Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
118 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino;
pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
2 Israeli anene kuti:
“Chikondi chake ndi chosatha.”
14 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;
Iye wakhala chipulumutso changa.
15 Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano
ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti:
“Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
16 Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba
Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
17 Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo
ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
18 Yehova wandilanga koopsa,
koma sanandipereke ku imfa.
19 Tsekulireni zipata zachilungamo,
kuti ndifike kudzayamika Yehova.
20 Ichi ndicho chipata cha Yehova
chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
21 Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha;
mwakhala chipulumutso changa.
22 Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana
wasanduka wapangodya;
23 Yehova ndiye wachita zimenezi
ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
24 Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga;
tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
3 Usiku wonse ndili pa bedi langa
ndinafunafuna amene mtima wanga umamukonda;
ndinamufunafuna koma osamupeza.
2 Ndikudzuka tsopano ndipo ndidzayendayenda mu mzinda,
mʼmisewu yake ndi mʼmabwalo ake;
ndidzamufunafuna amene mtima wanga umamukonda.
Kotero ine ndinamufunafuna iyeyo koma osamupeza.
3 Alonda anandipeza
pamene ankayendera mzinda.
“Kodi mwamuonako amene mtima wanga umamukonda?”
4 Nditawapitirira pangʼono
ndinamupeza amene mtima wanga umamukonda.
Ndinamugwira ndipo sindinamulole kuti achoke
mpaka nditamulowetsa mʼnyumba ya amayi anga,
mʼchipinda cha amene anandibereka.
5 Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani
pali gwape ndi mbawala yayikazi zakuthengo:
Musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa
mpaka pamene chifunire ichocho.
6 Kodi ndani amene akubwera kuchokera ku chipululu
ngati utsi watolotolo,
wonunkhira mure ndi lubani,
zopangidwa kuchokera ku zonunkhira zonse za anthu amalonda?
7 Ona! Chimenecho ndi chonyamulira Solomoni,
choperekezedwa ndi asilikali 60,
anthu amphamvu a ku Israeli,
8 onse atanyamula lupanga,
onse odziwa bwino nkhondo,
aliyense ali ndi lupanga pambali pake,
kukonzekera zoopsa za usiku.
9 Mfumu Solomoni anadzipangira chonyamulirachi;
anachipanga ndi matabwa ochokera ku Lebanoni.
10 Milongoti yake anayipanga yasiliva,
kumbuyo kwake kwa golide.
Mipando yake inakutidwa ndi nsalu yapepo,
anakongoletsa mʼkati mwake ndi chikondi
cha akazi a ku Yerusalemu.
11 Tukulani inu akazi a ku Ziyoni
ndipo mudzaone mfumu Solomoni atavala chipewa chaufumu,
chipewa chaufumu chimene amayi ake anamuveka
pa tsiku la ukwati wake,
tsiku limene mtima wake unasangalala.
Kuuka kwa Yesu
16 Litapita tsiku la Sabata, Mariya Magadalena, ndi amayi ake a Yakobo, ndi Salome anagula zonunkhiritsa ndi cholinga chakuti apite akadzoze thupi la Yesu. 2 Mmamawa, tsiku loyamba la Sabata, dzuwa litangotuluka kumene, anali pa ulendo wopita ku manda 3 ndipo anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Kodi akatikugudubuzira mwala pa khomo la manda ndani?”
4 Koma atakweza maso awo, anaona kuti mwala umene unali waukulu kwambiri wagubuduzidwa kale. 5 Atalowa mʼmanda, anaona mnyamata atavala mwinjiro woyera atakhala ku mbali ya kumanja, ndipo iwo anachita mantha.
6 Iye anati, “Musaope. Kodi mukufuna Yesu wa ku Nazareti, amene anapachikidwa? Wauka! Sali muno. Onani malo amene anamugonekapo. 7 Koma pitani, kawuzeni ophunzira ake ndi Petro kuti, ‘Iye watsogola kupita ku Galileya. Kumeneko mukamuona Iye monga momwe anakuwuzirani.’ ”
8 Akunjenjemera ndi kudabwa, amayiwo anatuluka ndipo anathawa ku mandako. Sananene china chilichonse kwa aliyense, chifukwa anachita mantha.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.