Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.
126 Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni,
tinali ngati amene akulota.
2 Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka;
malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe.
Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti,
“Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”
3 Yehova watichitira zinthu zazikulu,
ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.
4 Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova,
monga mitsinje ya ku Negevi.
5 Iwo amene amafesa akulira,
adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.
6 Iye amene amayendayenda nalira,
atanyamula mbewu yokafesa,
adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe,
atanyamula mitolo yake.
Mawu a Chitonthozo kwa Anthu a Mulungu
40 Atonthozeni, atonthozeni anthu anga,
akutero Mulungu wanu.
2 Ayankhuleni moleza mtima anthu a ku Yerusalemu
ndipo muwawuzitse
kuti nthawi ya ukapolo wawo yatha,
tchimo lawo lakhululukidwa.
Ndawalanga mokwanira
chifukwa cha machimo awo onse.
3 Mawu a wofuwula mʼchipululu akuti,
“Konzani njira ya Yehova
mʼchipululu;
wongolani njira zake;
msewu owongoka wa Mulungu wathu mʼdziko lopanda kanthu.
4 Chigwa chilichonse achidzaze.
Phiri lililonse ndi chitunda chilichonse azitsitse;
Dziko lokumbikakumbika alisalaze,
malo azitundazitunda awasandutse zidikha.
5 Ndipo ulemerero wa Yehova udzaonekera,
ndipo mitundu yonse ya anthu idzawuona,
pakuti wanena zimenezi ndi Yehova.”
6 Wina ananena kuti, “Lengeza.”
Ndipo ine ndinati, “Kodi ndifuwule chiyani?
“Pakuti anthu onse ali ngati udzu
ndipo kukongola kwawo kuli ngati maluwa akuthengo.
7 Udzu umanyala ndipo maluwa amafota
chifukwa cha kuwomba kwa mpweya wa Yehova.”
Mawu aja anatinso, “Ndithudi anthu sasiyana ndi udzu.
8 Udzu umanyala ndipo maluwa amafota,
koma mawu a Mulungu wathu adzakhalapo mpaka muyaya.”
9 Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Ziyoni,
kwera pa phiri lalitali.
Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Yerusalemu,
fuwula kwambiri,
kweza mawu, usachite mantha;
uza mizinda ya ku Yuda kuti,
“Mulungu wanu akubwera!”
10 Taonani, Ambuye Yehova akubwera mwamphamvu,
ndipo dzanja lake likulamulira,
taonani akubwera ndi mphotho yake
watsogoza zofunkha zako za ku nkhondo.
11 Iye adzasamalira nkhosa zake ngati mʼbusa:
Iye adzasonkhanitsa ana ankhosa aakazi mʼmanja mwake
ndipo Iye akuwanyamula pachifuwa chake
ndi kutsogolera bwinobwino nkhosa zoyamwitsa.
22 Ife tikudziwa kuti chilengedwe chonse chakhala chikubuwula ndi ululu ngati ululu wa nthawi yobereka mwana mpaka tsopano lino. 23 Si zokhazo ayi, ngakhale ife tomwe, amene tili ndi zipatso zoyamba za Mzimu, tikubuwulira mʼkati mwathu pomwe tikudikira mwachidwi kusankhidwa kwathu ngati ana, kuwomboledwa kwa matupi athu. 24 Pakuti ife tinapulumutsidwa mʼchiyembekezo ichi. Koma chiyembekezo chimene chimaoneka si chiyembekezo ayi. Kodi ndani amene amayembekezera chimene ali nacho kale? 25 Koma ngati ife tiyembekeza chimene tikanalibe, ndiye kuti tikuyembekeza modekha mtima.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.