Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 55:1-15

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya Davide. Pa zoyimbira za zingwe.

55 Mvetserani pemphero langa, Inu Mulungu,
    musakufulatire kupempha kwanga,
    mverani ndipo mundiyankhe.
Maganizo anga akundisautsa ndipo ndathedwa nzeru
    chifukwa cha mawu a adani anga,
    chifukwa cha kupondereza kwa anthu oyipa;
pakuti andidzetsera masautso
    ndipo akundizunza mu mkwiyo wawo.

Mtima wanga ukupweteka mʼkati mwanga;
    mantha a imfa andigwera.
Mantha ndi kunjenjemera zandizinga;
    mantha aakulu andithetsa nzeru.
Ndinati, “Ndithu, ndikanakhala ndi mapiko ankhunda!
    Ndikanawulukira kutali ndi kukapuma.
Ndikanathawira kutali
    ndi kukakhala mʼchipululu.
Ndikanathamangira kumalo anga a chitetezo;
    kutali ndi mphepo yaukali ndi yamkuntho.”

Sokonezani maganizo a oyipa, Inu Ambuye, tsutsani mawu awo;
    pakuti ine ndikuona chiwawa ndi mkangano mu mzinda.
10 Usana ndi usiku iwo akuzungulirazungulira pa makoma ake;
    nkhwidzi ndi kuzunza kuli mʼkati mwake.
11 Mphamvu zowononga zili pa ntchito mu mzinda;
    kuopseza ndi mabodza sizichoka mʼmisewu yake.

12 Akanakhala mdani akundinyoza, ine
    ndikanapirira;
akanakhala mdani akudzikweza yekha kutsutsana nane,
    ndikanakabisala.
13 Koma iweyo mnzanga, mnzanga woyenda naye,
    bwenzi langa la pondaapanʼpondepo, ndi amene ukuchita zimenezi.
14 Mnzanga amene nthawi ina tinkasangalala
    pa chiyanjano chokoma ku nyumba ya Mulungu.

15 Mulole imfa itenge adani anga mwadzidzidzi;
    alowe mʼmanda ali amoyo
    pakuti choyipa chili pakati pawo.

Yobu 8

Mawu a Bilidadi

Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,

“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti?
    Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama?
    Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu,
    Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
Koma utayangʼana kwa Mulungu,
    ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima
    ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako
    ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa
    koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.

“Funsa kwa anthu amvulazakale
    ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse,
    ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera?
    Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho?
    Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula;
    zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu;
    ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 Kulimba mtima kwake kumafowoka;
    zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka;
    amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa,
    nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 mizu yake imayanga pa mulu wa miyala
    ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo,
    pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 Ndithudi chomeracho chimafota,
    ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.

20 “Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa
    kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete
    ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 Adani ako adzachita manyazi,
    ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

1 Akorinto 7:1-9

Ukwati

Tsopano pa zinthu zomwe munandilembera nʼkwabwino kuti munthu asakwatire. Koma chifukwa choti chigololo chawanda, mwamuna aliyense akhale naye mkazi wakewake ndipo mkazi aliyense akhale naye mwamuna wakewake. Mwamuna akwaniritse udindo wake wa pa banja kwa mkazi wake, ndipo chimodzimodzi mkazi kwa mwamuna wake. Thupi la mkazi wokwatiwa si la iye mwini yekha koma ndi la mwamuna wakenso. Momwemonso, thupi la mwamuna si la iye mwini yekha koma ndi la mkazi wakenso. Musamakanizane, pokhapokha mutagwirizana awiri kuti mwakanthawi mudzipereke kumapemphero. Kenaka mukhalirenso pamodzi kuopa kuti Satana angakuyeseni chifukwa cholephera kudziretsa. Ndikunena zimenezi mokulolani chabe osati mokulamulani. Ine ndikanakonda anthu akanakhala ngati ine. Koma poti munthu aliyense ali ndi mphatso yakeyake yochokera kwa Mulungu, wina mphatso yake, wina yakenso.

Tsono kwa osakwatira onse, ndi akazi amasiye ndikuti, ndi bwino kwa iwo kukhala osakwatira monga mmene ndilili inemu. Koma ngati sangathe kudziretsa, akwatire, popeza ndi bwino kukwatira kusiyana ndi kudzizunza ndi chilakolako.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.