Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
2 Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga;
ndidzamudalira ndipo sindidzachita mantha.
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;
Iye wakhala chipulumutso changa.”
3 Mudzakondwera popeza Yehova
ali ngati chitsime cha chipulumutso chanu.
4 Tsiku limenelo mudzati:
“Yamikani Yehova, tamandani dzina lake;
mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu,
ndipo mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.
5 Imbirani Yehova, pakuti wachita ntchito zazikulu;
zimenezi zidziwike pa dziko lonse lapansi.
6 Fuwulani ndi kuyimba mwachimwemwe, inu anthu a ku Ziyoni;
pakuti Woyerayo wa Israeli ndi wamkulu pakati panu.”
Tsoka kwa Osalabadira Kanthu
6 Tsoka kwa amene simukulabadira kanthu ku Ziyoni,
ndiponso kwa inu amene mukukhala mwamtendere pa Phiri la Samariya,
inu anthu otchuka ochokera ku mtundu wa anthu omveka,
kumene Aisraeli amafikako!
2 Pitani ku mzinda wa Kaline mukawuyangʼane;
mukapitenso ku Hamati-raba mzinda waukulu uja,
ndipo mukatsikirenso ku Gati kwa Afilisti.
Kodi mizinda imeneyi ndi yopambana maufumu anu awiriwa?
Kodi dziko lawo ndi lalikulu kupambana lanu?
3 Inu simulabadirako kuti tsiku loyipa lidzafika,
zochita zanu zimafulumizitsa ulamuliro wankhanza.
4 Mumagona pa mabedi owakongoletsa ndi minyanga ya njovu,
mumagona pa mipando yanu ya wofuwofu.
Mumadya ana ankhosa onona
ndi ana angʼombe onenepa.
5 Mumayimba azeze anu ndi kumangopeka
nyimbo pa zingʼwenyengʼwenye ngati Davide.
6 Mumamwera vinyo mʼzipanda zodzaza
ndipo mumadzola mafuta abwino kwambiri,
koma simumva chisoni ndi kuwonongeka kwa Yosefe.
7 Nʼchifukwa chake inu mudzakhala mʼgulu la anthu oyamba kupita ku ukapolo;
maphwando ndi zikondwerero zanu zidzatheratu.
Yehova Amanyansidwa ndi Kunyada kwa Israeli
8 Ambuye Yehova walumbira mʼdzina lake. Yehova Mulungu Wamphamvuzonse walengeza kuti,
“Ndimanyansidwa ndi kunyada kwa Yakobo,
ndimadana ndi nyumba zake zaufumu;
Ine ndidzawupereka mzindawu
pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo.”
Kulimbikitsa Zopereka
8 Ndipo tsopano, abale, tikufuna kuti mudziwe za chisomo chimene Mulungu wapereka ku mipingo ya ku Makedoniya. 2 Pakati pa mayesero owawitsa, chimwemwe chawo chosefukira ndi umphawi wawo otheratu, anapereka mowolowamanja kwambiri. 3 Motero ndikuchitira umboni kuti anapereka mmene akanathera, ndipo mwinanso kuposera mmene akathera kupereka. Anapereka mosakakamizidwa, 4 ndipo anatipempha motiwumiriza kuti tiwapatse mwayi woti nawonso athandize anthu oyera mtima a ku Yudeya. 5 Iwo anachita moposera mmene ife timayembekezera. Choyamba anadzipereka kwa Ambuye ndipo kenaka kwa ife monga mwa chifuniro cha Mulungu. 6 Choncho tinamupempha Tito kuti atsirize poti nʼkuti atayamba kale ntchito yachisomoyi pakati panu. 7 Popeza pa zinthu zonse munachita bwino, monga pachikhulupiriro, poyankhula, pachidziwitso, pakhama lambiri ndi pachikondi chanu pa ife, onetsetsani kuti muchitenso bwino pachisomo ichi chopereka.
8 Sindikukulamulirani, koma ndikufuna kuona ngati chikondi chanu nʼchoona pofananitsa ndi changu cha anthu ena. 9 Pakuti mukudziwa chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu, kuti ngakhale anali wolemera, koma chifukwa cha inuyo anasanduka wosauka, kuti umphawi wakewo, inuyo mulemere.
10 Ndipo nawa malangizo anga pa zoyenera inu kuchita pa nkhaniyi. Chaka chatha munali oyamba, osati ongofuna kupereka kokha komanso okhala ndi mtima ofuna kupereka. 11 Tsopano tsirizani ntchitoyi, ndipo changu chanu chofunitsitsa kugwira ntchitoyi ndi kuyitsiriza chichitike molingana ndi zimene muli nazo. 12 Ndipo ngati mtima ofunitsitsa ulipo, mphatsoyo imalandiridwa molingana ndi zimene munthuyo ali nazo, osati zimene alibe.
13 Cholinga chathu sikuti tipeputse ena pamene inuyo mukuvutika, koma kuti pakhale kufanana. 14 Zambiri zimene muli nazo pakati panu muthandize nazo osowa, kuti nawonso akadzakhala nazo zambiri adzakuthandizeni pa zosowa zanu. Cholinga nʼkuchita mofanana, 15 monga kwalembedwa kuti, “Iye amene anatola zambiri sizinamutsalireko ndipo amene anatola pangʼono sizinamuchepere.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.