Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
2 Samueli 23:1-7

Mawu Otsiriza a Davide

23 Nawa mawu otsiriza a Davide:

“Mawu a Davide mwana wa Yese,
    mawu a munthu amene wakwezedwa ndi Wammwambamwamba,
munthu wodzozedwa ndi Mulungu wa Yakobo,
    woyimba nyimbo za Israeli:

“Mzimu wa Yehova unayankhula kudzera mwa ine;
    mawu ake anali pakamwa panga.
Mulungu wa Israeli anayankhula,
    Thanthwe la Israeli linati kwa ine:
‘Pamene munthu alamulira anthu mwachilungamo,
    pamene alamulira moopa Mulungu,
amakhala ngati kuwala kwa mmamawa,
    mmawa wopanda mitambo,
monga kuwala pamene mvula yaleka kugwa
    imene imameretsa udzu mʼnthaka.’

“Kodi banja langa silolungama pamaso pa Mulungu?
    Kodi Iye sanachite pangano losatha ndi ine,
    lokonzedwa ndi lotetezedwa mbali zonse?
Kodi sadzakwaniritsa chipulumutso changa,
    ndi kundipatsa chokhumba changa chilichonse?
Koma anthu oyipa ndiwo ayenera kutayidwa kunja ngati minga,
    imene sitengedwa ndi manja.
Aliyense amene wayikhudza mingayo
    amayidula pogwiritsa ntchito chigwandali kapena ndodo ya mkondo;
    nayitentha pa moto.”

Masalimo 132:1-12

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

132 Inu Yehova, kumbukirani Davide
    ndi mavuto onse anapirira.

Iye analumbira kwa Yehova
    ndi kulonjeza kwa Wamphamvu wa Yakobo kuti,
“Sindidzalowa mʼnyumba mwanga
    kapena kugona pa bedi langa:
sindidzalola kuti maso anga agone,
    kapena zikope zanga ziwodzere,
mpaka nditamupezera malo Yehova,
    malo okhala a Wamphamvu wa Yakobo.”

Zoonadi, tinamva za Bokosi la Chipangano ku Efurata,
    tinalipeza mʼminda ya ku Yaara:
“Tiyeni tipite ku malo ake okhalamo;
    tiyeni tikamulambire pa mapazi ake.
‘Dzukani Yehova, ndipo bwerani ku malo anu opumulira,
    Inuyo ndi Bokosi la Chipangano limene limafanizira mphamvu zanu.
Ansembe anu avekedwe chilungamo;
    anthu anu oyera mtima ayimbe nyimbo mwachimwemwe.’ ”

10 Chifukwa cha Davide mtumiki wanu,
    musakane wodzozedwa wanu.

11 Yehova analumbira kwa Davide,
    lumbiro lotsimikizika kuti Iye sadzasintha:
“Mmodzi wa ana ako
    ndidzamuyika pa mpando waufumu;
12 ngati ana ako azisunga pangano langa
    ndi malamulo amene ndiwaphunzitsa,
pamenepo ana awo adzakhala pa mpando
    wako waufumu kwamuyaya ndi muyaya.”

Masalimo 132:13-18

13 Pakuti Yehova wasankha Ziyoni,
    Iye wakhumba kuti akhale malo ake okhalamo:
14 “Awa ndi malo anga opumapo ku nthawi za nthawi;
    ndidzakhala pano pa mpando waufumu, pakuti ndakhumba zimenezi.
15 Ndidzadalitsa mzindawu ndi zinthu zambiri;
    anthu ake osauka ndidzawakhutitsa ndi chakudya.
16 Ndidzaveka ansembe ake chipulumutso,
    ndipo anthu ake oyera mtima adzayimba nthawi zonse nyimbo zachimwemwe.

17 “Pano ndidzachulukitsa mphamvu za Davide
    ndi kuyikapo nyale ya wodzozedwa wanga.
18 Ndidzaveka adani ake manyazi,
    koma chipewa chaufumu pamutu pake chidzakhala chowala.”

Chivumbulutso 1:4-8

Malonje kwa Mipingo Isanu ndi Iwiri

Ndine Yohane,

Kupita ku mipingo isanu ndi iwiri ya mʼchigawo cha Asiya.

Chisomo ndi mtendere kwa inu, kuchokera kwa Iye amene ali, amene analipo ndi amene akubwera ndi kwa mizimu isanu ndi iwiri yokhala patsogolo pa mpando wake waufumu, ndiponso kuchokera kwa Yesu Khristu mboni yokhulupirika, woyamba kuukitsidwa, ndi wolamulira mafumu a dziko lapansi.

Kwa Iye amene amatikonda ndipo watimasula ku machimo athu ndi magazi ake, ndipo watisandutsa mafumu ndi ansembe kuti tizitumikira Mulungu ndi Atate ake. Kwa Iye kukhale ulemerero ndi mphamvu ku nthawi zosatha, Ameni.

“Onani akubwera ndi mitambo,”
    ndipo “Aliyense adzamuona,
ndi amene anamubaya omwe.”
    Ndipo anthu a mitundu yonse ya pa dziko lapansi “adzalira chingʼangʼadza chifukwa cha Iye.”
Zidzakhaladi momwemo, Ameni.

“Ine ndine Alefa ndi Omega,” akutero Ambuye Mulungu Wamphamvuzonseyo “amene muli, amene munalipo, ndi amene mudzakhalapo.”

Yohane 18:33-37

33 Kenaka Pilato anapita mʼkati mwa nyumba yaufumu nayitanitsa Yesu, ndipo anamufunsa kuti, “Kodi iwe ndi mfumu ya Ayuda?”

34 Yesu anafunsa kuti, “Kodi amenewo ndi maganizo anu wokha? Kapena kuti ena anakuwuzani za Ine?”

35 Pilato anayankha kuti, “Kodi iwe ukuganiza kuti ine ndine Myuda? Ndi anthu ako ndi akulu a ansembe ako amene akupereka iwe kwa ine. Kodi walakwanji?”

36 Yesu anati, “Ufumu wanga si wa dziko lapansi lino. Ukanakhala wa pansi pano, antchito anga akanachita nkhondo kulepheretsa Ayuda kundigwira. Koma tsopano ufumu wanga ndi wochokera kumalo ena.”

37 Pilato anati, “Kani ndiwe mfumu!”

Yesu anayankha kuti, “Inu mwalondola ponena kuti, Ine ndine mfumu. Kunena zoona, Ine ndinabadwa chifukwa cha chimenechi, ndipo nʼchifukwa chake ndinabwera mʼdziko lapansi, kudzachitira umboni choonadi. Aliyense amene ali mbali yachoonadi amamvera mawu anga.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.