Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere.
60 Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza.
Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!
2 Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba,
konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.
3 Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto;
inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.
4 Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera
kuti tisonkhanireko pothawa uta.
5 Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja,
kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
6 Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika:
“Mwakupambana ndidzagawa Sekemu
ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.
7 Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso;
Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera,
Yuda ndi ndodo yanga yaufumu
8 Mowabu ndi mbale yanga yosambira,
pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga,
pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”
9 Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa?
Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
10 Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife
ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.
11 Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu,
pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.
12 Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano
ndipo tidzapondaponda adani athu.
Mkwiyo wa Yehova pa Israeli
13 Kale Efereimu ankati akayankhula, anthu ankanjenjemera;
anali wolemekezeka mu Israeli.
Koma analakwa popembedza Baala, motero anafa.
2 Tsopano akunka nachimwirachimwirabe;
akudzipangira mafano pogwiritsa ntchito siliva wawo,
zifanizo zopangidwa mwaluso,
zonsezo zopangidwa ndi amisiri.
Amanena za anthu awa kuti,
“Amatenga munthu ndi kumupereka nsembe
ndipo amapsompsona fano la mwana wangʼombe.”
3 Choncho adzakhala ngati nkhungu yammawa,
ngati mame amene amakamuka msanga,
ngati mungu wowuluka kuchokera pa malo opunthira tirigu,
ngati utsi umene ukutulukira pa zenera.
4 Koma Ine ndine Yehova Mulungu wanu,
amene ndinakutulutsani mu Igupto.
Simuyenera kudziwa Mulungu wina, koma Ine ndekha,
palibe Mpulumutsi wina kupatula Ine.
5 Ndinakusamalira mʼchipululu,
mʼdziko lotentha kwambiri.
6 Pamene ndinawadyetsa, iwo anakhuta;
iwo atakhuta anayamba kunyada;
ndipo anandiyiwala Ine.
7 Motero ndidzawalumphira ngati mkango,
ndidzawabisalira mu msewu ngati kambuku.
8 Ngati chimbalangondo cholandidwa ana ake,
ndidzawambwandira ndi kuwathyolathyola.
Ndidzawapwepweta ngati mkango;
chirombo chakuthengo chidzawakhadzula.
9 “Iwe Israeli, wawonongedwa,
chifukwa ukutsutsana ndi Ine, ukutsutsana ndi mthandizi wako.
10 Kodi mfumu yako ili kuti, kuti ikupulumutse?
Olamulira ako a mʼmizinda yonse ali kuti,
amene iwe unanena za iwo kuti,
‘Patseni mfumu ndi akalonga?’
11 Choncho Ine ndinakupatsani mfumu mwachipseramtima,
ndipo ndinayichotsa mwaukali.
12 Kulakwa kwa Efereimu kwasungidwa,
machimo ake alembedwa mʼbuku.
13 Zowawa zonga za mayi pa nthawi yobala mwana zamugwera,
koma iye ndi mwana wopanda nzeru,
pamene nthawi yake yobadwa yafika
iyeyo safuna kutuluka mʼmimba mwa amayi ake.
14 “Ndidzawapulumutsa ku mphamvu ya manda;
ndidzawawombola ku imfa.
Kodi iwe imfa, miliri yako ili kuti?
Kodi iwe manda, kuwononga kwako kuli kuti?
“Sindidzachitanso chifundo,
15 ngakhale Efereimu akondwe pakati pa abale ake,
mphepo ya kummawa yochokera kwa Yehova idzabwera,
ikuwomba kuchokera ku chipululu.
Kasupe wake adzaphwa
ndipo chitsime chake chidzawuma.
Chuma chake chonse chamtengowapatali
chidzafunkhidwa ndipo chidzatengedwa.
16 Anthu a ku Samariya adzalangidwa chifukwa cha zolakwa zawo,
chifukwa anawukira Mulungu wawo.
Adzaphedwa ndi lupanga;
ana awo adzaphedwa mowamenyetsa pansi,
akazi awo oyembekezera adzatumbulidwa pa mimba.”
Malangizo Ena
2 Pempherani modzipereka, mukhale atcheru ndiponso oyamika. 3 Ndipo muzitipemphereranso ife kuti Mulungu atitsekulire khomo la uthenga wathu, kuti tilalikire chinsinsi cha Khristu, chimene ndine womangidwa nacho mʼndende. 4 Pempherani kuti ndilalikire momveka bwino, monga ndikuyenera. 5 Mayendedwe anu pakati pa akunja, akhale anzeru ndipo mugwiritse ntchito mpata uliwonse umene muli nawo. 6 Mayankhulidwe anu nthawi zonse akhale odzaza ndi chisomo ndi okoma, kuti mudziwe kuyankha aliyense.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.