Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 85

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora.

85 Yehova munakomera mtima dziko lanu;
    munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo.
Munakhululukira mphulupulu za anthu anu
    ndi kuphimba machimo awo onse.
            Sela
Munayika pambali ukali wanu wonse
    ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa.

Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu,
    ndipo mutichotsere mkwiyo wanu.
Kodi mudzatikwiyira mpaka liti?
    Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse?
Kodi simudzatitsitsimutsanso,
    kuti anthu anu asangalale mwa Inu?
Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova,
    ndipo tipatseni chipulumutso chanu.

Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena;
    Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake,
    koma musawalole kuti abwerere ku zopusa.
Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye,
    kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu.

10 Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi;
    chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana.
11 Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi,
    ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba.
12 Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino,
    ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.
13 Wolungama amapita patsogolo pake
    ndi kukonza njira za mapazi ake.

Hoseya 4

Yehova Ayimba Mlandu Israeli

Inu Aisraeli, imvani mawu a Yehova,
    chifukwa Yehova ali ndi mlandu ndi inu
    amene mumakhala mʼdzikoli:
“Mʼdziko mwanu mulibe kukhulupirika, mulibe chikondi
    mulibe kulabadira za Mulungu.
Muli kutemberera kokha, kunama ndi kupha.
    Kuba ndi kuchita chigololo;
machimo achita kunyanya
    ndipo akungokhalira kuphana.
Chifukwa chake dziko likulira
    ndipo onse amene amakhalamo akuvutika;
zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga
    ndiponso nsomba zamʼnyanja zikufa.

“Koma wina asapeze mnzake chifukwa,
    wina aliyense asayimbe mlandu mnzake,
pakuti anthu ako ali ngati anthu
    amene amayimba mlandu wansembe.
Mumapunthwa usana ndi usiku
    ndipo aneneri amapunthwa nanu pamodzi.
Choncho ndidzawononga amayi anu.
    Anthu anga akuwonongeka chifukwa chosadziwa.

“Pakuti mwakana kudziwa,
    Inenso ndidzakukanani monga ansembe anga;
chifukwa mwayiwala lamulo la Mulungu wanu,
    Inenso ndidzayiwala ana anu.
Ansembe ankati akachuluka
    iwo ankandichimwiranso kwambiri;
    iwo anasinthanitsa ulemerero wawo ndi chinthu china chonyansa.
Amalemererapo pa machimo a anthu anga
    ndipo amafunitsitsa kuti anthuwo azipitiriza kuchimwa.
Ndipo zidzakhala motere: zochitikira anthu ena, zidzachitikiranso ansembe.
    Ndidzawalanga onsewo chifukwa cha njira zawo,
    ndidzawabwezera chifukwa cha machitidwe awo.

10 “Iwo azidzadya koma sadzakhuta;
    azidzachita zachiwerewere koma sadzachulukana,
chifukwa anasiya Yehova
kuti adzipereke 11     ku zachiwerewere,
ku vinyo wakale ndi watsopano,
    zimene zimachotsa nzeru zomvetsa zinthu
12 za anthu anga.
Anthu anga amapempha nzeru ku fano lamtengo
    ndipo ndodo yawo yamtengo imawayankha.
Mzimu wachiwerewere umawasocheretsa;
    iwo sakukhulupirika kwa Mulungu wawo.
13 Amapereka nsembe pamwamba pa mapiri
    ndi kufukiza lubani pa zitunda,
pa tsinde pa mtengo wa thundu, mnjale ndi mkundi,
    pamene pali mthunzi wabwino.
Nʼchifukwa chake ana anu aakazi akuchita zachiwerewere
    ndipo akazi a ana anu akuchita zigololo.

14 “Ine sindidzalanga ana anu aakazi
    pamene iwo adzachita zachiwerewere,
kapena akazi a ana anu
    pamene adzachita zigololo.
Paja inu nomwe amunanu mumayenda ndi akazi achiwerewere,
    ndipo mumapereka nsembe pamodzi ndi akazi achiwerewere a ku malo opembedzerako.
    Anthu amene alibe nzeru adzawonongeka ndithu!

15 “Ngakhale umachita chigololo, iwe Israeli,
    Yuda asapezeke ndi mlandu wotere.

“Usapite ku Giligala.
    Usapite ku Beti-Aveni.
    Ndipo usalumbire kuti, ‘Pali Yehova wamoyo!’
16 Aisraeli ndi nkhutukumve,
    ngosamva ngati ana angʼombe.
Kodi Yehova angathe kuwaweta bwanji
    ngati ana ankhosa pa msipu wabwino?
17 Efereimu waphathana ndi mafano;
    mulekeni!
18 Ngakhale pamene zakumwa zawo zatha,
    amapitiriza kuchita zachiwerewere;
    atsogoleri awo amakonda kwambiri njira zawo zochititsa manyazi.
19 Adzachotsedwa ndi kamvuluvulu
    ndipo adzachita manyazi chifukwa cha nsembe zawo.

Machitidwe a Atumwi 1:15-20

15 Pa nthawi imeneyo Petro anayimirira pakati pa okhulupirira (gulu la anthu pafupifupi 120). 16 Iye anati, “Abale anga, Malemba anayenera kukwaniritsidwa omwe Mzimu Woyera anayankhula kalekale kudzera mwa Davide za Yudasi, amene anatsogolera amene anamugwira Yesu. 17 Iye anali mmodzi wa gulu lathu ndipo anatumikira pamodzi ndi ife.”

18 (Yudasi anagula munda ndi ndalama zimene anazipeza pochita zoyipa zija; kumeneko, iye anagwa chamutu, naphulika pakati ndipo matumbo ake wonse anakhuthuka. 19 Aliyense mu Yerusalemu anamva zimenezi, kotero anatcha mundawo mʼchiyankhulo chawo kuti Akeledama, kutanthauza, Munda wa Magazi).

20 Petro anati, “Pakuti kwalembedwa mʼbuku la Masalimo kuti,

“Nyumba yake isanduke bwinja,
    ndipo pasakhale wogonamo.

Ndiponso,

“Wina atenge ntchito yake yautsogoleri.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.