Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kwa Yedutuni. Salimo la Davide.
39 Ndinati, “Ndidzasamalira njira zanga
ndipo ndidzasunga lilime langa kuti ndisachimwe;
ndidzatseka pakamwa panga ndi chitsekerero
nthawi yonse imene woyipa ali pamaso panga.”
2 Koma pamene ndinali chete
osanena ngakhale kanthu kalikonse kabwino
mavuto anga anachulukirabe.
3 Mtima wanga unatentha mʼkati mwanga,
ndipo pamene ndinkalingalira, moto unayaka;
kenaka ndinayankhula ndi lilime langa:
4 “Yehova ndionetseni mathero a moyo wanga
ndi chiwerengero cha masiku anga;
mundidziwitse kuti moyo wanga ndi wosakhalitsa motani.
5 Inu mwachititsa kuti masiku anga akhale ochepa kwambiri,
kutalika kwa zaka zanga ndi kopanda phindu pamaso panu;
moyo wa munthu aliyense ndi waufupi.
Sela
6 Munthu ali ngati chithunzithunzi chake pamene akuyenda uku ndi uku:
Iye amangovutika koma popanda phindu;
amadzikundikira chuma, osadziwa kuti chidzakhala chayani.
7 “Koma tsopano Ambuye kodi ndifunanso chiyani?
Chiyembekezo changa chili mwa Inu.
8 Pulumutseni ku zolakwa zanga zonse;
musandisandutse chonyozeka kwa opusa.
9 Ine ndinali chete; sindinatsekule pakamwa panga
pakuti Inu ndinu amene mwachita zimenezi.
10 Chotsani mkwapulo wanu pa ine;
ndagonjetsedwa ndi nkhonya ya dzanja lanu.
11 Inu mumadzudzula ndi kulanga anthu chifukwa cha tchimo lawo;
mumawononga chuma chawo monga njenjete;
munthu aliyense ali ngati mpweya.
Sela
12 “Imvani pemphero langa Inu Yehova,
mverani kulira kwanga kopempha thandizo;
musakhale chete pamene ndikulirira kwa Inu,
popeza ndine mlendo wanu wosakhalitsa;
monga anachitira makolo anga onse.
13 Musandiyangʼane mwaukali, choncho ndidzatha kusangalala
ndisanafe ndi kuyiwalika.”
Mawu a Yobu
26 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 “Wamuthandizadi munthu wopanda mphamvu!
Walimbitsadi dzanja la munthu wofowoka!
3 Wapereka malangizo kwa munthu amene alibe nzeru!
Ndipotu waonetsadi nzeru zochuluka!
4 Kodi wakuthandiza ndani kuti uyankhule mawu awa?
Ndipo ndi mzimu wa yani umene unayankhula pakamwa pako?
5 “Mizimu ya anthu akufa ikunjenjemera pansi pa madzi,
ndi zonse zokhala mʼmadzimo.
6 Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu;
chiwonongeko ndi chosaphimbidwa.
7 Mulungu anayala thambo la kumpoto pa phompho;
Iye anakoloweka dziko lapansi mʼmalo mwake pamene panali popanda nʼkanthu komwe.
8 Amasunga madzi ambiri mʼmitambo yake,
koma mitamboyo siphulika chifukwa cha kulemera kwa madziwo.
9 Iye amaphimba mwezi wowala,
amawuphimba ndi mitambo yake.
10 Mulungu anawalembera madzi malire wonga uta,
kukhala malire pakati pa kuwunika ndi mdima.
11 Mizati yochirikiza mitambo yakumwamba imanjenjemera,
ndi kudabwa pa kudzudzula kwake.
12 Ndi mphamvu zake anatontholetsa nyanja;
ndi nzeru zake anakantha chirombo cha mʼmadzi chija chotchedwa Rahabe.
13 Ndi mpweya wake anayeretsa zamumlengalenga,
dzanja lake linapha chinjoka chothawa chija.
14 Zimenezi ndi pangʼono chabe mwa ntchito yake;
tingomva pangʼono za Iye ngati kunongʼona!
Kodi ndani angathe kudziwa kukula kwa mphamvu zake?”
Gulu Lalikulu la Anthu Ovala Zoyera
9 Zitatha izi ndinayangʼana patsogolo panga ndipo ndinaona gulu lalikulu la anthu loti munthu sangathe kuliwerenga lochokera dziko lililonse, fuko lililonse, mtundu wa anthu uliwonse ndi chiyankhulo chilichonse, atayima patsogolo pa mpando waufumu, pamaso pa Mwana Wankhosa. Iwo anali atavala mikanjo yoyera ndi kunyamula nthambi za kanjedza mʼmanja mwawo. 10 Ndipo ankafuwula mokweza kuti:
“Chipulumutso chimachokera kwa Mulungu wathu,
wokhala pa mpando waufumu
ndi kwa Mwana Wankhosa.”
11 “Angelo onse anayimirira kuzungulira mpando waufumu uja, kuzunguliranso akuluakulu aja ndi zamoyo zinayi zija. Angelo aja anadzigwetsa pansi chafufumimba patsogolo pa mpando waufumu napembedza Mulungu. 12 Iwo anati,
“Ameni!
Matamando ndi ulemerero,
nzeru, mayamiko, ulemu,
ulamuliro ndi mphamvu
zikhale kwa Mulungu wathu kunthawi zanthawi,
Ameni!”
13 Pamenepo mmodzi wa akuluakulu aja anandifunsa kuti, “Kodi avala mikanjo yoyerawa ndani ndipo akuchokera kuti?”
14 Ine ndinayankha kuti, “Mbuye wanga mukudziwa ndinu.”
Tsono iye anandiwuza kuti, “Amenewa ndi amene anatuluka mʼmazunzo aakulu aja. Anachapa mikanjo yawo naziyeretsa mʼmagazi a Mwana Wankhosa. 15 Nʼchifukwa chake,
“iwowa ali patsogolo pa mpando waufumu wa Mulungu
ndipo akutumikira usana ndi usiku mʼNyumba ya Mulungu;
ndipo Iye wokhala pa mpando waufumu
adzawaphimba ndi tenti yake.
16 ‘Iwowa sadzamvanso njala,
sadzamvanso ludzu,
dzuwa kapena kutentha kulikonse
sikudzawawotcha.’
17 Pakuti Mwana Wankhosa amene ali pakati pa mpando waufumu
adzakhala mʼbusa wawo.
‘Iye adzawatsogolera ku akasupe a madzi amoyo.’
‘Ndipo Mulungu adzawapukuta misozi yonse mʼmaso mwawo.’ ”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.