Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
12 Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya;
kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.
13 Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni
pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo;
nthawi yoyikika yafika.
14 Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu;
fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.
15 Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova,
mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.
16 Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni
ndi kuonekera mu ulemerero wake.
17 Iye adzayankha pemphero la anthu otayika;
sadzanyoza kupempha kwawo.
18 Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo,
kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:
19 “Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba,
kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,
20 kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende,
kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”
21 Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni
ndi matamando ake mu Yerusalemu,
22 pamene mitundu ya anthu ndi maufumu
adzasonkhana kuti alambire Yehova.
23 Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga;
Iyeyo anafupikitsa masiku anga.
24 Choncho Ine ndinati:
“Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga;
zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.
25 Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi
ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.
26 Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo;
zidzatha ngati chovala.
Mudzazisintha ngati chovala
ndipo zidzatayidwa.
27 Koma Inu simusintha,
ndipo zaka zanu sizidzatha.
28 Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu;
zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”
Mawu a Yobu
6 Tsono Yobu anayankha kuti,
2 “Achikhala mavuto anga anayezedwa,
ndipo zipsinjo zanga zonse zikanayikidwa pa sikelo!
3 Ndithu, zikanalemera kupambana mchenga wa ku nyanja;
nʼchifukwa chake mawu anga akhala okhadzula.
4 Mivi ya Wamphamvuzonse yandibaya,
thupi langa likumva ululu wa miviyo;
zoopsa za Mulungu zandizinga.
5 Kodi bulu wakuthengo amalira akakhala ndi msipu,
nanga ngʼombe imalira ikakhala ndi chakudya?
6 Kodi chakudya chosakoma nʼkuchidya chopanda mchere,
nanga choyera cha dzira chimakoma?
7 Zakudya zimenezi sindifuna nʼkuzilawa komwe;
zakudya zimenezi zimabwerera kukhosi.
8 “Aa, ndikanalandira chimene ndikuchipempha,
chikhala Mulungu anandipatsa chimene ndikuchiyembekezera,
9 achikhala chinamukomera Mulungu kuti anditswanye,
kulola dzanja lake kuti lindimenye ndi kundiwonongeratu!
10 Pamenepo ine ndikanakhalabe ndi chitonthozo ichi,
ndikanakondwa mu ululu wanga wosalekezawu
podziwa kuti sindinakane mawu a Woyerayo.
11 “Kodi mphamvu zanga nʼzotani kuti ndizikhalabe ndi chiyembekezo?
Nanga zoyembekezera zanga nʼzotani kuti ndipirirebe?
12 Kodi ine ndili ndi mphamvu?
Nanga thupi langa ndi lolimba ngati chitsulo?
13 Kodi ndili ndi mphamvu zodzithandizira ndekha,
nanga pakuti thandizo lachotsedwa kwa ine?
Magulu a Anthu Amutsata Yesu
7 Yesu anachoka pamodzi ndi ophunzira ake napita ku nyanja, ndipo gulu lalikulu la anthu lochokera ku Galileya linamutsata. 8 Atamva zonse zimene amachita, anthu ambiri anabwera kwa Iye kuchokera ku Yudeya, Yerusalemu, Idumeya ndi madera a ku tsidya kwa mtsinje wa Yorodani ndi ozungulira Turo ndi Sidoni. 9 Chifukwa cha gulu la anthu, anawuza ophunzira ake kuti apezeretu bwato likhale, kuti anthu angamupanikize. 10 Pakuti anachiritsa ambiri, kotero kuti iwo amene anali ndi matenda amakankhana kutsogolo kuti amukhudze. 11 Nthawi iliyonse mizimu yoyipa ikamuona, imagwa pansi pamaso pake ndi kufuwula kuti, “Inu ndinu Mwana wa Mulungu!” 12 Koma anayichenjeza mwamphamvu kuti isanene kuti Iye anali ndani.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.