Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.
19 Zakumwamba zimalengeza za ulemerero wa Mulungu;
thambo limalalikira ntchito za manja ake.
2 Tsiku ndi tsiku zimayankhula mawu ambiri,
usiku ndi usiku zimaonetsa poyera nzeru.
3 Palibe kuyankhula, palibe mawu aliwonse;
liwu lawo silimveka.
4 Koma uthenga wawo umapita pa dziko lonse lapansi,
mawuwo amafika mpaka
kumalekezero a dziko lapansi.
5 Dzuwa lili ngati mkwatibwi wobwera kuchokera ku nsanja yake,
ngati katswiri wokondwerera kuthamanga pa mpikisano.
6 Limatuluka kuyambira mbali ina ya thambo
ndi kuzungulira mpaka mbali inanso;
palibe chinthu chotha kupewa kutentha kwake.
7 Lamulo la Yehova ndi langwiro,
kutsitsimutsa moyo.
Maumboni a Yehova ndi odalirika,
amapereka nzeru kwa wopanda nzeru.
8 Malangizo a Yehova ndi olungama,
amapereka chimwemwe mu mtima.
Malamulo a Yehova ndi onyezimira,
amapereka kuwala.
9 Kuopa Yehova ndiye chinthu changwiro,
chimakhala mpaka muyaya.
Maweruzo a Yehova ndi owona
ndipo onse ndi olungama;
10 ndi a mtengowapatali kuposa golide,
kuposa golide weniweni;
ndi otsekemera kuposa uchi,
kuposa uchi wochokera pa chisa chake.
11 Mtumiki wanu amachenjezedwa nawo;
powasunga pali mphotho yayikulu.
12 Ndani angathe kudziwa zolakwa zake?
Mundikhululukire zolakwa zanga zobisika.
13 Muteteze mtumiki wanunso ku machimo ochita akudziwa;
iwo asandilamulire.
Kotero ndidzakhala wosalakwa,
wopanda mlandu wa tchimo lalikulu.
14 Mawu a mʼkamwa mwanga ndi zolingalira za mu mtima mwanga
zikhale zokondweretsa pamaso panu,
Inu Yehova, Thanthwe langa ndi Mpulumutsi wanga.
15 Kuyankha kofatsa kumathetsa mkwiyo,
koma mawu ozaza amautsa ukali.
2 Munthu wanzeru amayankhula zinthu za nzeru,
koma pakamwa pa zitsiru pamatulutsa za uchitsiru.
3 Maso a Yehova ali ponseponse,
amayangʼana pa oyipa ndi abwino omwe.
4 Kuyankhula kodekha kuli ngati mtengo wopatsa moyo,
koma kuyankhula kopotoka kumapweteka mtima.
5 Chitsiru chimanyoza mwambo wa abambo ake,
koma wochenjera amasamala chidzudzulo.
6 Munthu wolungama amakhala ndi chuma chambiri,
zimene woyipa amapindula nazo zimamugwetsa mʼmavuto.
7 Pakamwa pa anthu anzeru pamafalitsa nzeru;
koma mitima ya zitsiru sitero.
8 Nsembe za anthu oyipa zimamunyansa Yehova,
koma amakondwera ndi pemphero la anthu owona mtima.
9 Ntchito za anthu oyipa zimamunyansa Yehova
koma amakonda amene amafunafuna chilungamo.
10 Amene amasiya njira yabwino adzalangidwa koopsa.
Odana ndi chidzudzulo adzafa.
11 Manda ndi chiwonongeko ndi zosabisika pamaso pa Yehova,
nanji mitima ya anthu!
12 Wonyoza sakonda kudzudzulidwa;
iye sapita kwa anthu anzeru.
13 Mtima wokondwa umachititsa nkhope kukhala yachimwemwe,
koma mtima wosweka umawawitsa moyo.
14 Mtima wa munthu wozindikira zinthu umafunafuna nzeru,
koma pakamwa pa zitsiru pamadya uchitsiru wawo.
15 Munthu woponderezedwa masiku ake onse amakhala oyipa,
koma mtima wachimwemwe umakhala pa chisangalalo nthawi zonse.
16 Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono nʼkumaopa Yehova,
kusiyana ndi kukhala ndi chuma chambiri uli pamavuto.
17 Kuli bwino kudyera ndiwo zamasamba pamene pali chikondi,
kusiyana ndi kudyera nyama yangʼombe yonenepa pamene pali udani.
17 Ndi chikhulupiriro Abrahamu, Mulungu atamuyesa, anapereka Isake ngati nsembe. Ngakhale anali munthu woti Mulungu anamulonjeza, anakhala wokonzeka kupereka nsembe mwana wake mmodzi yekhayo. 18 Za mwana ameneyu Mulungu anamuwuza iye kuti, “Zidzukulu zako zidzachokera mwa Isake.” 19 Abrahamu amazindikira kuti Mulungu angathe kuukitsa akufa, ndipo tingathe kunena mofanizira kuti iye analandiranso Isake ngati wouka kwa akufa.
20 Ndi chikhulupiriro Isake anadalitsa Yakobo ndi Esau pa zatsogolo lawo.
21 Ndi chikhulupiriro, pamene Yakobo ankamwalira anadalitsa ana awiri a Yosefe, ndipo anapembedza Mulungu atatsamira ndodo yake.
22 Ndi chikhulupiriro Yosefe ali pafupi kumwalira anayankhula za kutuluka kwa Aisraeli mu Igupto ndipo anawawuza zoti adzachite ndi mafupa ake.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.