Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Salimo la Asafu.
50 Wamphamvuyo, Yehova Mulungu,
akuyankhula ndi kuyitanitsa dziko lapansi
kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.
2 Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri
Mulungu akuwala.
3 Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete;
moto ukunyeketsa patsogolo pake,
ndipo pomuzungulira pali mphepo yamkuntho
4 Iye akuyitanitsa zamumlengalenga
ndi za pa dziko lapansi kuti aweruze anthu ake.
5 Mundisonkhanitsire okhulupirika anga,
amene anachita pangano ndi ine pochita nsembe.
6 Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake,
pakuti Mulungu mwini ndi woweruza.
7 Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula,
iwe Israeli, ndipo Ine ndidzayankhula mokutsutsa;
ndine Mulungu, Mulungu wako.
8 Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako,
kapena nsembe zako zopsereza zimene zili pamaso panga nthawi zonse.
22 “Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu
kuti ndingakukadzule popanda wokupulumutsa:
23 Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza,
ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse
chipulumutso cha Mulungu.”
Anthu Owukira
2 Tamverani, miyamba inu! Tchera khutu, iwe dziko lapansi!
Pakuti Yehova wanena kuti,
“Ndinabala ana ndi kuwalera,
koma anawo andiwukira Ine.
3 Ngʼombe imadziwa mwini wake,
bulu amadziwa kumene kuli gome la mbuye wake,
koma Israeli sadziwa,
anthu anga samvetsa konse.”
4 Haa, mtundu wochimwa,
anthu olemedwa ndi machimo,
obadwa kwa anthu ochita zoyipa,
ana odzipereka ku zoyipa!
Iwo asiya Yehova;
anyoza Woyerayo wa Israeli
ndipo afulatira Iyeyo.
5 Chifukwa chiyani mukufuna kuti muzingolangidwabe?
Chifukwa chiyani mukupitirira kukhala mʼmoyo wowukira?
Mutu wanu wonse uli ndi mabala,
mtima wanu wonse wafowokeratu.
6 Kuchokera ku phazi mpaka ku mutu
palibe pabwino,
paliponse pali mikwingwirima ndi zilonda,
mabala ali magazi chuchuchu,
mabala ake ngosatsuka, ngosamanga
ndiponso ngosapaka mafuta ofewetsa.
7 Dziko lanu lasanduka bwinja,
mizinda yanu yatenthedwa ndi moto;
minda yanu ikukololedwa ndi alendo
inu muli pomwepo,
dziko lanu lasanduka bwinja monga ngati lagonjetsedwa ndi alendo.
8 Mwana wamkazi wa Ziyoni watsala yekha
ngati nsanja mʼmunda wampesa,
ngati chisimba mʼmunda wa minkhaka,
ngati mzinda wozingidwa ndi nkhondo.
9 Yehova Wamphamvuzonse akanapanda
kutisiyira opulumuka,
tikanawonongeka ngati Sodomu,
tikanakhala ngati anthu a ku Gomora.
21 Taonani momwe mzinda wokhulupirika
wasandukira wadama!
Mzinda umene kale unali wodzaza ndi chiweruzo cholungama;
mu mzindamo munali chilungamo,
koma tsopano muli anthu opha anzawo!
22 Siliva wako wasanduka wachabechabe,
vinyo wako wabwino wasungunulidwa ndi madzi.
23 Atsogoleri ako ndi owukira,
anthu ogwirizana ndi mbala;
onse amakonda ziphuphu
ndipo amathamangira mphatso.
Iwo sateteza ana amasiye;
ndipo samvera madandawulo a akazi amasiye.
Za Chuma cha Kumwamba
19 “Musadziwunjikire chuma pa dziko lapansi, pamene njenjete ndi dzimbiri zimawononga ndi pamene mbala zimathyola ndi kuba. 20 Koma mudziwunjikire chuma kumwamba kumene njenjete ndi dzimbiri siziwononga ndipo mbala sizithyola ndi kuba. 21 Pakuti kumene kuli chuma chako, mtima wako udzakhala komweko.
Diso Nyale ya Thupi
22 “Diso ndi nyale ya thupi. Ngati maso ako ali bwino, thupi lako lonse lidzakhala mʼkuwala. 23 Koma ngati maso ako sali bwino, thupi lako lonse lidzakhala mu mdima. Koma ngati kuwala kuli mwa iwe ndi mdima, ndiye kuti mdimawo ndi waukulu bwanji!
24 “Palibe munthu angathe kukhala kapolo wa ambuye awiri. Pakuti pena adzamuda mmodzi ndi kukonda winayo kapena adzagwira ntchito mokhulupirika kwa mmodzi, nadzanyoza winayo. Simungathe kukhala kapolo wa Mulungu ndi wa chuma pa nthawi imodzi.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.