Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 150

150 Tamandani Yehova.

Tamandani Mulungu mʼmalo ake opatulika;
    mutamandeni ku thambo lake lamphamvu.
Mutamandeni chifukwa cha machitidwe ake amphamvu;
    mutamandeni chifukwa cha ukulu wake wopambana.
Mutamandeni poyimba malipenga,
    mutamandeni ndi pangwe ndi zeze.
Mutamandeni ndi matambolini ndi kuvina,
    mutamandeni ndi zingwe ndi zitoliro.
Mutamandeni ndi ziwaya zolira za malipenga,
    mutamandeni ndi ziwaya zolira kwambiri.

Chamoyo chilichonse chopuma chitamande Yehova.

Tamandani Yehova.

Hoseya 5:15-6:6

15 Ndipo ndidzabwerera ku malo anga
    mpaka anthu anga atavomereza kulakwa kwawo.
Ndipo iwo adzafunafuna nkhope yanga;
    mʼmasautso awo adzandifunitsitsa Ine.”

Kusalapa kwa Israeli

“Bwerani, tiyeni tibwerere kwa Yehova.
Iye watikhadzula,
    koma adzatichiritsa.
Iye wativulaza,
    koma adzamanga mabala athu.
Pakapita masiku awiri adzatitsitsimutsa;
    pa tsiku lachitatu Iye adzatiukitsa
    kuti tikhale ndi moyo pamaso pake.
Tiyeni timudziwe Yehova,
    tiyeni tilimbike kumudziwa Iye.
Adzabwera kwa ife mosakayikira konse
    ngati kutuluka kwa dzuwa;
adzabwera kwa ife ngati mvula ya mʼchilimwe,
    ngati mvula ya nthawi yamphukira imene imakhathamiritsa nthaka.”

Iwe Efereimu, kodi ndichite nawe chiyani?
    Kodi ndichite nawe chiyani, iwe Yuda?
Chikondi chanu chili ngati nkhungu yammawa,
    ngati mame a mmamawa amene amakamuka msanga.
Choncho ndakuwazani ngati nkhuni kudzera mwa aneneri anga,
    ndakuphani ndi mawu a pakamwa panga;
    chigamulo changa chinangʼanima ngati mphenzi pa inu.
Pakuti Ine ndimafuna chifundo osati nsembe,
    ndi kudziwa Mulungu kulekana ndi nsembe zopsereza.

2 Yohane 1-6

Ndine mkulu wampingo, kulembera:

Mayi wosankhidwa ndi Mulungu ndi kwa ana ake amene ndimawakonda mʼchoonadi. Ndipo sindine ndekha amene ndimawakonda, komanso onse odziwa choonadi. Timakukondani chifukwa cha choonadi chimene chimakhala mwa ife ndipo chidzakhala mwa ife mpaka muyaya.

Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi kwa Yesu Khristu, Mwana wa Atate, zikhale ndi ife mʼchoonadi ndi mʼchikondi.

Choonadi ndi Chikondi

Ndinakondwera kwambiri nditapeza ana anu ena akuyenda mʼchoonadi, monga Atate anatilamulira. Ndipo tsopano, amayi wokondedwa, sindikukulemberani lamulo latsopano koma lomwe lija takhala nalo kuyambira pachiyambi. Ine ndikukupemphani kuti tidzikondana wina ndi mnzake. Ndipo chikondi ndiye kuyenda momvera malamulo ake. Lamulo lake ndi lakuti mukhale moyo wachikondi monga munamva kuyambira pachiyambi.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.