Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
BUKU LACHITATU
Masalimo 73–89
Salimo la Asafu.
73 Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli,
kwa iwo amene ndi oyera mtima.
2 Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka;
ndinatsala pangʼono kugwa.
3 Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira,
pamene ndinaona mtendere wa anthu oyipa.
4 Iwo alibe zosautsa;
matupi awo ndi athanzi ndi amphamvu.
5 Saona mavuto monga anthu ena;
sazunzika ngati anthu ena onse.
6 Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo;
amadziveka chiwawa.
7 Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa;
zoyipa zochokera mʼmaganizo awo sizidziwa malire.
8 Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa;
mwa kudzikuza kwawo amaopseza ena nʼkumati, “Tikuponderezani.”
9 Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba
ndipo lilime lawo limayenda pa dziko lapansi.
10 Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo
ndi kumwa madzi mochuluka.
11 Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji?
Kodi Wammwambamwamba angadziwe kalikonse?”
12 Umu ndi mmene oyipa alili;
nthawi zonse ali pabwino ndipo chuma chawo chimachulukirachulukira.
13 Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera;
pachabe ndasamba mʼmanja mwanga mwa kusalakwa kwanga.
14 Tsiku lonse ndapeza mavuto;
ndakhala ndi kulangidwa mmawa uliwonse.
15 Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,”
ndikanachita chosakhulupirika kwa ana anu.
16 Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi,
zinandisautsa kwambiri
17 kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu;
pamenepo ndinamvetsa mathero awo.
18 Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera;
Mumawagwetsa pansi kuti awonongeke.
19 Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa,
amasesedwa kwathunthu ndi mantha!
20 Monga loto pamene wina adzuka,
kotero pamene Inu muuka, Inu Ambuye,
mudzawanyoza ngati maloto chabe.
32 “Ndiye tsono ana inu, ndimvereni;
odala anthu amene amasunga njira zanga.
33 Mverani malangizo anga kuti mukhale ndi nzeru;
musanyozere mawu anga.
34 Wodala munthu amene amandimvera,
amene amakhala pa khomo panga tsiku ndi tsiku,
kudikirira pa chitseko changa.
35 Paja aliyense amene apeza ine wapeza moyo
ndipo Yehova amamukomera mtima.
36 Koma amene alephera kundipeza, amadzipweteka yekha;
onse amene amandida amakonda imfa.”
Za Nzeru ndi Uchitsiru
9 Nzeru inamanga nyumba yake;
inayimika nsanamira zake zisanu ndi ziwiri.
2 Inapha ziweto zake ndipo yasakaniza vinyo wake;
inasakaniza vinyo wake ndi kuyala tebulo lake.
3 Nzeruyo inatuma adzakazi ake,
kuti akakhale pamwamba penipeni pa mzinda ndi kukalengeza kuti,
4 “Aliyense amene ali munthu wamba, abwere kuno!”
Kwa onse opanda nzeru inkanena kuti,
5 “Bwerani, dzadyeni chakudya changa
ndipo dzamweni vinyo amene ndakonza.
6 Lekani zopusa zanu kuti mukhale ndi moyo;
yendani njira ya nzeru yomvetsa zinthu.”
29 Ndi chikhulupiriro Aisraeli anawoloka Nyanja Yofiira ngati pa mtunda powuma, koma Aigupto atayesa kutero anamizidwa.
30 Ndi chikhulupiriro mpanda wa Yeriko unagwa, Aisraeli atawuzungulira kasanu ndi kawiri.
31 Ndi chikhulupiriro Rahabe, mkazi wadama sanaphedwe pamodzi ndi osamvera aja chifukwa analandira bwino ozonda aja ku nyumba kwake.
32 Kodi ndinenenso chiyani? Nthawi yandichepera yoti ndinene za Gideoni, Baraki, Samsoni, Yefita, Davide, Samueli ndi aneneri, 33 amene ndi chikhulupiriro anagonjetsa mafumu, anakhazikitsa chilungamo ndi kulandira zimene zinalonjezedwa. Anatseka pakamwa pa mikango, 34 anazimitsa moto waukali, ndipo anapulumuka osaphedwa ndi lupanga. Anali ofowoka koma analandira mphamvu; anasanduka amphamvu pa nkhondo, nathamangitsa magulu a ankhondo a adani awo. 35 Amayi ena analandira anthu awo amene anafa, ataukitsidwanso. Enanso anazunzidwa ndipo anakana kumasulidwa, kuti adzaukenso ndi moyo wabwino. 36 Ena anawaseka ndi kuwakwapula, pamenenso ena anamangidwa ndi kupita ku ndende. 37 Anagendedwa miyala; anachekedwa pakati; ena anaphedwa ndi lupanga. Iwo anayendayenda atavala zikopa zankhosa ndi zikopa zambuzi, umphawi okhaokha, ozunzidwa ndi kuvutitsidwa. 38 Dziko lapansi silinawayenere. Anayendayenda mʼzipululu ndi mapiri, ndiponso mʼmapanga ndi mʼmaenje.
39 Onsewa anayamikidwa chifukwa cha chikhulupiriro chawo, komabe palibe wa iwo amene analandira zimene analonjezedwa. 40 Mulungu anatikonzera ife kanthu koposa, kuti iwo asayesedwe angwiro popanda ife.
Yesu Chitsanzo Chathu
12 Tsono popeza ifenso tazunguliridwa ndi gulu lalikulu la mboni, tiyeni titaye chilichonse chimene chimatitchinga, makamaka tchimo limene limatikola mosavuta, ndipo tithamange ndi khama mpikisano umene tayambawu. 2 Tiyeni tiyangʼanitsitse Yesu, amene ndi woyamba ndi wotsiriza wa chikhulupiriro chathu. Chifukwa cha chimwemwe chimene chimamudikira anapirira zowawa zapamtanda. Iye ananyoza manyazi a imfa yotere ndipo tsopano akukhala ku dzanja lamanja la mpando waufumu wa Mulungu.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.