Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
5 Mayiko akumwamba amatamanda zozizwitsa zanu Yehova,
kukhulupirika kwanunso, mu msonkhano wa oyera mtima anu.
6 Pakuti ndani mu mlengalenga angalingane ndi Yehova?
Ndani wofanana ndi Yehova pakati pa zolengedwa zakumwamba?
7 Mu msonkhano wa oyera mtima Mulungu amaopedwa kwambiri;
Iye ndiye wochititsa mantha kupambana onse amene amuzungulira.
8 Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, ndani wofanana nanu?
Yehova ndinu wamphamvu ndipo kukhulupirika kwanu kwakuzungulirani.
9 Mumalamula nyanja ya mafunde awukali;
pamene mafunde ake awundana Inu mumawakhalitsa bata.
10 Munaphwanya Rahabe monga munthu wophedwa;
ndi dzanja lanu lamphamvu munabalalitsa adani anu.
11 Mayiko akumwamba ndi anu ndiponso dziko lapansi ndi lanu;
munapanga dziko lonse ndi zonse zili mʼmenemo.
12 Munalenga Kumpoto ndi Kummwera;
Tabori ndi Herimoni akuyimba ndi chimwemwe pa dzina lanu.
13 Mkono wanu ndi wamphamvu;
dzanja lanu ndi lamphamvu, dzanja lanu lamanja ndi lopambana.
14 Chilungamo ndi chiweruzo cholungama ndiye maziko a mpando wanu waufumu;
chikondi ndi kukhulupirika zimayenda patsogolo panu.
15 Ndi odala amene aphunzira kuyamika Inu,
amene amayenda mʼkuwunika kwa nkhope yanu Yehova.
16 Amakondwera mʼdzina lanu tsiku lonse lathunthu;
amasangalala koposa mʼchilungamo chanu.
17 Pakuti Inu ndiye ulemerero wawo ndi mphamvu yawo
ndipo mwa kukoma mtima kwanu Inu mumakweza nyanga yathu.
18 Ndithudi, chishango chathu ndi cha Yehova,
Mfumu yathu kwa Woyerayo wa Israeli.
19 Kale munayankhula mʼmasomphenya,
kwa anthu anu okhulupirika munati,
“Ndapatsa mphamvu wankhondo;
ndakweza mnyamata wochokera pakati pa anthu.
20 Ndamupeza mtumiki wanga Davide;
ndamudzoza ndi mafuta opatulika.
21 Dzanja langa lidzamuchirikiza;
zoonadi, mkono wanga udzamupatsa mphamvu.
22 Adani sadzamulamula kuti apereke msonkho;
anthu oyipa sadzamusautsa.
23 Ndidzaphwanya adani ake pamaso pake
ndi kukantha otsutsana naye.
24 Chikondi changa chokhulupirika chidzakhala naye,
ndipo kudzera mʼdzina langa nyanga yake idzakwezedwa.
25 Ndidzayika dzanja lake pa nyanja,
dzanja lake lamanja pa mitsinje.
26 Iyeyo adzafuwula kwa Ine kuti, ‘Ndinu Atate anga,
Mulungu wanga, Thanthwe ndi Chipulumutso changa.’
27 Ndidzamuyika kuti akhale mwana wanga woyamba kubadwa;
wokwezedwa kwambiri pakati pa mafumu a dziko lapansi.
28 Ndidzamusungira chifundo changa kwamuyaya,
ndipo pangano langa ndi iye silidzatha.
29 Ine ndidzakhazikitsa zidzukulu zake mpaka muyaya,
mpando wake waufumu ngati masiku a miyamba.
30 “Ngati ana ake adzataya lamulo langa
ndi kusatsatira malangizo anga,
31 ngati adzaswa malamulo anga
ndi kulephera kusunga ziphunzitso zanga,
32 Ine ndidzalanga tchimo lawo ndi ndodo,
mphulupulu zawo powakwapula.
33 Koma sindidzachotsa chikondi changa pa iye,
kapena kukhala wosakhulupirika kwa iyeyo.
34 Sindidzaswa pangano langa
kapena kusintha zimene milomo yanga yayankhula.
35 Ndinalumbira kamodzi mwa kuyera kwanga
ndipo sindidzanama kwa Davide,
36 kuti zidzukulu zake zidzakhale kwamuyaya
ndipo mpando wake waufumu udzakhazikika pamaso panga ngati dzuwa;
37 udzakhazikika kwamuyaya monga mwezi,
mboni yokhulupirika mʼmitambo.
Sela
Chipulumutso Chamuyaya cha Ziyoni
51 “Mverani Ine, inu amene mukufuna chipulumutso
ndiponso amene mumafunafuna Yehova:
Taganizani za thanthwe kumene munasemedwa
ndipo ku ngwenya kumene anakukumbani;
2 taganizani za Abrahamu, kholo lanu,
ndi Sara, amene anakubalani.
Pamene ndinkamuyitana nʼkuti alibe mwana,
koma ndinamudalitsa ndi kumupatsa ana ambiri.
3 Yehova adzatonthozadi Ziyoni,
ndipo adzachitira chifundo mabwinja ake onse;
Dziko lake la chipululu adzalisandutsa ngati Edeni,
malo ake owuma ngati munda wa Yehova.
Anthu adzayimba nyimbo zonditamanda
ndi kundiyamika.
4 “Mverani Ine, anthu anga:
tcherani khutu, inu mtundu wanga:
malangizo adzachokera kwa Ine;
cholungama changa chidzawunikira anthu a mitundu yonse.
5 Ndili pafupi kubwera kudzawombola anthu anga.
Ndidzabwera mofulumira ngati kuwunika kudzapulumutsa anthu anga;
ndipo ndidzalamulira anthu a mitundu yonse.
Mayiko akutali akundiyembekezera.
Iwo akudikira kuti ndidzawapulumutse.
6 Kwezani maso anu mlengalenga,
yangʼanani pansi pa dziko;
mlengalenga udzazimirira ngati utsi,
dziko lapansi lidzatha ngati chovala
ndipo anthu ake adzafa ngati nsabwe.
Koma chipulumutso changa chidzakhala mpaka muyaya,
chilungamo changa chidzakhala cha nthawi zonse.
7 “Mverani Ine, inu amene mukudziwa choonadi,
anthu inu amene mukusunga malangizo anga mʼmitima yanu;
musaope kudzudzulidwa ndi anthu
kapena kuopsezedwa akamakulalatirani.
8 Pakuti njenjete idzawadya ngati chovala;
mbozi idzawadya ngati thonje.
Koma chilungamo changa chidzakhala mpaka muyaya,
chipulumutso changa chidzakhala mpaka mibadomibado.”
9 Dzambatukani, dzambatukani! Valani zilimbe,
Inu Yehova;
dzambatukani, monga munkachitira masiku amakedzana,
monga nthawi ya mibado yakale.
Si ndinu kodi amene munaduladula Rahabe,
amene munabaya chinjoka cha mʼnyanja chija?
10 Kodi sindinu amene munawumitsa nyanja yayikulu,
madzi ozama kwambiri aja?
Kodi sindinu amene munapanga njira pa madzi ozama,
kuti anthu amene munawapulumutsa awoloke powuma?
11 Anthu amene Yehova anawawombola adzabwerera
nakafika ku Ziyoni nyimbo ili pakamwa;
chimwemwe chamuyaya chizidzaonekera pa nkhope zawo.
Adzakhala ndi chikondwerero ndi chimwemwe,
chisoni ndi kubuwula zidzathawa.
12 Yehova akuti, “Ndinetu amene ndimakutonthozani mtima.
Chifukwa chiyani mukuopa munthu woti adzafa?
Mukuopa munthu woti monga udzu sadzakhalitsa.
13 Koma inu mumayiwala Yehova Mlengi wanu,
amene anayala za mlengalenga
ndi kuyika maziko a dziko lapansi.
Inu nthawi zonse mumaopsezedwa
chifukwa cha ukali wa anthu okuponderezani
amene angofuna kukuwonongani.
Kodi uli kuti tsopano ukali wa anthu okuponderezaniwo?
14 Amʼndende adzamasulidwa posachedwa;
sadzalowa mʼmanda awo,
kapena kusowa chakudya.
15 Pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu,
amene ndimavundula nyanja kotero mafunde ake amakokoma.
Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
16 Ndayika mawu anga mʼkamwa mwanu
ndipo ndakuphimbani ndi mthunzi wa dzanja langa.
Ine ndimayika pa malo pake zinthu za mlengalenga,
ndipo ndinayika maziko a dziko lapansi,
ndimawuza anthu a ku Ziyoni kuti, ‘Ndinu anthu anga.’ ”
Mtumiki Wosankhidwa ndi Mulungu
15 Podziwa zimenezi, Yesu anachoka kumalo amenewo. Ambiri anamutsata Iye ndipo anachiritsira odwala awo onse 16 nawachenjeza kuti asamuwulule kuti yani. 17 Uku kunali kukwaniritsa zimene zinayankhulidwa kudzera mwa mneneri Yesaya kuti,
18 “Taonani mnyamata wanga amene ndinamusankha,
Wokondedwa wanga, amene moyo wanga ukondwera naye.
Pa Iye ndidzayika Mzimu wanga,
ndipo Iye adzalalikira chiweruzo kwa akunja.
19 Sadzalimbana, sadzafuwula,
ngakhale mmodzi sadzamva mawu ake mʼmakwalala.
20 Bango lophwanyika sadzalithyola,
ndi nyale yofuka sadzayizimitsa,
kufikira Iye adzatumiza chiweruziro chikagonjetse.
21 Ndipo akunja adzakhulupirira dzina lake.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.