Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.
124 Akanapanda kukhala mbali yathu Yehova,
anene tsono Israeli,
2 akanapanda kukhala mbali yathu Yehova,
potiwukira anthuwo,
3 iwo atatipsera mtima,
akanatimeza amoyo;
4 chigumula chikanatimiza,
mtsinje ukanatikokolola,
5 madzi a mkokomo
akanatikokolola.
6 Atamandike Yehova,
amene sanalole kuti tikhale chakudya cha mano awo.
7 Moyo wathu wawonjoka ngati mbalame
yokodwa mu msampha wa mlenje;
msampha wathyoka,
ndipo ife tapulumuka.
8 Thandizo lathu lili mʼdzina la Yehova
wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
4 Inu anthu, ndikuyitana inu;
ndikuyitanatu anthu onse.
5 Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera;
inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu.
6 Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri;
ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama.
7 Pakamwa panga pamayankhula zoona
ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa.
8 Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama;
mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka.
9 Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona;
kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza.
10 Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva,
nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino.
11 Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali,
ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru.
12 Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera.
Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino.
13 Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa.
Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama,
kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga.
14 Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino;
ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu.
15 Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira.
Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama.
16 Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula.
Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko.
17 Ndimakonda amene amandikonda,
ndipo amene amandifunafuna amandipeza.
18 Ine ndili ndi chuma ndi ulemu,
chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika.
19 Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala;
zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri.
20 Ndimachita zinthu zolungama.
Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo.
21 Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda
ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma.
15 Samalani makhalidwe anu, musakhale ngati opanda nzeru koma ngati anzeru. 16 Gwiritsani ntchito mpata uliwonse, chifukwa masiku ano ndi oyipa. 17 Choncho musakhale opusa, koma mudziwe zimene Ambuye akufuna kuti muchite. 18 Musaledzere ndi vinyo, chifukwa adzawononga moyo wanu. Mʼmalo mwake, mudzazidwe ndi Mzimu Woyera. 19 Muziyankhulana wina ndi mnzake mawu a Masalimo, nyimbo za Mulungu ndi nyimbo za uzimu. Muziyimbira Ambuye movomerezana ndi mitima yanu. 20 Muziyamika Mulungu Atate nthawi zonse chifukwa cha zonse, mʼdzina la Ambuye athu Yesu Khristu.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.