Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 26

Salimo la Davide.

26 Weruzeni Inu Yehova
    pakuti ndakhala moyo wosalakwa.
Ndadalira Yehova
    popanda kugwedezeka.
Patseni mayeso, Inu Yehova ndipo ndiyeseni,
    santhulani mtima wanga ndi maganizo anga;
pakuti chikondi chanu chili pamaso panga nthawi zonse,
    ndipo ndimayenda mʼchoonadi chanu nthawi zonse.
Ine sindikhala pansi pamodzi ndi anthu achinyengo,
    kapena kufunsa nzeru kwa achiphamaso.
Ndimanyansidwa ndi msonkhano wa anthu ochita zoyipa
    ndipo ndimakana kukhala pansi pamodzi ndi oyipa.
Ndimasamba mʼmanja mwanga kuonetsa kusalakwa kwanga
    ndi kupita kukatumikira pa guwa lanu la nsembe, Inu Yehova,
kulengeza mofuwula za matamando anu
    ndi kuwuza onse za ntchito zanu zodabwitsa.
Ndimakonda Nyumba imene Inu Yehova mumakhalamo,
    malo amene ulemerero wanu umapezekako.

Musachotse moyo wanga pamodzi ndi ochimwa,
    moyo wanga pamodzi ndi anthu akupha anzawo,
10 amene mʼmanja mwawo muli ndondomeko zoyipa,
    dzanja lawo lamanja ladzaza ndi ziphuphu.
11 Koma ine ndimakhala moyo wosalakwa;
    mu msonkhano wa anthu anu ndidzatamanda Yehova.

12 Ndayima pa malo wopanda zovuta
    ndipo ndidzatamanda Yehova mu msonkhano waukulu.

Yobu 4

Mawu a Elifazi

Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,

“Ngati wina atakuyankha, kodi ungakhumudwe?
    Koma ndani angakhale chete wosayankhula?
Taganiza momwe iwe walangizira anthu ambiri,
    momwe walimbitsira anthu ofowoka.
Mawu ako analimbitsa anthu ofuna kugwa;
    unachirikiza anthu wotha mphamvu.
Koma tsopano mavuto akufikira ndipo wataya mtima,
    zakukhudza ndipo uli ndi mantha.
Kodi kuopa Mulungu kwako sindiko kulimbika mtima kwako?
    Ndipo moyo wako wosalakwa ndiye chiyembekezo chako?

“Ganiza bwino tsopano: Kodi munthu wosalakwa anawonongekapo nʼkale lonse?
    Nʼkuti kumene munthu wolungama mtima anaphedwa?
Monga ndaonera ine, anthu amene amatipula zoyipa,
    ndi iwo amene amadzala mavuto, amakolola zomwezo.
Iwo amaphedwa ndi mpweya wa Mulungu;
    amawonongeka ndi mpweya waukali wa mkwiyo wake.
10 Mikango imabangula ndi kulira,
    komabe mano a mikango yamphamvu amathyoledwa.
11 Mkango umafa chifukwa chosowa nyama,
    ndipo ana amkango amamwazikana.

12 “Mawu anabwera kwa ine mwamseri,
    makutu anga anamva kunongʼona kwake.
13 Mʼkati mwa maloto ochititsa mantha usiku,
    nthawi imene anthu amagona tulo tofa nato,
14 ndinagwidwa ndi mantha, ndi kuyamba kunjenjemera
    ndipo mafupa anga onse anaweyeseka.
15 Pamenepo mzimu unadutsa pamaso panga,
    ndipo ubweya wa pa thupi langa unayima kuti njoo.
16 Chinthucho chinayimirira
    koma sindinathe kuzindikira kuti chinali chiyani.
Chinthu chinayima patsogolo panga,
    kunali zii ndipo ndinamva mawu akuti,
17 ‘Kodi munthu angathe kukhala wolungama kupambana Mulungu?
    Kodi munthu angathe kukhala wangwiro kupambana Mlengi wake?
18 Ngati Mulungu sakhulupirira atumiki ake omwe,
    ngati Iye amawapeza angelo ake ndi cholakwa,
19 nanga kuli bwanji ndi iwo amene amakhala mʼnyumba zadothi,
    amene maziko awo ndi fumbi,
    amene amathudzuka mosavuta ngati kadziwotche!
20 Mmawa ali moyo, pofika madzulo afa;
    mwakachetechete, amawonongeka kwamuyaya.
21 Kodi zonse zimene ali nazo sizimatheratu,
    kotero kuti amafa osadziwa nʼkanthu komwe?’

Aroma 8:1-11

Moyo Watsopano mwa Khristu

Choncho, tsopano amene ali mwa Khristu Yesu alibe mlandu owatsutsa chifukwa mwa Khristu Yesu, lamulo la Mzimu Woyera amene amapereka moyo, lawamasula ku lamulo la tchimo ndi la imfa. Pakuti zimene Malamulo sanathe kuzichita, popeza anali ofowoka chifukwa cha khalidwe lathu la uchimo, Mulungu anazichita potumiza Mwana wake mʼchifanizo cha munthu ochimwa kuti akhale nsembe yauchimo. Ndipo Iye anagonjetsa tchimo mʼthupi la munthu, ndi cholinga chakuti chilungamo chofunikira cha lamulo chikwaniritsidwe kwathunthu mwa ife amene sitikhala monga mwachikhalidwe chathu cha uchimo koma mwa Mzimu.

Pakuti anthu amene amakhala monga mwa makhalidwe oyipa a thupi amayika malingaliro awo pa zinthu zathupi. Koma amene amakhala monga mwa Mzimu amayika malingaliro awo pa zinthu za Mzimu. Kuyika mtima pa zathupi ndi imfa koma kuyika mtima pa za Mzimu ndi moyo ndi mtendere. Pakuti mtima umene wakhazikika pa zathupi ndi wodana ndi Mulungu. Sunagonjere lamulo la Mulungu ndipo sungathe kutero. Ndipo anthu amene amalamulidwa ndi khalidwe lauchimo sangathe kukondweretsa Mulungu.

Koma inu simulamulidwanso ndi khalidwe lanu lauchimo koma ndi Mzimu ngati Mzimu wa Mulungu akhaladi mwa inu. Koma ngati munthu aliyense alibe Mzimu wa Khristu, iyeyu si wa Khristu. 10 Ndipo ngati Khristu ali mwa inu, thupi lanu ndi lakufa chifukwa cha uchimo, koma mzimu wanu ndi wamoyo chifukwa cha chilungamo. 11 Ndipo ngati Mzimu wa Mulungu amene anaukitsa Yesu kwa akufa akhala mwa inu, Iyeyo amene anaukitsa Khristu kwa akufa adzapatsanso moyo matupi anu amene amafa kudzera mwa Mzimu wake amene amakhala mwa inu.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.