Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 82

Salimo la Asafu.

82 Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu;
    Iye akuweruza pakati pa “milungu.”

“Mudzateteza osalungama mpaka liti,
    ndi kukondera anthu oyipa?
Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye;
    mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.
Landitsani anthu ofowoka ndi osowa;
    apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.

“Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse.
    Amayendayenda mu mdima;
    maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.

“Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu,
    nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’
Koma mudzafa ngati anthu wamba;
    mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”

Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi,
    pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.

Amosi 2:12-3:8

12 “Koma inu munawamwetsa vinyo anaziri aja,
    ndipo munalamula aneneri kuti asanenere.

13 “Tsono Ine ndidzakupsinjani
    monga imapsinjikira ngolo imene yadzaza ndi tirigu.
14 Munthu waliwiro sadzatha kuthawa,
    munthu wamphamvu sadzakhalanso ndi nyonga,
    wankhondo sadzapulumutsa moyo wake.
15 Munthu wa uta sadzalimbika,
    msilikali wothamanga kwambiri sadzapulumuka,
    ndipo wokwera pa akavalo sadzapulumutsa moyo wake.
16 Ngakhale asilikali olimba mtima kwambiri
    adzathawa ali maliseche pa tsikulo,”
            akutero Yehova.

Mboni Zotsutsa Israeli

Inu Aisraeli, imvani mawu awa amene Yehova wayankhula kutsutsana nanu, kutsutsana ndi banja lonse limene analitulutsa mu Igupto:

“Inu nokha ndi amene ndinakusankhani
    pakati pa mabanja onse a dziko lapansi;
nʼchifukwa chake ndidzakulangani
    chifukwa cha machimo anu onse.”

Kodi anthu awiri nʼkuyendera limodzi
    asanapangane?
Kodi mkango umabangula mʼnkhalango
    usanagwire nyama?
Kodi msona wamkango umalira mʼphanga mwake
    pamene sunagwire kanthu?
Kodi mbalame nʼkutera pa msampha
    pamene palibe nyambo yake?
Kodi msampha umafwamphuka
    usanakole kanthu?
Kodi pamene lipenga la nkhondo lalira mu mzinda,
    anthu sanjenjemera?
Pamene tsoka lafika mu mzinda,
    kodi si Yehova amene wachititsa zimenezo?

Zoonadi Ambuye Yehova sachita kanthu
    asanawulule zimene akufuna kuchita
    kwa atumiki ake, aneneri.

Mkango wabangula,
    ndani amene sachita mantha?
Ambuye Yehova wayankhula,
    ndani amene sanganenere?

Yohane 3:16-21

16 “Pakuti Mulungu anakonda dziko lapansi, kotero anapereka Mwana wake wobadwa yekha, kuti aliyense wokhulupirira Iye asatayike koma akhale ndi moyo wosatha. 17 Pakuti Mulungu sanatume Mwana wake ku dziko lapansi, kuti akaweruze, koma kuti akapulumutse dziko lapansi. 18 Aliyense wokhulupirira Iye saweruzidwa, koma aliyense wosakhulupirira waweruzidwa kale chifukwa sanakhulupirire dzina la Mwana wobadwa yekha wa Mulungu. 19 Ndipo chiweruzo ndi ichi: kuwunika kunabwera mʼdziko lapansi, koma anthu anakonda mdima mʼmalo mwa kuwunikako, chifukwa ntchito zawo zinali zoyipa. 20 Aliyense wochita zoyipa amadana ndi kuwunika, ndipo sabwera poyera chifukwa cha mantha kuti ntchito zake zingaonekere. 21 Koma aliyense wokhala mu choonadi amabwera ku kuwunika, kuti zionekere poyera zimene iye wachita zachitika kudzera mwa Mulungu.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.