Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.
128 Odala ndi onse amene amaopa Yehova,
amene amayenda mʼnjira zake.
2 Udzadya chipatso cha ntchito yako;
madalitso ndi chuma zidzakhala zako.
3 Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka
mʼkati mwa nyumba yako;
ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi
kuzungulira tebulo lako.
4 Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa
amene amaopa Yehova.
5 Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni
masiku onse a moyo wako;
uwone zokoma za Yerusalemu,
6 ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako.
Mtendere ukhale ndi Israeli.
27 Usamanyadire za mawa,
pakuti sudziwa zimene zidzachitike pa tsikulo.
2 Munthu wina akutamande, koma osati wekha;
mlendo akakutamanda, ndiponi koma osati ndi pakamwa pako.
3 Mwala ndi wolemera ndipo mchenganso ndi wolemera kwambiri,
koma makani a chitsiru ndi oposa zonsezo kulemera kwake.
4 Mkwiyo umadzetsa nkhanza ndipo kupsa mtima kumachititsa zoopsa.
Koma nsanje imachita zoopsa zopambana.
5 Kudzudzula munthu poyera nʼkwabwino
kuposa chikondi chobisika.
6 Munthu amene amakukonda ngakhale akupweteke zili bwino,
koma mdani wako amakupsompsona mwachinyengo.
7 Iye amene wakhuta amayipidwa ndi chisa cha uchi,
koma kwa munthu wanjala ngakhale chimene chili chowawa chimamukomera.
8 Munthu amene wasochera ku nyumba kwake,
ali monga mbalame imene yasochera pa chisa chake.
9 Mafuta ndi zonunkhira zimasangalatsa mtima,
ndipo kukoma mtima kwa bwenzi kwagona pa malangizo ake.
10 Usasiye bwenzi lako ndiponso bwenzi la abambo ako,
ndipo usapite ku nyumba ya mʼbale wako pamene wakumana ndi mavuto;
mnzako wokhala naye pafupi amaposa mʼbale wako wokhala kutali.
11 Mwana wanga, khala wanzeru, ndipo ukondweretse mtima wanga;
pamenepo ine ndidzatha kuyankha aliyense amene amandinyoza.
12 Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala,
koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amakumana ndi mavuto.
13 Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole;
ngati chigwiriro chifukwa waperekera chikole mlendo wosadziwika.
14 Ngati munthu apatsa mnzake moni mofuwula mmamawa kwambiri,
anthu adzamuyesa kuti akutemberera.
15 Mkazi wolongolola ali ngati
mvula yamvumbi.
16 Kumuletsa mkazi wotereyu zimenezi zili ngati kuletsa mphepo
kapena kufumbata mafuta mʼdzanja.
17 Chitsulo chimanoledwa ndi chitsulo chinzake,
chomwechonso munthu amanoledwa ndi munthu mnzake.
18 Amene amasamalira mtengo wamkuyu adzadya zipatso zake,
ndipo iye amene amasamalira mbuye wake adzalandira ulemu.
19 Monga momwe nkhope imaonekera mʼmadzi,
chomwechonso mtima wa munthu umadziwika ndi ntchito zake.
20 Manda sakhuta,
nawonso maso a munthu sakhuta.
21 Siliva amasungunulira mu uvuni ndipo golide mʼngʼanjo,
chomwechonso munthu amadziwika ndi zomwe akudzitamandira nazo.
22 Ngakhale utakonola chitsiru mu mtondo
ndi musi ngati chimanga,
uchitsiru wakewo sudzachoka.
23 Uzidziwe bwino nkhosa zako momwe zilili.
Kodi usamalire bwino ziweto zako?
24 Paja chuma sichikhala mpaka muyaya,
ndipo ufumu sukhala mpaka mibado yonse.
25 Pamene udzu watha, msipu nʼkumera;
ndipo atatuta udzu wa ku mapiri,
26 ana ankhosa adzakupatsani chovala
ndipo pogulitsa mbuzi mudzapeza ndalama yogulira munda.
27 Mudzakhala ndi mkaka wambuzi wambiri
kuti muzidya inuyo ndi banja lanu
ndi kudyetsa antchito anu aakazi.
8 Sendezani kufupi ndi Mulungu ndipo Iye adzasendeza kwa inu. Sambani mʼmanja mwanu, inu anthu ochimwa. Yeretsani mitima yanu, inu anthu okayikira. 9 Chitani chisoni chifukwa cha zimene mwachita, lirani misozi. Kuseka kwanu kusanduke kulira, ndipo chimwemwe chanu chisanduke chisoni. 10 Dzichepetseni pamaso pa Ambuye ndipo Iye adzakukwezani.
11 Abale musamanenane. Aliyense wonenera zoyipa mʼbale wake kapena kumuweruza, akusinjirira ndi kuweruza Malamulo. Pamene muweruza malamulo, ndiye kuti simukusunga malamulowo, koma mukuwaweruza. 12 Pali mmodzi yekha Wopereka Malamulo ndi Woweruza. Ndiye amene akhoza kupulumutsa ndi kuwononga. Kodi ndiwe yani kuti uziweruza mnzako?
Kunyadira za Mawa
13 Tsono tamverani, inu amene mumati, “Lero kapena mawa tipita ku mzinda wakutiwakuti, tikatha chaka chimodzi tikuchita malonda ndi kupanga ndalama.” 14 Chifukwa chiyani mukutero? Inu simukudziwa zimene ziti zichitike mawa. Kodi moyo wanu ndi wotani? Inu muli ngati nkhungu imene imangooneka kwa kanthawi kochepa ndipo kenaka ndikuzimirira. 15 Koma inuyo muyenera kunena kuti, “Ambuye akalola, tikadzakhala ndi moyo, tidzachita zakutizakuti.” 16 Koma mmene zililimu mumangodzitama ndi kudzikuza. Kudzitama konse kotereku ndi koyipa. 17 Aliyense amene amadziwa zabwino zimene amayenera kuchita koma osazichita, ndiye kuti wachimwa.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.