Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kwa Yedutuni. Salimo la Davide.
39 Ndinati, “Ndidzasamalira njira zanga
ndipo ndidzasunga lilime langa kuti ndisachimwe;
ndidzatseka pakamwa panga ndi chitsekerero
nthawi yonse imene woyipa ali pamaso panga.”
2 Koma pamene ndinali chete
osanena ngakhale kanthu kalikonse kabwino
mavuto anga anachulukirabe.
3 Mtima wanga unatentha mʼkati mwanga,
ndipo pamene ndinkalingalira, moto unayaka;
kenaka ndinayankhula ndi lilime langa:
4 “Yehova ndionetseni mathero a moyo wanga
ndi chiwerengero cha masiku anga;
mundidziwitse kuti moyo wanga ndi wosakhalitsa motani.
5 Inu mwachititsa kuti masiku anga akhale ochepa kwambiri,
kutalika kwa zaka zanga ndi kopanda phindu pamaso panu;
moyo wa munthu aliyense ndi waufupi.
Sela
6 Munthu ali ngati chithunzithunzi chake pamene akuyenda uku ndi uku:
Iye amangovutika koma popanda phindu;
amadzikundikira chuma, osadziwa kuti chidzakhala chayani.
7 “Koma tsopano Ambuye kodi ndifunanso chiyani?
Chiyembekezo changa chili mwa Inu.
8 Pulumutseni ku zolakwa zanga zonse;
musandisandutse chonyozeka kwa opusa.
9 Ine ndinali chete; sindinatsekule pakamwa panga
pakuti Inu ndinu amene mwachita zimenezi.
10 Chotsani mkwapulo wanu pa ine;
ndagonjetsedwa ndi nkhonya ya dzanja lanu.
11 Inu mumadzudzula ndi kulanga anthu chifukwa cha tchimo lawo;
mumawononga chuma chawo monga njenjete;
munthu aliyense ali ngati mpweya.
Sela
12 “Imvani pemphero langa Inu Yehova,
mverani kulira kwanga kopempha thandizo;
musakhale chete pamene ndikulirira kwa Inu,
popeza ndine mlendo wanu wosakhalitsa;
monga anachitira makolo anga onse.
13 Musandiyangʼane mwaukali, choncho ndidzatha kusangalala
ndisanafe ndi kuyiwalika.”
17 Mose atawatuma kuti akazonde Kanaani anati, “Mupite kudzera ku Negevi, mukapitirire mpaka ku dziko la mapiri. 18 Mukaone dzikolo kuti ndi lotani ndi anthu okhala mʼmenemo ngati ndi amphamvu kapena ofowoka, ochepa kapena ambiri. 19 Nanga dziko limene akukhalako ndi lotani? Ndi labwino kapena loyipa? Mizinda imene akukhalamo ndi yotani? Kodi ilibe malinga kapena ndi ya malinga? 20 Nthaka yake ndi yotani? Yachonde kapena yopanda chonde? Kodi dzikolo lili ndi mitengo kapena lilibe mitengo? Mukayesetse kubweretsako zipatso za mʼdzikomo.” (Inali nthawi yamphesa zoyamba kupsa).
21 Choncho anapita kukazonda dzikolo kuchokera ku chipululu cha Zini mpaka ku Rehobu, mopenyana ndi Lebo Hamati. 22 Anapita kudzera ku Negevi ndi kukafika ku Hebroni, kumene Ahimani, Sesai ndi Talimai, ana a Anaki ankakhala. (Anamanga Hebroni zaka zisanu ndi ziwiri asanamange Zowani ku Igupto). 23 Atafika ku chigwa cha Esikolo, anadulako nthambi ya mpesa ya phava limodzi la mphesa ndipo anthu awiri ananyamulizana, natenganso makangadza ndi nkhuyu. 24 Malo amenewo anawatcha chigwa cha Esikolo chifukwa cha phava la mphesa limene Aisraeli anadula kumeneko. 25 Patapita masiku makumi anayi, anthu aja anabwerako kokazonda dziko lija.
Kufotokoza Zomwe Anakaona
26 Ndipo atabwerako anapita kwa Mose ndi Aaroni ndi kwa Aisraeli onse ku Kadesi mʼchipululu cha Parani. Kumeneko anafotokozera anthu onse nawaonetsanso zipatso za mʼdzikolo. 27 Anthuwo anafotokozera Mose kuti, “Tinapita ku dziko komwe munatituma. Dzikolo ndi loyenda mkaka ndi uchi ndipo zipatso zake ndi izi.
Fanizo la Mbewu ya Mpiru ndi la Yisiti
18 Kenaka Yesu anafunsa kuti, “Kodi ufumu wa Mulungu uli ngati chiyani? Kodi Ine ndingawufanizire ndi chiyani? 19 Uli ngati mbewu ya mpiru, imene munthu anatenga ndi kudzala mʼmunda mwake. Inakula, nʼkukhala mtengo, ndipo mbalame zamlengalenga zinakhala mʼnthambi zake.”
20 Iye anafunsanso kuti, “Kodi ufumu wa Mulungu ndingawufanizire ndi chiyani? 21 Uli ngati yisiti amene mayi anatenga ndi kusakaniza ndi ufa wambiri mpaka anafufumitsa ufawo.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.