Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
2 “Koma iwe Betelehemu Efurata,
ngakhale uli wonyozeka pakati pa mafuko a Yuda,
mwa iwe mudzatuluka
munthu amene adzalamulira Israeli,
amene chiyambi chake nʼchakalekale,
nʼchamasiku amakedzana.”
3 Nʼchifukwa chake Israeli adzasiyidwa
mpaka pa nthawi imene mayi amene ali woyembekezera adzachire.
Ndipo abale ake onse otsalira adzabwerera
kudzakhala pamodzi ndi Aisraeli.
4 Iye adzalimbika, ndipo adzaweta nkhosa zake
mwa mphamvu ya Yehova,
mu ulemerero wa dzina la Yehova Mulungu wake.
Ndipo iwo adzakhala mu mtendere,
pakuti ukulu wake udzakhala ponseponse pa dziko lapansi.
5 Ndipo Iye adzakhala mtendere wawo.
Chipulumutso ndi Chiwonongeko
Asiriya akadzalowa mʼdziko lathu
ndi kuyamba kuthira nkhondo malo athu otetezedwa,
tidzawadzutsira abusa asanu ndi awiri,
ngakhalenso atsogoleri asanu ndi atatu.
Nyimbo ya Mariya
46 Ndipo Mariya anati:
“Moyo wanga ulemekeza Ambuye.
47 Ndipo mzimu wanga ukondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga,
48 pakuti wakumbukira
kudzichepetsa kwa mtumiki wake.
Kuyambira tsopano mibado yonse idzanditcha wodala,
49 pakuti Wamkuluyo wandichitira ine zinthu zazikulu,
dzina lake ndi loyera.
50 Chifundo chake chifikira kwa iwo amene amuopa Iye
kufikira mibadomibado.
51 Iye wachita zamphamvu ndi dzanja lake;
Iye anabalalitsa iwo amene ali onyada mʼmaganizo awo.
52 Iye anachotsa olamulira pa mipando yawo yaufumu,
koma wakweza odzichepetsa.
53 Iye wakhutitsa a njala ndi zinthu zabwino
koma anachotsa olemera wopanda kanthu.
54 Iye anathandiza mtumiki wake Israeli,
pokumbukira chifundo chake.
55 Kwa Abrahamu ndi zidzukulu zake ku nthawi zonse
monga ananena kwa makolo athu.”
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Salimo la Asafu.
80 Tcherani khutu Inu mʼbusa wa Israeli,
Inu amene mumatsogolera Yosefe monga nkhosa;
Inu amene mumakhala pa mpando waufumu pakati pa akerubi, walani
2 kwa Efereimu, Benjamini ndi Manase.
Utsani mphamvu yanu;
bwerani ndi kutipulumutsa.
3 Tibwezereni mwakale Inu Mulungu;
nkhope yanu itiwalire
kuti tipulumutsidwe.
4 Inu Mulungu Wamphamvuzonse,
mpaka liti mkwiyo wanu udzanyeka
kutsutsana ndi mapemphero a anthu anu?
5 Mwawadyetsa buledi wa misozi;
mwachitisa iwo kumwa misozi yodzaza mbale.
6 Mwachititsa kuti tikhale gwero la mikangano pakati pa anansi athu,
ndipo adani athu akutinyoza.
7 Tibwezereni mwakale Inu Mulungu Wamphamvuzonse,
nkhope yanu itiwalire
kuti tipulumutsidwe.
5 Nʼchifukwa chake Khristu atabwera pa dziko lapansi anati,
“Simunafune nsembe kapena zopereka,
koma thupi munandikonzera.
6 Simunakondwere nazo nsembe zopsereza
ndi nsembe zopereka chifukwa cha tchimo.
7 Tsono, Ine ndinati, ‘Ndili pano Ine,
Inu Mulungu, ndabwera kudzachita zimene mukufuna monga zinalembedwa mʼMalemba.’ ”
8 Poyamba Iye anati, “Nsembe kapena zopereka zopsereza ndi nsembe zopereka chifukwa cha tchimo, Inu simunazifune kapena kukondwera nazo.” Ngakhale kuti Malamulo ndiye amanena kuti ziperekedwe. 9 Pamenepo Iye anati, “Ndili pano Ine, ndabwera kudzachita zimene mukufuna.” Khristu anachotsa nsembe zoyamba zija kuti mʼmalo mwake ayikemo nsembe za mtundu wachiwiri. 10 Chifukwa chakuti Yesu Khristu anachita zimene Mulungu anafuna kuti achite, ndife oyeretsedwa ndi nsembe ya thupi lake, limene analipereka kamodzi kokha.
Mariya Acheza kwa Elizabeti
39 Nthawi imeneyo anakonzeka ndipo anapita mofulumira ku mudzi wa ku mapiri a dziko la Yudeya, 40 kumene anakalowa mʼnyumba ya Zakariya nalonjera Elizabeti. 41 Elizabeti atamva moni wa Mariya, mwana anatakataka mʼmimba mwake, ndipo Elizabeti anadzazidwa ndi Mzimu Woyera. 42 Anafuwula ndi mawu akulu kuti, “Ndiwe wodala pakati pa akazi, ndipo ndi wodala mwana amene udzabereke! 43 Koma nʼchifukwa chiyani andikomera mtima kuti amayi a Ambuye anga abwere kwa ine? 44 Nthawi yomwe ndinamva mawu akulonjera kwanu, mwana anatakataka mʼmimba mwanga chifukwa cha chimwemwe. 45 Wodala iye amene wakhulupirira kuti chimene Ambuye wanena kwa iye chidzakwaniritsidwa!”
Nyimbo ya Mariya
46 Ndipo Mariya anati:
“Moyo wanga ulemekeza Ambuye.
47 Ndipo mzimu wanga ukondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga,
48 pakuti wakumbukira
kudzichepetsa kwa mtumiki wake.
Kuyambira tsopano mibado yonse idzanditcha wodala,
49 pakuti Wamkuluyo wandichitira ine zinthu zazikulu,
dzina lake ndi loyera.
50 Chifundo chake chifikira kwa iwo amene amuopa Iye
kufikira mibadomibado.
51 Iye wachita zamphamvu ndi dzanja lake;
Iye anabalalitsa iwo amene ali onyada mʼmaganizo awo.
52 Iye anachotsa olamulira pa mipando yawo yaufumu,
koma wakweza odzichepetsa.
53 Iye wakhutitsa a njala ndi zinthu zabwino
koma anachotsa olemera wopanda kanthu.
54 Iye anathandiza mtumiki wake Israeli,
pokumbukira chifundo chake.
55 Kwa Abrahamu ndi zidzukulu zake ku nthawi zonse
monga ananena kwa makolo athu.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.