Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 118:1-2

118 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino;
    pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.

Israeli anene kuti:
    “Chikondi chake ndi chosatha.”

Masalimo 118:14-24

14 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;
    Iye wakhala chipulumutso changa.

15 Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano
    ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti:
“Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
16     Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba
    Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”

17 Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo
    ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
18 Yehova wandilanga koopsa,
    koma sanandipereke ku imfa.

19 Tsekulireni zipata zachilungamo,
    kuti ndifike kudzayamika Yehova.
20 Ichi ndicho chipata cha Yehova
    chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
21 Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha;
    mwakhala chipulumutso changa.

22 Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana
    wasanduka wapangodya;
23 Yehova ndiye wachita zimenezi
    ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
24 Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga;
    tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.

Nyimbo ya Solomoni 3

Usiku wonse ndili pa bedi langa
    ndinafunafuna amene mtima wanga umamukonda;
    ndinamufunafuna koma osamupeza.
Ndikudzuka tsopano ndipo ndidzayendayenda mu mzinda,
    mʼmisewu yake ndi mʼmabwalo ake;
ndidzamufunafuna amene mtima wanga umamukonda.
    Kotero ine ndinamufunafuna iyeyo koma osamupeza.
Alonda anandipeza
    pamene ankayendera mzinda.
    “Kodi mwamuonako amene mtima wanga umamukonda?”
Nditawapitirira pangʼono
    ndinamupeza amene mtima wanga umamukonda.
Ndinamugwira ndipo sindinamulole kuti achoke
    mpaka nditamulowetsa mʼnyumba ya amayi anga,
    mʼchipinda cha amene anandibereka.
Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani
    pali gwape ndi mbawala yayikazi zakuthengo:
Musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa
    mpaka pamene chifunire ichocho.

Kodi ndani amene akubwera kuchokera ku chipululu
    ngati utsi watolotolo,
wonunkhira mure ndi lubani,
    zopangidwa kuchokera ku zonunkhira zonse za anthu amalonda?
Ona! Chimenecho ndi chonyamulira Solomoni,
    choperekezedwa ndi asilikali 60,
    anthu amphamvu a ku Israeli,
onse atanyamula lupanga,
    onse odziwa bwino nkhondo,
aliyense ali ndi lupanga pambali pake,
    kukonzekera zoopsa za usiku.
Mfumu Solomoni anadzipangira chonyamulirachi;
    anachipanga ndi matabwa ochokera ku Lebanoni.
10 Milongoti yake anayipanga yasiliva,
    kumbuyo kwake kwa golide.
Mipando yake inakutidwa ndi nsalu yapepo,
    anakongoletsa mʼkati mwake ndi chikondi
    cha akazi a ku Yerusalemu.
11 Tukulani inu akazi a ku Ziyoni
    ndipo mudzaone mfumu Solomoni atavala chipewa chaufumu,
    chipewa chaufumu chimene amayi ake anamuveka
pa tsiku la ukwati wake,
    tsiku limene mtima wake unasangalala.

Marko 16:1-8

Kuuka kwa Yesu

16 Litapita tsiku la Sabata, Mariya Magadalena, ndi amayi ake a Yakobo, ndi Salome anagula zonunkhiritsa ndi cholinga chakuti apite akadzoze thupi la Yesu. Mmamawa, tsiku loyamba la Sabata, dzuwa litangotuluka kumene, anali pa ulendo wopita ku manda ndipo anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Kodi akatikugudubuzira mwala pa khomo la manda ndani?”

Koma atakweza maso awo, anaona kuti mwala umene unali waukulu kwambiri wagubuduzidwa kale. Atalowa mʼmanda, anaona mnyamata atavala mwinjiro woyera atakhala ku mbali ya kumanja, ndipo iwo anachita mantha.

Iye anati, “Musaope. Kodi mukufuna Yesu wa ku Nazareti, amene anapachikidwa? Wauka! Sali muno. Onani malo amene anamugonekapo. Koma pitani, kawuzeni ophunzira ake ndi Petro kuti, ‘Iye watsogola kupita ku Galileya. Kumeneko mukamuona Iye monga momwe anakuwuzirani.’ ”

Akunjenjemera ndi kudabwa, amayiwo anatuluka ndipo anathawa ku mandako. Sananene china chilichonse kwa aliyense, chifukwa anachita mantha.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.