Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 52

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, ndakatulo ya Davide; pamene Doegi Mwedomu anapita kwa Sauli ndi kunena kuti “Davide wapita ku nyumba ya Ahimeleki.”

52 Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira ndi zoyipa, iwe munthu wamphamvu?
    Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira tsiku lonse,
    iwe munthu wochititsa manyazi pamaso pa Mulungu?
Tsiku lonse umakhalira kuganizira za kuwononga ena;
    lilime lako lili ngati lumo lakuthwa,
    ntchito yako nʼkunyenga.
Iwe umakonda choyipa mʼmalo mwa kuyankhula choonadi.
    Umakonda kunama kupambana kuyankhula zoona.
            Sela
Umakonda mawu onse opweteka,
    iwe lilime lachinyengo!

Zoonadi Mulungu adzakutsitsa kupita ku chiwonongeko chamuyaya:
    iye adzakukwatula ndi kukuchotsa mʼtenti yako;
    iye adzakuzula kuchoka mʼdziko la amoyo.
Olungama adzaona zimenezi ndi kuchita mantha;
    adzamuseka nʼkumanena kuti,
“Pano tsopano pali munthu
    amene sanayese Mulungu linga lake,
koma anakhulupirira chuma chake chambiri
    nalimbika kuchita zoyipa!”

Koma ine ndili ngati mtengo wa olivi
    wobiriwira bwino mʼnyumba ya Mulungu;
ndimadalira chikondi chosatha cha Mulungu
    kwa nthawi za nthawi.
Ine ndidzakutamandani kwamuyaya chifukwa cha zimene mwachita;
    chifukwa cha zimene mwachita; mʼdzina lanu ndidzayembekezera
    pakuti dzina lanulo ndi labwino. Ndidzakutamandani pamaso pa oyera mtima anu.

Amosi 6

Tsoka kwa Osalabadira Kanthu

Tsoka kwa amene simukulabadira kanthu ku Ziyoni,
    ndiponso kwa inu amene mukukhala mwamtendere pa Phiri la Samariya,
inu anthu otchuka ochokera ku mtundu wa anthu omveka,
    kumene Aisraeli amafikako!
Pitani ku mzinda wa Kaline mukawuyangʼane;
    mukapitenso ku Hamati-raba mzinda waukulu uja,
    ndipo mukatsikirenso ku Gati kwa Afilisti.
Kodi mizinda imeneyi ndi yopambana maufumu anu awiriwa?
    Kodi dziko lawo ndi lalikulu kupambana lanu?
Inu simulabadirako kuti tsiku loyipa lidzafika,
    zochita zanu zimafulumizitsa ulamuliro wankhanza.
Mumagona pa mabedi owakongoletsa ndi minyanga ya njovu,
    mumagona pa mipando yanu ya wofuwofu.
Mumadya ana ankhosa onona
    ndi ana angʼombe onenepa.
Mumayimba azeze anu ndi kumangopeka
    nyimbo pa zingʼwenyengʼwenye ngati Davide.
Mumamwera vinyo mʼzipanda zodzaza
    ndipo mumadzola mafuta abwino kwambiri,
    koma simumva chisoni ndi kuwonongeka kwa Yosefe.
Nʼchifukwa chake inu mudzakhala mʼgulu la anthu oyamba kupita ku ukapolo;
    maphwando ndi zikondwerero zanu zidzatheratu.

Yehova Amanyansidwa ndi Kunyada kwa Israeli

Ambuye Yehova walumbira mʼdzina lake. Yehova Mulungu Wamphamvuzonse walengeza kuti,

“Ndimanyansidwa ndi kunyada kwa Yakobo,
    ndimadana ndi nyumba zake zaufumu;
Ine ndidzawupereka mzindawu
    pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo.”

Ngati anthu khumi otsala adzabisala mʼnyumba imodzi, nawonso adzafa ndithu. 10 Ndipo ngati mʼbale wake wa wina wakufayo, woyenera kusamala za maliro, adzafika kudzatulutsa mitembo mʼnyumbamo nʼkufunsa aliyense amene akubisalabe mʼnyumbamo kuti, “Kodi uli ndi wina wamoyo mʼmenemo?” Ndipo munthu wobisalayo ndi kuyankha kuti, “Ayi,” mʼbaleyo adzanena kuti, “Khala chete! Ife tisayerekeze kutchula dzina la Yehova.”

11 Pakuti Yehova walamula kuti
    nyumba zikuluzikulu Iye adzazigamulagamula,
    ndipo nyumba zazingʼono zidzasanduka maduka okhaokha.

12 Kodi akavalo amathamanga pa thanthwe?
    Kodi wina amatipula ndi ngʼombe mʼnyanja?
Koma chiweruzo cholungama mwachisandutsa kukhala zinthu zakupha
    ndipo chipatso cha chilungamo mwachisandutsa kukhala chowawa.
13 Inu amene mukunyadira kuti munagonjetsa Lo Debara
    ndipo mukunena kuti, “Kodi sitinatenge Karinaimu ndi mphamvu zathu zokha?”

14 Koma Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akulengeza kuti,
    “Inu nyumba ya Israeli, ndidzakudzutsirani mtundu wina wa anthu
umene udzakuzunzani
    kuchokera ku Lebo Hamati mpaka ku Chigwa cha Araba.”

Luka 8:4-10

Anthu ambiri ankasonkhana, ndipo pamene anthu ankabwera kwa Yesu kuchokera ku midzi, Iye anawawuza fanizo ili, “Mlimi anapita kukafesa mbewu zake. Akufesa mbewuzo, zina zinagwa mʼmbali mwa njira; zinapondedwa, ndipo mbalame zamlengalenga zinadya. Zina zinagwa pa thanthwe, ndipo pamene zinamera, zinafota chifukwa panalibe chinyezi. Mbewu zina zinagwera pakati pa minga, zinakulira pamodzi ndi mingazo ndipo zinalepheretsa mmerawo kukula. Mbewu zina zinagwera pa nthaka yabwino. Zinamera ndipo zinabala mowirikiza 100 kuposa zimene zinafesedwa zija.”

Atanena izi, anafuwula kuti, “Amene ali ndi makutu, amve.”

Ophunzira ake anamufunsa tanthauzo lake la fanizolo. 10 Iye anati, “Kudziwa zinsinsi za ufumu wa Mulungu kwapatsidwa kwa inu, koma kwa ena ndimawayankhula mʼmafanizo kuti,

“ngakhale akuona, asapenye;
    ngakhale akumva, asazindikire.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.