Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 148

148 Tamandani Yehova.

Tamandani Yehova, inu a kumwamba,
    mutamandeni Iye, inu a mlengalenga.
Mutamandeni, inu angelo ake onse,
    mutamandeni, mutamandeni, inu zolengedwa za mmwamba.
Mutamandeni, inu dzuwa ndi mwezi,
    mutamandeni, inu nonse nyenyezi zowala.
Mutamandeni, inu thambo la kumwambamwamba
    ndi inu madzi a pamwamba pa thambo.
Zonse zitamande dzina la Yehova
    pakuti Iye analamula ndipo zinalengedwa.
Iye anaziyika pa malo ake ku nthawi za nthawi;
    analamula ndipo sizidzatha.

Tamandani Yehova pa dziko lapansi,
    inu zolengedwa zikuluzikulu za mʼnyanja, ndi nyanja zonse zakuya,
inu zingʼaningʼani ndi matalala, chipale ndi mitambo,
    mphepo yamkuntho imene imakwaniritsa mawu ake,
inu mapiri ndi zitunda zonse,
    inu mitengo ya zipatso ndi mikungudza yonse,
10 inu nyama zakuthengo ndi ngʼombe zonse,
    inu zolengedwa zingʼonozingʼono ndi mbalame zowuluka.
11 Inu mafumu a dziko lapansi ndi anthu a mitundu yonse,
    inu akalonga ndi olamulira a dziko lapansi.
12 Inu anyamata ndi anamwali,
    inu nkhalamba ndi ana omwe.

13 Onsewo atamande dzina la Yehova
    pakuti dzina lake lokha ndi lolemekezeka;
    ulemerero wake ndi woopsa pa dziko lapansi pano ndi kumwamba komwe.
14 Iye wakwezera nyanga anthu ake,
    matamando a anthu ake onse oyera mtima,
    Aisraeli, anthu a pamtima pake.

Tamandani Yehova.

Yesaya 49:13-23

13 Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga;
    kondwera, iwe dziko lapansi;
    imbani nyimbo inu mapiri!
Pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake,
    ndipo wachitira chifundo anthu ake ovutika.

14 Koma Ziyoni anati, “Yehova wandisiya,
    Ambuye wandiyiwala.”

15 “Kodi amayi angathe kuyiwala mwana wawo wakubere
    ndi kusachitira chifundo mwana amene anabereka iwo eni?
Ngakhale iye angathe kuyiwala,
    Ine sindidzakuyiwala iwe!
16 Taona, ndakulemba iwe mʼzikhantho zanga;
    makoma ako ndimawaona nthawi zonse.
17 Amisiri odzakumanganso akubwerera mofulumira,
    ndipo amene anakupasula akuchokapo.
18 Kweza maso ako ndipo uyangʼaneyangʼane
    ana ako onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe.
Yehova akuti, ‘Ine Yehova wamoyo,
    anthu ako adzakhala ngati chinthu chodzikongoletsa
    chimene mkwatibwi wavala pa mkono pake.’

19 “Ngakhale unasanduka bwinja ndi kuwonongedwa
    ndipo dziko lako ndi kusakazidwa,
chifukwa cha kuchuluka kwa anthu malo okhalamo adzakhala operewera
    ndipo amene anakuwononga iwe aja adzakhala kutali.
20 Ana obadwa nthawi yako yachisoni
    adzanena kuti,
‘Malo ano atichepera,
    tipatse malo ena woti tikhalemo.’
21 Tsono iwe udzadzifunsa kuti,
    ‘Kodi ndani anandiberekera ana amenewa?
Ana anga onse anamwalira ndipo sindinathenso kukhala ndi ana ena;
    ndinapita ku ukapolo ndipo ndinachotsedwa.
    Ndani anawalera ana amenewa?
Ndinatsala ndekha,
    nanga awa, achokera kuti?’ ”

22 Zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi,

“Taonani, Ine ndidzakodola Anthu a mitundu ina kuti abwere.
    Ndidzawakwezera anthu a mitundu ina mbendera yanga kuti abwere.
Tsono adzabwera ndi ana ako aamuna atawanyamula mʼmanja mwawo
    ndipo adzanyamula ana ako aakazi pa mapewa awo.
23 Mafumu adzakhala abambo wongokulera
    ndipo akazi a mafumu adzakhala amayi wongokulera.
Iwo adzagwetsa nkhope
    zawo pansi.
Ndiye inu mudzazindikira kuti Ine ndine Yehova;
    iwo amene amadalira Ine sadzakhumudwa.”

Mateyu 18:1-14

Wamkulu mu Ufumu Wakumwamba

18 Pa nthawi imeneyo ophunzira anabwera kwa Yesu ndipo anamufunsa kuti, “Wamkulu woposa onse ndani mu ufumu wakumwamba?”

Iye anayitana kamwana kakangʼono ndi kukayimiritsa pakati pawo. Ndipo Iye anati, “Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti ngati simusintha ndi kukhala ngati tiana tatingʼono, simudzalowa konse mu ufumu wakumwamba. Chifukwa chake, aliyense amene adzichepetsa yekha ngati kamwana aka, ameneyo ndiye wamkulu koposa onse mu ufumu wakumwamba. Ndipo aliyense amene alandira kamwana kakangʼono ngati aka mu dzina langa, alandira Ine.

Za Kuchimwitsa Ena

“Koma ngati wina aliyense achimwitsa mmodzi wa ana awa, amene akhulupirira Ine, kuti achimwe, kukanakhala bwino kuti iye amangiriridwe chimwala chachikulu mʼkhosi mwake ndi kumizidwa pansi pa nyanja. Tsoka dziko lapansi chifukwa cha zinthu zimene ziyenera kubwera, koma tsoka kwa munthu amene abweretsa zotere! Ngati dzanja lako kapena phazi lako likuchimwitsa, lidule ndi kulitaya. Ndi bwino kwa iwe kulowa mʼmoyo wosatha wolumala kusiyana ndi kukhala ndi manja awiri kapena mapazi awiri ndi kukaponyedwa ku moto wosatha. Ndipo ngati diso lako likuchimwitsa, ulichotse ndi kulitaya. Ndi bwino kwa iwe kuti ukalowe ku moyo wosatha ndi diso limodzi kuposa ndi kukhala ndi maso awiri ndi kukaponyedwa ku moto wa gehena.”

Fanizo la Nkhosa Yotayika

10 “Onetsetsani kuti musanyoze mmodzi wa anawa. Pakuti ndikuwuzani kuti angelo awo kumwamba amakhala pamaso pa Atate anga akumwamba nthawi zonse.” 11 (Mwana wa Munthu anabwera kudzapulumutsa chimene chinatayika).

12 “Kodi mukuganiza bwanji? Ngati munthu ali ndi nkhosa 100 ndipo imodzi nʼkusowa, kodi sasiya 99 zija mʼmapiri ndi kupita kukafuna imodzi yosocherayo? 13 Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti akayipeza amasangalala kwambiri chifukwa cha nkhosa imodziyo kuposa nkhosa 99 zimene sizinasochere. 14 Chimodzimodzinso Atate anu akumwamba safuna kuti mmodzi wa anawa atayike.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.