Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Nyimbo ya anamwali.
46 Mulungu ndiye kothawira kwathu ndi mphamvu yathu,
thandizo lopezekeratu pa nthawi ya mavuto.
2 Nʼchifukwa chake sitidzaopa ngakhale dziko lapansi lisunthike,
ngakhale mapiri agwe pakati pa nyanja,
3 ngakhale madzi ake atakokoma ndi kuchita thovu,
ngakhale mapiri agwedezeke ndi kukokoma kwake.
4 Kuli mtsinje umene njira zake za madzi zimasangalatsa mzinda wa Mulungu,
malo oyera kumene Wammwambamwamba amakhalako.
5 Mulungu ali mʼkati mwake, iwo sudzagwa;
Mulungu adzawuthandiza mmawa.
6 Mitundu ikupokosera, mafumu akugwa;
Iye wakweza mawu ake, dziko lapansi likusungunuka.
7 Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ife,
Mulungu wa Yakobo ndi linga lathu.
8 Bwerani kuti mudzaone ntchito za Yehova,
chiwonongeko chimene wachibweretsa pa dziko lapansi.
9 Iye amathetsa nkhondo ku malekezero a dziko lapansi;
Iye amathyola uta ndi kupindapinda mkondo;
amatentha zishango ndi moto.
10 Iye akuti, “Khala chete, ndipo dziwa kuti ndine Mulungu;
ndidzakwezedwa pakati pa mitundu ya anthu;
ine ndidzakwezedwa mʼdziko lapansi.”
11 Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ife,
Mulungu wa Yakobo ndi linga lathu.
Nzeru Ikuyitana
8 Kodi nzeru sikuyitana?
Kodi nzeru yomvetsa zinthu sinakweze mawu ake?
2 Nzeru imayima pa zitunda mʼmbali mwa njira,
imayima pa mphambano ya misewu.
3 Imafuwula pafupi ndi zipata zolowera mu mzinda,
pa makomo olowera imafuwula kuti,
4 Inu anthu, ndikuyitana inu;
ndikuyitanatu anthu onse.
5 Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera;
inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu.
6 Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri;
ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama.
7 Pakamwa panga pamayankhula zoona
ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa.
8 Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama;
mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka.
9 Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona;
kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza.
10 Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva,
nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino.
11 Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali,
ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru.
12 Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera.
Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino.
13 Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa.
Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama,
kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga.
14 Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino;
ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu.
15 Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira.
Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama.
16 Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula.
Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko.
17 Ndimakonda amene amandikonda,
ndipo amene amandifunafuna amandipeza.
18 Ine ndili ndi chuma ndi ulemu,
chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika.
19 Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala;
zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri.
20 Ndimachita zinthu zolungama.
Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo.
21 Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda
ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma.
Yesu Asankha Ophunzira Khumi ndi Awiri
13 Yesu anakwera ku phiri ndipo anayitana amene anawafuna, ndipo anabwera kwa Iye. 14 Iye anasankha khumi ndi awiri, nawayika akhale atumwi; pokhala ndi Iye aziwatuma kukalalikira 15 ndi kuti akhale ndi ulamuliro wotulutsa ziwanda. 16 Awa ndi khumi ndi awiri amene anawasankha: Simoni (amene anapatsidwa dzina lakuti Petro); 17 Yakobo mwana wa Zebedayo, ndi mʼbale wake Yohane (iwowa anawapatsa dzina lakuti Bowanege, ndiye kuti ana a bingu); 18 Andreya, Filipo, Bartumeyu, Mateyu, Tomasi, Yakobo mwana wa Alufeyo, Tadeyo, Simoni Zelote, 19 ndi Yudasi Isikarioti, amene anamupereka Iye.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.