Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
150 Tamandani Yehova.
Tamandani Mulungu mʼmalo ake opatulika;
mutamandeni ku thambo lake lamphamvu.
2 Mutamandeni chifukwa cha machitidwe ake amphamvu;
mutamandeni chifukwa cha ukulu wake wopambana.
3 Mutamandeni poyimba malipenga,
mutamandeni ndi pangwe ndi zeze.
4 Mutamandeni ndi matambolini ndi kuvina,
mutamandeni ndi zingwe ndi zitoliro.
5 Mutamandeni ndi ziwaya zolira za malipenga,
mutamandeni ndi ziwaya zolira kwambiri.
6 Chamoyo chilichonse chopuma chitamande Yehova.
Tamandani Yehova.
15 Ndipo ndidzabwerera ku malo anga
mpaka anthu anga atavomereza kulakwa kwawo.
Ndipo iwo adzafunafuna nkhope yanga;
mʼmasautso awo adzandifunitsitsa Ine.”
Kusalapa kwa Israeli
6 “Bwerani, tiyeni tibwerere kwa Yehova.
Iye watikhadzula,
koma adzatichiritsa.
Iye wativulaza,
koma adzamanga mabala athu.
2 Pakapita masiku awiri adzatitsitsimutsa;
pa tsiku lachitatu Iye adzatiukitsa
kuti tikhale ndi moyo pamaso pake.
3 Tiyeni timudziwe Yehova,
tiyeni tilimbike kumudziwa Iye.
Adzabwera kwa ife mosakayikira konse
ngati kutuluka kwa dzuwa;
adzabwera kwa ife ngati mvula ya mʼchilimwe,
ngati mvula ya nthawi yamphukira imene imakhathamiritsa nthaka.”
4 Iwe Efereimu, kodi ndichite nawe chiyani?
Kodi ndichite nawe chiyani, iwe Yuda?
Chikondi chanu chili ngati nkhungu yammawa,
ngati mame a mmamawa amene amakamuka msanga.
5 Choncho ndakuwazani ngati nkhuni kudzera mwa aneneri anga,
ndakuphani ndi mawu a pakamwa panga;
chigamulo changa chinangʼanima ngati mphenzi pa inu.
6 Pakuti Ine ndimafuna chifundo osati nsembe,
ndi kudziwa Mulungu kulekana ndi nsembe zopsereza.
1 Ndine mkulu wampingo, kulembera:
Mayi wosankhidwa ndi Mulungu ndi kwa ana ake amene ndimawakonda mʼchoonadi. Ndipo sindine ndekha amene ndimawakonda, komanso onse odziwa choonadi. 2 Timakukondani chifukwa cha choonadi chimene chimakhala mwa ife ndipo chidzakhala mwa ife mpaka muyaya.
3 Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi kwa Yesu Khristu, Mwana wa Atate, zikhale ndi ife mʼchoonadi ndi mʼchikondi.
Choonadi ndi Chikondi
4 Ndinakondwera kwambiri nditapeza ana anu ena akuyenda mʼchoonadi, monga Atate anatilamulira. 5 Ndipo tsopano, amayi wokondedwa, sindikukulemberani lamulo latsopano koma lomwe lija takhala nalo kuyambira pachiyambi. Ine ndikukupemphani kuti tidzikondana wina ndi mnzake. 6 Ndipo chikondi ndiye kuyenda momvera malamulo ake. Lamulo lake ndi lakuti mukhale moyo wachikondi monga munamva kuyambira pachiyambi.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.