Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Salimo la matamando la Davide.
145 Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga;
ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
2 Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku
ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
3 Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse;
ukulu wake palibe angawumvetsetse.
4 Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina;
Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
5 Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu,
ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
6 Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri,
ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
7 Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu,
ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
8 Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo,
wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
9 Yehova ndi wabwino kwa onse;
amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
10 Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova;
oyera mtima adzakulemekezani.
11 Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu
ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
12 kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu
ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
13 Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya,
ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse.
Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse
ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
14 Yehova amagwiriziza onse amene akugwa
ndipo amakweza onse otsitsidwa.
15 Maso a onse amayangʼana kwa Inu,
ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
16 Mumatsekula dzanja lanu
ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
17 Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse,
ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
18 Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana,
onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
19 Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa;
amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
20 Yehova amayangʼana onse amene amamukonda
koma adzawononga anthu onse oyipa.
21 Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova.
Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera
ku nthawi za nthawi.
Mwamuna
4 Ndiwe wokongoladi wokondedwa wanga!
Ndithudi, ndiwe wokongola!
Maso ako ali ngati nkhunda kumbuyo kwa nsalu yophimba kumutu.
Tsitsi lako lili ngati gulu la mbuzi
zikutsetsereka kuchokera ku Giliyadi.
2 Mano ako ali ngati gulu la nkhosa zomwe zangometedwa kumene,
zochokera kozisambitsa kumene.
Iliyonse ili ndi ana amapasa;
palibe imene ili yokha.
3 Milomo yako ili ngati mbota yofiira;
pakamwa pako ndi pokongola kwambiri.
Kukhalira kumbuyo kwa nsalu yako yophimba
kumutuyo, masaya ako akuoneka ngati mabandu a makangadza.
4 Khosi lako lili ngati nsanja ya Davide,
yomangidwa bwino ndi yosalala;
pa nsanja imeneyo pali zishango 1,000,
zishango zonsezo za anthu ankhondo.
5 Mawere ako ali ngati tiana tiwiri ta nswala,
ngati ana amapasa a nswala
amene akudya pakati pa maluwa okongola.
6 Kamphepo kamadzulo kakayamba kuwuzira
ndipo mithunzi ikayamba kuthawa,
ndidzapita ku phiri la mure
ndi ku chitunda cha lubani.
7 Ndiwe wokongola kwambiri wokondedwa wanga;
palibe chilema pa iwe.
8 Tiye tichoke ku Lebanoni iwe mkwatibwi wanga,
tiye tichoke ku Lebanoni,
utsikepo pa msonga ya Amana,
kuchoka pa msonga ya phiri la Seniri, pamwamba penipeni pa Herimoni,
kuchoka ku mapanga a mikango
ndiponso kumapiri kumene akambuku amavutitsa.
3 Landirani chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye athu Yesu Khristu.
Kuthokoza
4 Nthawi zonse ndimayamika Mulungu chifukwa cha inu chifukwa cha chisomo chake chopatsidwa kwa inu mwa Khristu Yesu. 5 Pakuti mwa Iye mwalemekezedwa mʼnjira iliyonse, mʼkuyankhula kwanu konse ndi mʼkudziwa kwanu konse, 6 chifukwa umboni wathu pa za Khristu unatsimikizidwa mwa inu. 7 Choncho inu simusowa mphatso yauzimu iliyonse pamene mukudikira mofunitsitsa kuti Ambuye athu Yesu Khristu avumbulutsidwe. 8 Adzakulimbikitsani mpaka kumapeto kuti mudzakhale wopanda mlandu pa tsiku lobwera Ambuye athu Yesu Khristu. 9 Mulungu amene wakuyitanani inu mu chiyanjano ndi Mwana wake Yesu Khristu Ambuye athu ngokhulupirika.
Kugawikana mu Mpingo
10 Ndidandaulira inu, abale, mʼdzina la Ambuye athu Yesu Khristu kuti nonsenu muvomerezane wina ndi mnzake kuti pasakhale kugawikana pakati panu ndi kuti mukhale amodzi kwenikweni mu nzeru ndi mʼmaganizo. 11 Abale anga, ena a ku nyumba ya Kloe andidziwitsa kuti pali mkangano pakati panu. 12 Chimene ndikutanthauza ndi ichi: wina amati, “Ndimatsatira Paulo,” wina, “Ndimatsatira Apolo,” wina, “Ndimatsatira Kefa,” winanso, “Ndimatsatira Khristu.”
13 Kodi Khristu wagawikana? Kodi Paulo anapachikidwa pa mtanda chifukwa cha inu? Kodi munabatizidwa mʼdzina la Paulo? 14 Ine ndikuyamika kuti sindinabatizepo mmodzi mwa inu kupatula Krispo ndi Gayo, 15 mwakuti palibe amene anganene kuti anabatizidwa mʼdzina langa. 16 (Inde, ine ndinabatizanso a mʼbanja la Stefano, koma sindikumbukira ngati ndinabatizanso wina aliyense). 17 Pakuti Khristu sananditume ine kudzabatiza, koma kudzalalikira Uthenga Wabwino, osati ndi mawu anzeru za umunthu, kuopa kuti mtanda wa Khristu ungakhale wopanda mphamvu.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.