Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Salimo la matamando la Davide.
145 Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga;
ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
2 Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku
ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
3 Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse;
ukulu wake palibe angawumvetsetse.
4 Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina;
Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
5 Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu,
ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
6 Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri,
ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
7 Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu,
ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
8 Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo,
wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
9 Yehova ndi wabwino kwa onse;
amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
10 Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova;
oyera mtima adzakulemekezani.
11 Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu
ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
12 kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu
ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
13 Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya,
ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse.
Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse
ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
14 Yehova amagwiriziza onse amene akugwa
ndipo amakweza onse otsitsidwa.
15 Maso a onse amayangʼana kwa Inu,
ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
16 Mumatsekula dzanja lanu
ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
17 Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse,
ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
18 Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana,
onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
19 Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa;
amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
20 Yehova amayangʼana onse amene amamukonda
koma adzawononga anthu onse oyipa.
21 Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova.
Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera
ku nthawi za nthawi.
9 Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, wanditenga mtima,
iwe wanditenga mtima
ndi kapenyedwe ka maso ako,
ndiponso ndi umodzi mwa mikanda ya mʼkhosi mwako.
10 Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, chikondi chako nʼchosangalatsa!
Chikondi chako nʼchosangalatsa kwambiri kupambana vinyo,
ndiponso fungo la mafuta ako ndi lopambana zonunkhiritsa zonse!
11 Iwe mkwatibwi wanga, milomo yako ikuchucha uchi ngati chisa cha njuchi;
pansi pa lilime lako pali mkaka ndi uchi.
Fungo lonunkhira la zovala zako likumveka ngati fungo la ku Lebanoni.
12 Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, ndiwe munda wopiringidzidwa;
ndiwe kasupe wotchingidwa, chitsime chotetezedwa.
13 Zomera zako ndi munda wa zipatso za makangadza;
muli zipatso zokoma kwambiri,
muli hena ndi nadi,
14 nadi ndi safiro,
kalamusi ndi sinamoni,
komanso mtengo uliwonse wonunkhira bwino.
Mulinso mure ndi aloe
ndi zonunkhiritsa zonse zabwino kwambiri.
15 Iwe ndiwe kasupe wa mʼmunda,
chitsime cha madzi oyenda,
mtsinje wa madzi ochokera ku Lebanoni.
Mkazi
16 Dzuka, iwe mphepo yakumpoto,
ndipo bwera, iwe mphepo yakummwera!
Uzira pa munda wanga,
kuti fungo lake lonunkhira lifalikire ponseponse.
Bwenzi langa alowe mʼmunda mwake
ndi kudya zipatso zake zabwino kwambiri.
Mwamuna
5 Ndalowa mʼmunda mwanga, iwe mlongo wanga, iwe mkwatibwi wanga;
ndasonkhanitsa mure wanga ndi zokometsera zakudya zanga.
Ndadya uchi wanga pamodzi ndi zisa zake zomwe;
ndamwa vinyo wanga ndi mkaka wanga.
Abwenzi
Idyani abwenzi anga, imwani;
Inu okondana, imwani kwambiri.
Yesu Afunsidwa za Kusala Kudya
33 Iwo anati kwa Iye, “Ophunzira a Yohane amasala kudya ndi kupemphera kawirikawiri, monganso ophunzira a Afarisi, koma anu amangodya ndi kumwa.”
34 Yesu anawayankha kuti, “Kodi alendo a mkwati angasale kudya pamene mkwati ali pakati pawo? 35 Koma nthawi ikubwera pamene mkwati adzachotsedwa pakati pawo. Masiku amenewo adzasala kudya.”
36 Iye anawawuza fanizo ili: “Palibe amene amangʼamba chigamba kuchokera pa chovala chatsopano ndi kuchisokerera pa chakale. Ngati atatero, ndiye kuti adzangʼamba chovala chatsopanocho, ndipo chigamba chochokera pa chovala chatsopano chija sichidzagwirizana ndi chakale. 37 Ndipo palibe amene amakhuthulira vinyo watsopano mʼmatumba a vinyo akale. Ngati atatero, vinyo watsopanoyo adzaphulitsa zikopazo, vinyo adzatayika ndipo zikopa za vinyozo zidzawonongeka. 38 Ayi, vinyo watsopano ayenera kuthiridwa mʼmatumba a vinyo azikopa zatsopano. 39 Ndipo palibe amene atamwa vinyo wakale amafuna watsopano, pakuti amati, ‘Wakale ndi okoma.’ ”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.