Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 39

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kwa Yedutuni. Salimo la Davide.

39 Ndinati, “Ndidzasamalira njira zanga
    ndipo ndidzasunga lilime langa kuti ndisachimwe;
ndidzatseka pakamwa panga ndi chitsekerero
    nthawi yonse imene woyipa ali pamaso panga.”
Koma pamene ndinali chete
    osanena ngakhale kanthu kalikonse kabwino
    mavuto anga anachulukirabe.
Mtima wanga unatentha mʼkati mwanga,
    ndipo pamene ndinkalingalira, moto unayaka;
    kenaka ndinayankhula ndi lilime langa:

“Yehova ndionetseni mathero a moyo wanga
    ndi chiwerengero cha masiku anga;
    mundidziwitse kuti moyo wanga ndi wosakhalitsa motani.
Inu mwachititsa kuti masiku anga akhale ochepa kwambiri,
    kutalika kwa zaka zanga ndi kopanda phindu pamaso panu;
    moyo wa munthu aliyense ndi waufupi.
            Sela
Munthu ali ngati chithunzithunzi chake pamene akuyenda uku ndi uku:
    Iye amangovutika koma popanda phindu;
    amadzikundikira chuma, osadziwa kuti chidzakhala chayani.

“Koma tsopano Ambuye kodi ndifunanso chiyani?
    Chiyembekezo changa chili mwa Inu.
Pulumutseni ku zolakwa zanga zonse;
    musandisandutse chonyozeka kwa opusa.
Ine ndinali chete; sindinatsekule pakamwa panga
    pakuti Inu ndinu amene mwachita zimenezi.
10 Chotsani mkwapulo wanu pa ine;
    ndagonjetsedwa ndi nkhonya ya dzanja lanu.
11 Inu mumadzudzula ndi kulanga anthu chifukwa cha tchimo lawo;
    mumawononga chuma chawo monga njenjete;
    munthu aliyense ali ngati mpweya.
            Sela

12 “Imvani pemphero langa Inu Yehova,
    mverani kulira kwanga kopempha thandizo;
    musakhale chete pamene ndikulirira kwa Inu,
popeza ndine mlendo wanu wosakhalitsa;
    monga anachitira makolo anga onse.
13 Musandiyangʼane mwaukali, choncho ndidzatha kusangalala
    ndisanafe ndi kuyiwalika.”

Yobu 32

Mawu a Elihu

32 Tsono anthu atatuwa analeka kumuyankha Yobu, chifukwa chakuti iyeyo ankadziona kuti ndi wolungama. Koma Elihu, mwana wa Barakeli, wa fuko la Buzi, wa banja la Ramu, anapsera mtima kwambiri Yobu chifukwa choti Yobuyo anakana kuvomera kuti anachimwa ndi kuti Mulungu anakhoza pomulanga. Anapseranso mtima abwenzi ake atatu aja chifukwa sanapeze njira yomutsutsira Yobu, ngakhale iwo anamupeza kuti anali wolakwa. Tsono Elihu anadikira kuti ayankhule ndi Yobu chifukwa choti abwenziwo anali akuluakulu kupambana iyeyo. Koma Elihu ataona kuti anthu atatuwo analibe mawu oti ayankhulenso, iye anapsa mtima.

Choncho Elihu mwana wa Barakeli wa fuko la Buzi anati:

“Ine ndine wamngʼono,
    inuyo ndinu akuluakulu,
nʼchifukwa chake ndimaopa,
    ndimachita mantha kuti ndikuwuzeni zimene ndimadziwa.
Ndimaganiza kuti, ‘Ayambe ndi akuluakulu kuyankhula;
    anthu amvulazakale ndiwo amaphunzitsa nzeru.’
Koma mzimu wa Mulungu mwa munthu,
    mpweya wa Wamphamvuzonse, ndi umene umapereka nzeru zomvetsa zinthu.
Si okalamba amene ali ndi nzeru,
    si amvulazakale okha amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu zimene zili zoyenera.

10 “Nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Mvereni;
    inenso ndikukuwuzani zimene ndikuzidziwa.’
11 Ndadikira nthawi yonseyi,
    ndimamvetsera mwachidwi zimene mumayankhula,
pamene mumafunafuna mawu oti muyankhule,
12     ineyo ndinakumvetseranidi.
Koma palibe ndi mmodzi yemwe wa inu amene anatsutsa Yobu;
    palibe aliyense wa inu amene anamuyankha mawu ake.
13 Musanene kuti, ‘Ife tapeza nzeru;
    Mulungu ndiye amutsutse, osati munthu.’
14 Koma Yobu sanayankhule motsutsana ndi ine,
    ndipo ine sindimuyankha monga mmene inu mwamuyankhira.

15 “Iwo asokonezeka ndipo alibe choti ayankhulenso;
    mawu awathera.
16 Kodi ine ndidikire chifukwa iwo sakuyankhula tsopano,
    pakuti angoyima phee wopanda yankho?
17 Inenso ndiyankhulapo tsopano;
    nanenso ndinena zimene ndikudziwa.
18 Pakuti ndili nawo mawu ambiri,
    ndipo mtima wanga ukundikakamiza;
19 mʼkati mwanga ndili ngati botolo lodzaza ndi vinyo,
    ngati matumba a vinyo watsopano amene ali pafupi kuphulika.
20 Ndiyenera kuyankhula kuti mtima utsike;
    ndiyenera kutsekula pakamwa panga ndi kuyankha.
21 Sindidzakondera munthu wina aliyense,
    kapena kuyankhula zoshashalika,
22 pakuti ndikanakhala wa luso loyankhula moshashalika,
    Mlengi wanga akanandilanga msanga.”

Luka 16:19-31

Za Munthu Wachuma ndi Lazaro

19 “Panali munthu wachuma amene ankavala zovala zofiirira za mtengowapatali ndipo ankakhala moyo wachisangalalo tsiku lililonse. 20 Pa khomo la mpanda wake ankagonekapo munthu wopempha wotchedwa Lazaro, wazilonda thupi lonse 21 ndipo ankafunitsitsa atadya zomwe zinkagwa pansi kuchokera pamene munthu wolemerayo amadyerapo. Agalu ankabweranso ndi kumanyambita zilonda zake.

22 “Nthawi inafika imene wopemphayo anamwalira ndipo angelo anamunyamula nakamuyika mʼmanja mwa Abrahamu. Munthu wolemerayo anamwaliranso ndipo anayikidwa mʼmanda. 23 Ali mʼgehena kuzunzika, anakweza maso ake ndipo anaona Abrahamu ali ndi Lazaro pambali pake. 24 Ndipo anafuwula kwa iye kuti, ‘Abambo Abrahamu, mundimvere chisoni ine ndipo mutumeni Lazaroyo kuti aviyike msonga ya chala chake mʼmadzi kuti aziziritse lilime langa, chifukwa ndikumva ululu mʼmoto muno.’

25 “Koma Abrahamu anayankha kuti, ‘Mwanawe kumbukira kuti nthawi yamoyo wako unalandira zinthu zako zabwino, pamene Lazaro analandira zinthu zoyipa, koma tsopano akusangalatsidwa kuno ndipo iwe uli mʼmazunzo. 26 Ndipo kuwonjezera pa zonsezi, pakati pa inu ndi ife pali chiphompho chachikulu chimene chinayikidwa, kotero kuti amene akufuna kubwera kumeneko sangathe, kapena palibe amene angawoloke kuchokera kumeneko kudzafika kuno.’

27 “Iye anayankha kuti, ‘Ndipo ndikupemphani inu, abambo, mutumeni Lazaro ku nyumba ya abambo anga, 28 pakuti ine ndili ndi abale asanu. Lolani iye akawachenjeze kotero kuti asadzabwere kumalo ano amazunzo.’

29 “Abrahamu anayankha kuti, ‘Ali ndi Mose ndi Aneneri; aleke amvere iwo.’

30 “Iye anati, ‘Ayi, bambo Abrahamu, koma ngati wina ochokera kwa akufa adzapita kwa iwo, adzatembenuka mtima.’

31 “Anati kwa iye, ‘Ngati iwo samvera Mose ndi Aneneri, sadzakhulupirira ngakhale wina atauka kwa akufa.’ ”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.