Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Salimo la Asafu.
80 Tcherani khutu Inu mʼbusa wa Israeli,
Inu amene mumatsogolera Yosefe monga nkhosa;
Inu amene mumakhala pa mpando waufumu pakati pa akerubi, walani
2 kwa Efereimu, Benjamini ndi Manase.
Utsani mphamvu yanu;
bwerani ndi kutipulumutsa.
8 Munatulutsa mpesa kuchoka ku Igupto;
munathamangitsa anthu a mitundu ina ndi kuwudzala mpesawo.
9 Munawulimira munda wamphesawo,
ndipo unamera ndi kudzaza dziko.
10 Mapiri anaphimbidwa ndi mthunzi wake,
mikungudza yamphamvu ndi nthambi zake.
11 Unatambalitsa nthambi zake mpaka ku nyanja,
mphukira zake mpaka ku mtsinje.
12 Chifukwa chiyani mwagwetsa makoma ake
kuti onse amene akudutsa athyole mphesa zake?
13 Nguluwe zochokera mʼnkhalango zikuwononga
ndipo zirombo za mthengo zimawudya.
14 Bweraninso kwa ife Inu Mulungu Wamphamvuzonse!
Yangʼanani pansi muli kumwambako ndipo muone!
Uyangʼanireni mpesa umenewu,
15 muzu umene dzanja lanu lamanja ladzala,
mwana amene inu munamukuza nokha.
16 Mpesa wanu wadulidwa ndi kutenthedwa ndi moto;
pakudzudzula kwanu anthu anu awonongeka.
17 Dzanja lanu likhale pa munthu amene ali ku dzanja lanu lamanja,
mwana wa munthu amene mwalera nokha.
18 Ndipo ife sitidzatembenukira kumbali kuchoka kwa Inu;
titsitsimutseni ndipo tidzayitana pa dzina lanu.
19 Tibwezereni mwakale Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse
nkhope yanu itiwalire
kuti tipulumutsidwe.
5 Inu nyumba ya Yakobo, bwerani,
tiyeni tiyende mʼkuwala kwa Yehova.
Tsiku la Yehova
6 Inu Yehova mwawakana anthu anu,
nyumba ya Yakobo.
Iwo adzaza ndi zamatsenga zochokera Kummawa;
amawombeza mawula ngati Afilisti,
ndipo amayanjana ndi anthu osapembedza Mulungu.
7 Dziko lawo ndi lodzaza ndi siliva ndi golide;
ndipo chuma chawo ndi chosatha.
Dziko lawo ndi lodzaza ndi akavalo;
ndipo magaleta awo ankhondo ngosawerengeka.
8 Dziko lawo ndi lodzaza ndi mafano;
iwo amapembedza ntchito ya manja awo,
amagwadira zomwe anapanga ndi zala zawo.
9 Tsono munthu aliyense adzachepetsedwa
ndi kutsitsidwa.
Inu Yehova musawakhululukire.
10 Lowani mʼmatanthwe,
bisalani mʼmaenje,
kuthawa kuopsa kwa Yehova
ndi ulemerero wa ufumu wake!
11 Kudzikuza kwa anthu kudzatha,
ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa;
Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu pa tsiku limenelo.
26 Ngati ife tipitirira kuchimwa mwadala pamene tikudziwa choona, palibenso nsembe ina imene ingaperekedwe chifukwa cha machimo athuwo. 27 Koma kumangodikira kokha ndi mantha chiweruzo ndiponso moto woopsa umene udzawononga adani a Mulungu 28 Aliyense amene amakana malamulo a Mose amaphedwa popanda nʼchifundo chomwe, malingana pali mboni ziwiri kapena zitatu. 29 Koposa kotani nanga ululu wachilango chimene adzalandire munthu amene amapeputsa Mwana wa Mulungu, amene amayesa magazi a pangano, amene anamuyeretsa, kukhala chinthu chodetsedwa, ndi kunyoza Mzimu wachisomo? 30 Pakuti timadziwa amene anati, “Kubwezera chilango nʼkwanga; ndidzawalanga ndine.” Iye anatinso, “Ambuye adzaweruza anthu ake.” 31 Nʼchinthu choopsa kugwa mʼmanja a Mulungu wamoyo.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.