Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Salimo la Davide.
28 Kwa Inu ine ndiyitana, Yehova ndinu Thanthwe langa;
musakhale osamva kwa ine.
Pakuti mukapitirira kukhala chete,
ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
2 Imvani kupempha chifundo kwanga
pomwe ndikuyitana kwa Inu kuti mundithandize,
pomwe ndikukweza manja anga
kuloza ku malo anu oyeretsetsa.
3 Musandikokere kutali pamodzi ndi anthu oyipa,
pamodzi ndi iwo amene amachita zoyipa,
amene amayankhula mwachikondi ndi anzawo
koma akusunga chiwembu mʼmitima mwawo.
4 Muwabwezere chifukwa cha zochita zawo
ndi ntchito zawo zoyipa;
abwezereni chifuwa cha zimene manja awo achita
ndipo mubweretse pa iwo zimene zowayenera.
5 Popeza iwowo sakhudzidwa ndi ntchito za Yehova,
ndi zimene manja ake anazichita,
Iye adzawakhadzula
ndipo sadzawathandizanso.
6 Matamando apite kwa Yehova,
popeza Iye wamva kupempha chifundo kwanga.
7 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi chishango changa;
mtima wanga umadalira Iye, ndipo Ine ndathandizidwa.
Mtima wanga umalumphalumpha chifukwa cha chimwemwe
ndipo ndidzayamika Iye mʼnyimbo.
8 Yehova ndi mphamvu ya anthu ake,
linga la chipulumutso kwa wodzozedwa wake.
9 Pulumutsani anthu anu ndipo mudalitse cholowa chanu;
mukhale mʼbusa wawo ndipo muwakweze kwamuyaya.
9 Anthu akuti, “Chifukwa cha zimenezi chilungamo chatitalikira;
ndipo chipulumutso sichitifikira.
Timafunafuna kuwala koma timangopeza mdima okhaokha;
tinayembekezera kuyera koma timayenda mu mdima wandiweyani.
10 Timapapasapapasa khoma ngati munthu wosaona,
kuyangʼanayangʼana njira ngati anthu opanda maso.
Timapunthwa dzuwa lili paliwombo ngati kuti ndi usiku;
timakhala pansi mu mdima ngati anthu akufa.
11 Tonse timabangula ngati zimbalangondo:
Timalira modandaula ngati nkhunda.
Tinayembekezera kuweruza kolungama; koma sitikupeza.
Timayembekezera chipulumutso koma chimakhala nafe kutali.”
12 Pakuti zolakwa zathu nʼzochuluka pamaso panu,
ndipo machimo athu akutsutsana nafe.
Zolakwa zathu zili ndi ife nthawi zonse
ndipo tikuvomereza machimo athu:
13 Tawukira ndi kumukana Yehova.
Tafulatira Mulungu wathu,
pa kupondereza anzathu ndi kupandukira Yehova,
ndi pa kuyankhula mabodza amene tawaganiza mʼmitima mwathu.
14 Motero kuweruza kolungama kwalekeka
ndipo choonadi chili kutali ndi ife;
kukhulupirika sikukupezekanso mʼmabwalo a milandu,
ndipo kuona mtima sikukupezekanso mʼmenemo.
15 Choonadi sichikupezeka kumeneko,
ndipo wina akakana kuchita nawo zoyipa amapeza mavuto.
Yehova anaziona zimenezi ndipo zinamunyansa
kuti panalibe chiweruzo cholungama.
16 Yehova anaona kuti panalibe ndi mmodzi yemwe,
Iye anadabwa kuti panalibe ndi mmodzi yemwe woti nʼkupembedzera;
Choncho mphamvu zake zomwe zinamuthandiza,
ndipo anadzilimbitsa ndi kulungama kwake;
17 Iye anavala chilungamo ngati chovala chachitsulo chapachifuwa,
ndipo kumutu kwake amavala chipewa chachipulumutso;
anavala kulipsira ngati chovala
ndipo anadzikuta ndi mkwiyo ngati chofunda.
18 Iye adzawabwezera chilango adani a anthu ake
molingana ndi zimene anachita,
adzaonetsa ukali kwa adani ake
ndi kubwezera chilango odana naye.
Adzalanga ngakhale okhala mayiko akutali.
19 Choncho akadzabwera ngati madzi
oyendetsedwa ndi mphepo yamphamvu yamkuntho.
Anthu onse kuyambira kumadzulo mpaka kummawa
adzaopa dzina la Yehova ndi ulemerero wake.
2 Choncho, lekani zoyipa zonse, chinyengo chilichonse, chiphamaso, nsanje ndi kusinjirira kulikonse. 2 Monga makanda obadwa kumene amalirira mkaka, inunso muzilakalaka mkaka weniweni wauzimu, kuti mukule ndi kukufikitsani ku chipulumutso chanu, 3 pakuti tsopano mwalawadi kuti Ambuye ndi wabwino.
Mwala wa Moyo ndi Anthu Osankhidwa
4 Pamene mukubwera kwa Iye, amene ndi Mwala wa moyo, umene anthu anawukana, koma Mulungu anawusankha kuti ndi wa mtengowapatali, 5 inunso, mukhale ngati miyala ya moyo yoti Mulungu amangire nyumba yake yauzimu kuti mukhale ansembe opatulika, opereka nsembe zauzimu zovomerezeka ndi Mulungu mwa Yesu Khristu. 6 Pakuti mʼMalemba mwalembedwa kuti,
“Taonani, ndikuyika mwala wa maziko mu Ziyoni,
wosankhika ndi wamtengowapatali.
Amene akhulupirira Iye
sadzachititsidwa manyazi.”
7 Tsono kwa inu okhulupirira, mwalawo ndi wamtengowapatali. Koma kwa amene sakhulupirira,
“Mwala umene amisiri anawukana
wasanduka mwala wa maziko,
8 ndi
“Mwala wopunthwitsa anthu
ndiponso thanthwe limene limagwetsa anthu.”
Iwo amapunthwa chifukwa samvera uthenga, pakuti ichi ndiye chinali chifuniro cha Mulungu pa iwo.
9 Koma inu ndinu anthu osankhidwa ndi Mulungu, ansembe achifumu, mtundu woyera mtima, anthu ake enieni a Mulungu, munasankhidwa kuti mulalikire za ntchito zamphamvu za Iye amene anakuyitanani kuti mutuluke mu mdima ndi kulowa mʼkuwunika kwake kodabwitsa. 10 Kale simunali anthu ake, koma tsopano ndinu anthu a Mulungu. Kale simunalandire chifundo, koma tsopano mwalandira chifundo.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.