Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 27

Salimo la Davide.

27 Yehova ndiye kuwunika kwanga ndi chipulumutso changa;
    ndidzaopa yani?
Yehova ndi linga la moyo wanga;
    ndidzachita mantha ndi yani?
Pamene anthu oyipa abwera kudzalimbana nane
    kudzadya mnofu wanga,
pamene adani anga ndi achiwembu andithira nkhondo,
    iwo adzapunthwa ndi kugwa.
Ngakhale gulu lankhondo lindizinge,
    mtima wanga sudzaopa.
Ngakhale nkhondo itayambika kulimbana nane,
    ngakhale nthawi imeneyo, ine ndidzalimbika mtima.

Chinthu chimodzi chokha chimene ndipempha kwa Yehova,
    ichi ndi chimene ndidzachifunafuna:
kuti ndikhale mʼNyumba ya Yehova
    masiku onse a moyo wanga,
ndi kuyangʼana kukongola kwa Yehova,
    ndi kumufunafuna Iye mʼNyumba yake.
Pakuti pa tsiku la msautso
    Iye adzanditeteza mʼmalo ake okhalamo;
adzandibisa mʼkati mwa Nyumba yake
    ndi kukhazika ine pamwamba pa thanthwe.
Kotero mutu wanga udzakwezedwa
    kuposa adani anga amene andizungulira;
pa Nyumba yake ndidzapereka nsembe ndi mfuwu wachimwemwe;
    ndidzayimba nyimbo kwa Yehova.

Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu Yehova
    mundichitire chifundo ndipo mundiyankhe.
Mtima wanga ukuti kwa Inu, “Funafuna nkhope yake!”
    Nkhope yanu Yehova ndidzayifunafuna.
Musandibisire nkhope yanu,
    musamubweze mtumiki wanu mwamkwiyo;
    mwakhala muli thandizo langa.
Musandikane kapena kunditaya,
    Inu Mulungu Mpulumutsi wanga.
10 Ngakhale abambo ndi amayi anga anditaya
    Yehova adzandisamala.
11 Phunzitseni njira yanu Inu Yehova,
    munditsogolere mʼnjira yowongoka
    chifukwa cha ondizunza.
12 Musandipereke ku zokhumba za adani anga,
    pakuti mboni zambiri zauka kutsutsana nane
    ndipo zikundiopseza.

13 Ine ndikutsimikiza mtima za zimenezi;
    ndidzaona ubwino wa Yehova
    mʼdziko la anthu amoyo.
14 Dikirani pa Yehova;
    khalani anyonga ndipo limbani mtima
    nimudikire Yehova.

Yesaya 4:2-6

Nthambi ya Yehova

Tsiku limenelo Nthambi ya Yehova idzakhala yokongola ndi yaulemerero, ndipo chipatso cha mʼdziko chidzakhala chonyaditsa ndi chopereka ulemerero kwa onse opulumuka mu Israeli. Iwo amene adzatsale mu Ziyoni, amene adzatsalire mu Yerusalemu, adzatchedwa oyera, onse amene mayina awo alembedwa pakati pa anthu amoyo okhala mu Yerusalemu. Ambuye adzasambitsa akazi a Ziyoni ndi kuchotsa zonyansa zawo. Adzatsuka magazi amene anakhetsedwa mu Yerusalemu ndi mzimu wachiweruzo ndiponso mzimu wamoto. Tsono Yehova adzayika mtambo wake pamwamba ponse pa phiri la Ziyoni, ndipo pa onse amene asonkhana masana padzakhala mtambo wa utsi ndipo usiku padzakhala malawi amoto. Pamwamba pa zonse padzakhala ulemerero wa Yehova. Ulemerero wake udzakhala mthunzi wothawiramo kutentha kwa masana, udzakhala malo opeweramo mphepo ndi owusiramo mvula.

Machitidwe a Atumwi 11:1-18

Petro Afotokozera Mpingo

11 Atumwi ndi abale a ku Yudeya konse anamva kuti anthu a mitundu ina analandiranso Mawu a Mulungu. Tsono Petro atafika ku Yerusalemu, abale amene anali a mdulidwe anamutsutsa iye, ndipo anati, “Iwe unalowa mʼnyumba ya anthu osachita mdulidwe ndi kudya nawo.”

Koma Petro anayamba kuwafotokozera zonse mwatsatanetsatane momwe zinachitikira kuti, “Ine ndimapemphera mu mzinda wa Yopa ndipo ndili ngati wokomoka ndinaona masomphenya. Ndinaona chinthu chokhala ngati chinsalu chachikulu chikutsika kuchokera kumwamba chogwiridwa msonga zake zinayi, ndipo chinatsikira pa ine. Ine ndinayangʼana mʼkati mwake ndipo ndinaona nyama za miyendo inayi za mʼdziko lapansi, zirombo, zokwawa, ndi mbalame zamlengalenga. Kenaka ine ndinamva mawu akuti, ‘Petro, Imirira. Ipha, nudye.’

“Ine ndinayankha kuti, ‘Ayi, Ambuye! Pakuti chinthu chodetsedwa ndi chonyansa sindinadyepo pakamwa pangapa.’

“Mawu ochokera kumwamba ananenanso kachiwiri kuti, ‘Chimene Mulungu wachiyeretsa usanene kuti ndi chodetsedwa.’ 10 Zimenezi zinachitika katatu ndipo kenaka zonse zinatengedwa kupita kumwamba.

11 “Nthawi yomweyo anthu atatu amene anatumidwa kuchokera ku Kaisareya anayima pa nyumba yomwe ndimakhalayo. 12 Mzimu anandiwuza kuti ndisakayike, koma ndipite nawo. Abale asanu ndi mmodzi awa anapitanso nane ndipo tinalowa mʼnyumba ya munthuyo. 13 Iye anatiwuza mmene anaonera mngelo atayimirira mʼnyumba mwake ndi kumuwuza kuti, ‘Tumiza anthu ku Yopa kuti akayitane Simoni wotchedwa Petro. 14 Iye adzakuwuza uthenga umene udzapulumutsa iwe ndi a pa banja ako.’

15 “Nditangoyamba kuyankhula, Mzimu Woyera anafika pa iwo monga momwe anafikira pa ife poyamba paja. 16 Kenaka ndinakumbukira zimene Ambuye ananena kuti, ‘Yohane anabatiza ndi madzi, koma inu mudzabatizidwa ndi Mzimu Woyera.’ 17 Tsono ngati Mulungu anawapatsa iwo mphatso yomweyo imene anatipatsa ife, amene tinakhulupirira Ambuye Yesu Khristu, ndine yani kuti nditsutsane ndi Mulungu?”

18 Iwo atamva zimenezi analibenso chonena ndipo anayamika Mulungu nati, “Potero Mulungu wapatsa anthu a mitundu ina mwayi wotembenuka mtima ndi kulandira moyo.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.