Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
12 Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova,
anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
13 Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi
ndi kuona anthu onse;
14 kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira
onse amene amakhala pa dziko lapansi.
15 Iye amene amapanga mitima ya onse,
amaona zonse zimene akuchita.
16 Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo;
palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
17 Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso,
ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
18 Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye;
amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
19 kuwawombola iwo ku imfa
ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
20 Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo;
Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
21 Mwa Iye mitima yathu imakondwera,
pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
22 Chikondi chanu chosatha
chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.
37 “Mtima wanga ukulumphalumpha pa chimenechinso
ndipo ukuchoka mʼmalo mwake.
2 Tamverani! Tamverani kubangula kwa liwu lake,
kugunda kumene kukuchokera mʼkamwa mwake.
3 Iye amaponya chingʼaningʼani chake pansi pa thambo lonse
ndipo amachitumiza ku dziko lapansi.
4 Pambuyo pake kubangula kwake kumamveka.
Iye amabangula ndi liwu lake laulemerero.
Pamene wabangula,
palibe chimene amalephera kuchita.
5 Liwu la Mulungu limabangula mʼnjira zambiri zodabwitsa
Iye amachita zinthu zazikulu zimene sitingathe kuzimvetsa.
6 Amalamula chisanu chowundana kuti, ‘Igwa pa dziko lapansi,’
ndipo amalamulanso mvula yamawawa kuti, ‘Khala mvula yamphamvu.’
7 Kuti anthu onse amene anawalenga athe kuzindikira ntchito yake.
Iye amalepheretsa anthu kugwira ntchito zawo.
8 Zirombo zimakabisala
ndipo zimakhala mʼmaenje mwawo.
9 Mphepo yamkuntho imatuluka ku malo ake,
kuzizira kumatuluka mʼmphepo yamkunthoyo.
10 Mpweya wa Mulungu umawunditsa madzi
ndipo madzi a mʼnyanja amawuma kuti gwaa.
11 Iye amadzaza mitambo ndi madzi a mvula,
amabalalitsa zingʼaningʼani zake kuchokera mʼmitambomo.
12 Mulungu amayendetsa mitamboyo
mozungulirazungulira dziko lonse lapansi
kuti ichite zonse zimene Iye akufuna pa dziko lapansi.
13 Iye amagwetsa mvula kuti alange anthu,
kapena kubweretsa chinyontho pa dziko lapansi kuti aonetse chikondi chake.
50 Ndikunenetsa, abale, kuti thupi ndi magazi sizingathe kulowa mu ufumu wa Mulungu, ndipo zimene zimavunda sizingathe kulowa kumene zinthu sizivunda. 51 Tamverani, ndikuwuzeni chinsinsi. Tonse sitidzagona tulo, koma tonse tidzasandulika. 52 Zidzachitika mwadzidzidzi, mʼkamphindi kochepa, monga ngati kuphethira kwa diso, pa lipenga lotsiriza. Pakuti lipenga lidzalira, akufa adzaukitsidwa opanda chovunda, ndipo ife tidzasandulika. 53 Pakuti chovunda chiyenera kuvala chosavunda, ndi thupi ili lakufa liyenera kuvala losafa. 54 Pamene thupi lovundali likadzasanduka losavunda, ndipo thupi lotha kufali likadzasanduka losatha kufa, pamenepo zidzakwaniritsidwa zimene zinalembedwa zakuti, “Imfa yogonjetsedwa kwathunthu.”
55 “Iwe imfa, kupambana kwako kuli kuti?
Iwe imfa, ululu wako uli kuti?”
56 Ululu wa imfa ndi tchimo, ndipo mphamvu ya tchimo ndi lamulo. 57 Koma tiyamike Mulungu amene amatipambanitsa mwa Ambuye athu Yesu Khristu.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.