Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
147 Tamandani Yehova.
Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu,
nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda!
2 Yehova akumanga Yerusalemu;
Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli.
3 Akutsogolera anthu osweka mtima
ndi kumanga mabala awo.
4 Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi,
ndipo iliyonse amayitchula dzina.
5 Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri;
nzeru zake zilibe malire.
6 Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa,
koma amagwetsa pansi anthu oyipa.
7 Imbirani Yehova ndi mayamiko;
imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.
8 Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo;
amapereka mvula ku dziko lapansi
ndi kumeretsa udzu mʼmapiri.
9 Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe
ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya.
10 Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo,
kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu.
11 Yehova amakondwera ndi amene amamuopa,
amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika.
20 Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu;
anthu enawo sadziwa malamulo ake.
Tamandani Yehova.
36 Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
2 “Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani
kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
3 Nzeru zanga ndimazitenga kutali;
ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
4 Ndithudi mawu anga si abodza;
wanzeru zangwiro ali ndi inu.
5 “Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu;
Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
6 Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo
koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
7 Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama;
amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu
ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
8 Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo,
ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
9 Iye amawafotokozera zomwe anachita,
kuti iwo anachimwa modzikuza.
10 Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake
ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
11 Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira,
adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere,
adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
12 Koma ngati samvera,
adzaphedwa ndi lupanga
ndipo adzafa osadziwa kanthu.
13 “Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo;
akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
14 Amafa akanali achinyamata,
pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
15 Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo;
Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
16 “Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso,
kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani,
kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
17 Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu;
chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
18 Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma;
musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
19 Kodi chuma chanu
kapena mphamvu zanu zonse
zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
20 Musalakalake kuti usiku ubwere,
pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
21 Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo,
chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
22 “Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu.
Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
23 Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite,
kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
Paulo Chitsanzo cha Mtumiki wa Uthenga Wabwino
9 Kodi sindine mfulu? Kodi sindine mtumwi? Kodi sindinamuone Ambuye athu Yesu? Kodi inu sindiye zotsatira za ntchito yanga mwa Ambuye? 2 Ngakhale kwa ena sindingakhale mtumwi, mosakayika ndine mtumwi kwa inu! Poti inu ndi chizindikiro cha utumwi wanga mwa Ambuye.
3 Kwa iwo wofuna kundizenga milandu ndimawayankha kuti: 4 Kodi ife tilibe ulamuliro wakudya ndi kumwa? 5 Kodi ife tilibe ulamuliro wotenga mkazi wokhulupirira nʼkumayenda naye monga amachitira atumwi ena ndi abale awo a Ambuye ndiponso Kefa? 6 Kodi kapena ine ndekha ndi Barnaba ndiye tikuyenera kugwira ntchito kuti tipeze zotisowa?
7 Ndani angagwire ntchito ya usilikali namadzipezera yekha zofunika zonse? Kodi ndani amadzala mpesa koma wosadyako zipatso zake? Ndani amaweta nkhosa koma wosamwako mkaka wake? 8 Kodi moti zimene ndikunenazi ndimaganizo a umunthu chabe? Kodi Malamulo sakunena chimodzimodzinso? 9 Popeza analemba mʼMalamulo a Mose kuti, “Musamange ngʼombe pakamwa pamene ikupuntha tirigu.” Kodi pamene Mulungu ananena zimenezi ankalabadira za ngʼombe zokha? 10 Ndithu Iyeyo amanena za ifenso, kodi si choncho? Inde, izi anazilemba chifukwa cha ife, pakuti wolima ndiponso wopuntha, onsewo amagwira ntchito mwachiyembekezo chodzagawana zokololazo. 11 Ngati tidzala mbewu yauzimu pakati panu, kodi ndi chovuta kwambiri kuti tikolole zosowa zathu kuchokera kwa inu? 12 Ngati ena ali ndi ufulu wothandizidwa ndi inu, kodi ife sitikuyenera kukhala nawo ufulu ochulukirapo?
Koma ife sitinagwiritse ntchito ufulu umenewu. Mʼmalo mwake timangodzichitira chilichonse posafuna kutsekereza ena kumva Uthenga Wabwino wa Khristu.
13 Kodi simukudziwa kuti wogwira ntchito mʼNyumba ya Mulungu amapeza chakudya chawo mʼNyumbamo, ndipo kuti otumikira pa guwa lansembe amagawana zimene zaperekedwa pa guwa lansembelo. 14 Chomwechonso Ambuye akulamula kuti wolalikira Uthenga Wabwino azilandira thandizo lawo polalikira Uthenga Wabwinowo.
15 Koma ine sindinagwiritse ntchito ufulu woterewu. Sindikulemba izi ndi chiyembekezo choti mundichitire zoterezi. Kuli bwino ndife kusiyana nʼkuti wina alande zomwe ndimazinyadira. 16 Komatu ndikamalalikira Uthenga Wabwino, sindingadzitamandire popeza ndimawumirizidwa kulalikira. Tsoka kwa ine ngati sindilalikira Uthenga Wabwino!
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.