamvera chisoni amene anali mʼndende ndiponso munkalola mokondwera kuti akulandeni katundu wanu chifukwa munkadziwa kuti muli nacho chuma choposa ndi chosatha.

35 Tsono musataye kulimbika mtima kwanuko pakuti mudzalandira nako mphotho yayikulu. 36 Nʼkofunika kuti mupirire kuti pamene muchita chifuniro cha Mulungu mudzalandire zimene Iye analonjeza. 37 Pakuti nʼkanthawi kochepa chabe,

Iye amene akubwera adzabwera ndipo sadzachedwa ayi.
38 Koma wolungama wangayo adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.
    Ndipo ngati iye abwerera mʼmbuyo chifukwa cha mantha,
    Ine sindidzakondwera naye.

39 Koma ife sindife amodzi a iwo obwerera mʼmbuyo mwa mantha ndi owonongedwa, koma ndife amodzi a amene akukhulupirira ndi wopulumutsidwa.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.