Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 7

Sigioni wa Davide, amene anayimbira Yehova zokhudza Kusi, wa fuko la Benjamini.

Inu Yehova Mulungu wanga, Ine ndikuthawira kwa Inu;
    pulumutseni ndi kundilanditsa kwa onse amene akundithamangitsa,
mwina angandikadzule ngati mkango,
    ndi kundingʼamba popanda wondipulumutsa.

Inu Yehova Mulungu wanga,
    ngati ndachita izi ndipo ndapezeka wolakwa,
ngati ndachita zoyipa kwa iye amene ndili naye pa mtendere,
    kapena popanda chifukwa ndalanda mdani wanga,
pamenepo lolani adani anga andithamangitse ndi kundipitirira,
    lolani kuti moyo wanga aupondereze pansi
    ndipo mundigoneke pa fumbi.
            Sela

Nyamukani Yehova, mu mkwiyo wanu;
    nyamukani kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga.
    Dzukani Mulungu wanga, lamulirani chilungamo chanu.
Lolani gulu la anthu a mitundu ina lisonkhane mokuzungulirani.
    Alamulireni muli kumwambako;
    Yehova aweruzeni anthu a mitundu inayo.
Ndiweruzeni Yehova, monga mwa chilungamo changa,
    monga mwa moyo wanga wangwiro, Inu Wammwambamwamba.
Inu Mulungu wolungama,
    amene mumasanthula maganizo ndi mitima,
thetsani chiwawa cha anthu oyipa
    ndipo wolungama akhale motetezedwa.

10 Chishango changa ndi Mulungu Wammwambamwamba,
    amene amapulumutsa olungama mtima.
11 Mulungu amaweruza molungama,
    Mulungu amene amaonetsa ukali wake tsiku ndi tsiku.
12 Ngati munthu satembenuka,
    Mulungu adzanola lupanga lake,
    Iye adzawerama ndi kukoka uta.
13 Mulungu wakonza zida zake zoopsa;
    Iye wakonzekera mivi yake yoyaka moto.

14 Taonani, munthu woyipa amalingalira zoyipa zokhazokha nthawi zonse.
    Zochita zake ndi zosokoneza ndi zovutitsa anthu ena.
15 Iye amene akumba dzenje ndi kulizamitsa
    amagwera mʼdzenje limene wakumbalo.
16 Mavuto amene amayambitsa amamubwerera mwini;
    chiwawa chake chimatsikira pa mutu wake womwe.

17 Ine ndidzayamika Yehova chifukwa cha chilungamo chake;
    ndipo ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina la Yehova Wammwambamwamba.

Amosi 5:1-9

Mawu Odandawulira Aisraeli

Israeli, imva mawu awa, nyimbo ya maliro imene ndikuyimba za iweyo:

“Namwali Israeli wagwa,
    moti sadzadzukanso,
wasiyidwa mʼdziko lake lomwe,
    popanda woti ndi kumudzutsa.”

Ambuye Yehova akuti,

“Mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 1,000 amphamvu
    udzatsala ndi anthu 100 okha;
mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 100 amphamvu
    udzatsala ndi anthu khumi okha basi.”

Zimene Yehova akunena kwa nyumba ya Israeli ndi izi:

“Mundifunefune kuti mukhale ndi moyo;
    musafunefune Beteli,
musapite ku Giligala,
    musapite ku Beeriseba.
Pakuti Giligala adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo,
    ndipo Beteli adzawonongekeratu.”
Funani Yehova kuti mukhale ndi moyo,
    mukapanda kutero Iye adzatentha nyumba ya Yosefe ngati moto;
motowo udzawononga,
    ndipo sipadzakhala wina wozimitsa motowo ku Beteli.

Inu amene mumasandutsa chiweruzo cholungama kukhala chowawa
    ndi kunyoza chilungamo.
(Iye amene analenga nyenyezi za Nsangwe ndi Akamwiniatsatana,
    amene amasandutsa mdima kuti ukhale mmawa
    ndi kudetsa usana kuti ukhale usiku,
amene amayitana madzi a mʼnyanja
    ndi kuwathira pa dziko lapansi,
    Yehova ndiye dzina lake.
Iyeyo amabweretsa chiwonongeko modzidzimutsa pa anthu amphamvu
    ndi kuwononga mizinda yotetezedwa),

Mateyu 25:31-46

Nkhosa ndi Mbuzi

31 “Pamene Mwana wa Munthu adzabwera mu ulemerero wake, pamodzi ndi angelo ake onse, adzakhala pa mpando waufumu mu ulemerero wakumwamba. 32 Mitundu yonse ya anthu idzasonkhanitsidwa pamaso pake, ndipo adzawalekanitsa iwo wina ndi mnzake monga mʼbusa amalekanitsa nkhosa ndi mbuzi. 33 Adzayika nkhosa ku dzanja lake lamanja ndi mbuzi ku lamanzere.

34 “Pamenepo mfumu idzati kwa a ku dzanja lamanja, ‘Bwerani inu odalitsika ndi Atate anga; landirani ufumu umene unakonzedwa chifukwa cha inu kuyambira pachiyambi cha dziko. 35 Pakuti ndinali ndi njala ndipo munandipatsa chakudya, ndinali ndi ludzu ndipo munandipatsa madzi akumwa, ndinali mlendo ndipo munandilandira, 36 ndinali wausiwa ndipo munandiveka, ndinali wodwala ndipo munandisamalira, ndinali ku ndende ndipo inu munandiyendera.’

37 “Ndipo olungamawo adzamuyankha kuti, ‘Ambuye ndi liti tinakuonani muli ndi njala ndipo tinakudyetsani, kapena ludzu ndipo tinakupatsani madzi akumwa? 38 Ndi liti tinakuonani muli mlendo ndipo tinakulandirani, kapena wa usiwa ndipo tinakuvekani? 39 Ndi liti tinakuonani mutadwala kapena ku ndende ndipo tinakuyenderani?’

40 “Mfumu idzayankha kuti, ‘Zoonadi, ndikuwuzani kuti chilichonse chimene munachitira mmodzi wa abale anga onyozekawa munandichitira Ine.’

41 “Pamenepo adzanena kwa akumanzere kwake kuti, ‘Chokani kwa Ine, inu otembereredwa, pitani ku moto wosatha wokonzedwera mdierekezi ndi angelo ake. 42 Pakuti ndinali ndi njala ndipo simunandipatse chakudya, ndinali ndi ludzu ndipo simunandipatse madzi akumwa, 43 ndinali mlendo koma inu simunandilandire, ndinali wa usiwa koma simunandiveke, ndinali wodwala komanso ku ndende simunandisamalire.’

44 “Iwo adzayankha kuti, ‘Ambuye ndi liti tinakuonani muli ndi njala kapena ludzu kapena mlendo kapena wausiwa kapena wodwala kapena mʼndende, ndipo kuti sitinakuthandizeni?’

45 “Iye adzayankha kuti, ‘Zoonadi, ndikuwuzani kuti chilichonse chimene simunachitire mmodzi wa abale anga onyozekawa simunandichitire Ine.’

46 “Amenewa adzapita ku chilango chosatha pamene olungama ku moyo wosatha.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.