Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 1

BUKU LOYAMBA

Masalimo 1–41

Wodala munthu
    amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa,
kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa,
    kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.
Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova
    ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.
Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi,
    umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake
ndipo masamba ake safota.
    Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.
Sizitero ndi anthu oyipa!
    Iwo ali ngati mungu
    umene umawuluzidwa ndi mphepo.
Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo,
    kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.

Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama,
    koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.

Miyambo 30:1-10

Mawu a Aguri

30 Nawa mawu a Aguri mwana wa Yake wa ku Masa:

Munthuyo anati kwa Itieli, “Inu Mulungu, ine ndatopa.
    Inu Mulungu, ine ndatopa. Ndalefukiratu.

“Ine ndine munthu wopusa kuposa anthu onse;
    ndilibe nzeru zomvetsa zinthu zonga za munthu.
Sindinaphunzire nzeru,
    ndipo Woyerayo sindimudziwa.
Kodi ndani anakwera kumwamba ndi kutsikako?
    Ndani anafumbatapo mphepo mʼmanja mwake?
Ndani anamanga madzi mʼchovala chake?
    Ndani anakhazikitsa mathero onse a dziko lapansi?
Dzina lake ndani? Ndiwuze ngati ukudziwa!
    Ndipo mwana wake dzina lake ndani?

“Mawu ali wonse a Mulungu ndi opanda cholakwika;
    Iye ndi chishango kwa amene amathawira kwa Iye.
Usawonjezepo kanthu pa mawu ake,
    kuopa kuti Iye angadzakudzudzule ndi kukupeza kuti ndiwe wabodza.”

“Inu Yehova, ndikukupemphani zinthu ziwiri
    musandimane zimenezo ndisanafe:
Choyamba, mundichotsere kutali nane mabodza ndi chinyengo.
    Chachiwiri, ndisakhale mʼmphawi kapena munthu wachuma.
    Koma muzindidyetsa chakudya chondikwanira tsiku ndi tsiku
kuopa kuti ndikakhuta kwambiri ndingayambe kukukanani,
    nʼkumanena kuti, ‘Yehova ndiye yaninso?’
Kuopanso kuti ndikakhala wosauka ndingayambe kuba,
    potero nʼkuyipitsa dzina la Mulungu wanga.”

10 “Usamusinjirire wantchito kwa mbuye wake
    kuopa kuti angakutemberere ndipo iweyo nʼkupezeka wolakwa.”

1 Akorinto 2:1-5

Pamene ndinabwera kwa inu, abale, sindinabwere ndi luntha lodziwa kuyankhula kapena nzeru zapamwamba pamene ndinachitira umboni chinsinsi cha Mulungu. Pakuti ndinatsimikiza pamene ndinali ndi inu kuti ndisadziwe kanthu kena kupatula Yesu Khristu wopachikidwayo. Ndinabwera kwa inu wofowoka ndi wamantha, ndiponso wonjenjemera kwambiri. Uthenga ndi ulaliki wanga sunali wa mawu anzeru ndi onyengerera koma woonetsa mphamvu za Mzimu, kuti chikhulupiriro chanu chisatsamire pa nzeru ya anthu koma pa mphamvu za Mulungu.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.