Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Gimeli
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo;
kuti tsono ndisunge mawu anu.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona
zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi;
musandibisire malamulo anu.
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka
malamulo anu nthawi zonse.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa,
amene achoka pa malamulo anu.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo
pakuti ndimasunga malamulo anu.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza,
mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
24 Malamulo anu amandikondweretsa;
ndiwo amene amandilangiza.
Daleti
25 Moyo wanga wakangamira fumbi;
tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha;
phunzitseni malamulo anu.
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu;
pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni;
limbikitseni monga mwa mawu anu.
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo;
mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
30 Ndasankha njira ya choonadi;
ndayika malamulo anu pa mtima panga.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova;
musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu,
pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
13 “Tsiku limenelo
“anamwali okongola ndi anyamata amphamvu
adzakomoka ndi ludzu.
14 Onse amene amalumbira pa tchimo la Samariya,
kapena kumanena kuti, ‘Iwe Dani, pali mulungu wako wamoyo,’
kapena, ‘Pali mulungu wamoyo wa ku Beeriseba.’
Iwowo adzagwa
ndipo sadzadzukanso.”
Israeli Adzawonongedwa
9 Ine ndinaona Ambuye atayima pambali pa guwa lansembe, ndipo anati:
“Kantha mitu ya nsanamira
kuti ziwundo za nyumba zigwedezeke.
Muzigwetsere pa mitu ya anthu onse,
onse amene atsalira ndidzawapha ndi lupanga.
Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzathawe,
palibe amene adzapulumuke.
2 Ngakhale atakumba pansi mpaka ku malo a anthu akufa,
dzanja langa lidzawatulutsa kumeneko.
Ngakhale atakwera kumwamba
Ine ndidzawatsakamutsa kumeneko.
3 Ngakhale atakabisala pamwamba pa phiri la Karimeli,
Ine ndidzawasaka kumeneko ndi kuwagwira.
Ngakhale atakabisala pansi pa nyanja yayikulu,
ndidzalamula njoka kuti iwalume kumeneko.
4 Ngakhale adani awo awakusire ku ukapolo,
ndidzalamula lupanga kuti liwaphe kumeneko.
Ndidzawayangʼanitsitsa
kuti zoyipa ziwagwere; osati zabwino.”
2 Inu Ana anga okondedwa, ndikukulemberani zimenezi kuti musachimwe. Koma wina akachimwa, tili nayo Nkhoswe yotinenera kwa Atate, Yesu Khristu, Wolungamayo. 2 Iyeyo ndiye nsembe yopepesera machimo athu, ndipo osati athu okha, komanso machimo onse a dziko lapansi.
Chikondi ndi Chidani
3 Ife timatsimikiza kuti tikumudziwa ngati tikusunga malamulo ake. 4 Munthu akamanena kuti, “Ine ndimadziwa Mulungu,” koma samvera malamulo a Mulunguyo, ndi wabodza ameneyo ndipo mwa iye mulibe choonadi. 5 Koma munthu aliyense akamvera mawu ake, ndiye kuti chikondi cha Mulungu chafikadi penipeni mwa iyeyo. Pamenepo timatsimikizadi kuti tili mwa Iye. 6 Aliyense amene amati amakhala mwa Mulungu, ayenera kukhala moyo umene Yesu ankakhala.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.