Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
148 Tamandani Yehova.
Tamandani Yehova, inu a kumwamba,
mutamandeni Iye, inu a mlengalenga.
2 Mutamandeni, inu angelo ake onse,
mutamandeni, mutamandeni, inu zolengedwa za mmwamba.
3 Mutamandeni, inu dzuwa ndi mwezi,
mutamandeni, inu nonse nyenyezi zowala.
4 Mutamandeni, inu thambo la kumwambamwamba
ndi inu madzi a pamwamba pa thambo.
5 Zonse zitamande dzina la Yehova
pakuti Iye analamula ndipo zinalengedwa.
6 Iye anaziyika pa malo ake ku nthawi za nthawi;
analamula ndipo sizidzatha.
7 Tamandani Yehova pa dziko lapansi,
inu zolengedwa zikuluzikulu za mʼnyanja, ndi nyanja zonse zakuya,
8 inu zingʼaningʼani ndi matalala, chipale ndi mitambo,
mphepo yamkuntho imene imakwaniritsa mawu ake,
9 inu mapiri ndi zitunda zonse,
inu mitengo ya zipatso ndi mikungudza yonse,
10 inu nyama zakuthengo ndi ngʼombe zonse,
inu zolengedwa zingʼonozingʼono ndi mbalame zowuluka.
11 Inu mafumu a dziko lapansi ndi anthu a mitundu yonse,
inu akalonga ndi olamulira a dziko lapansi.
12 Inu anyamata ndi anamwali,
inu nkhalamba ndi ana omwe.
13 Onsewo atamande dzina la Yehova
pakuti dzina lake lokha ndi lolemekezeka;
ulemerero wake ndi woopsa pa dziko lapansi pano ndi kumwamba komwe.
14 Iye wakwezera nyanga anthu ake,
matamando a anthu ake onse oyera mtima,
Aisraeli, anthu a pamtima pake.
Tamandani Yehova.
5 Yehova anandiwumba ine
mʼmimba mwa amayi anga kuti ndikhale mtumiki wake
kuti ndibweze fuko la Yakobo kwa Iye
ndi kusonkhanitsa Israeli kwa Iye,
choncho ndimalemekezeka mʼmaso mwa Yehova,
ndipo ndimapeza mphamvu mwa Mulungu wanga.
6 Yehovayo tsono akuti,
“Nʼchinthu chochepa kwambiri kwa iwe kuti ukhale mtumiki wanga,
kuti udzutse mafuko a Yakobo
ndi kuwabweretsa kwawo Aisraeli amene anapulumuka.
Choncho iwe udzakhala ngati chowunikira,
udzafikitsa uthenga wa chipulumutso changa ku mathero a dziko lapansi.”
7 Yehova Mpulumutsi ndi Woyerayo wa Israeli akuyankhula,
Woyerayo wa Israeli akunena,
amene mitundu ya anthu inamuda,
amenenso anali kapolo wa mafumu ankhanza uja kuti,
“Mafumu adzaona ntchito ya chipulumutso changa ndipo adzayimirira.
Akalonga nawonso adzagwada pansi.
Zimenezi zidzachitika chifukwa cha Yehova amene ndi wokhulupirika
ndi Woyerayo wa Israeli amene wakusankha iwe.”
Kubwezeretsedwa kwa Israeli
8 Yehova akuti,
“Pa nthawi imene ndinakukomera mtima ndinakuyankha,
ndipo pa tsiku lachipulumutso ndinakuthandiza;
ndinakusunga ndi kukusandutsa
kuti ukhale pangano kwa anthu,
kuti dziko libwerere mwakale
ndi kuti cholowa changa chowonongeka chija ndichigawegawenso.
9 Ndidzawuza a mʼndende kuti atuluke
ndi a mu mdima kuti aonekere poyera.
“Adzapeza chakudya mʼmphepete mwa njira
ndi msipu pa mʼmalo owuma.
10 Iwo sadzamva njala kapena ludzu,
kutentha kwa mʼchipululu kapena dzuwa silidzawapsereza;
chifukwa Iye amene amawachitira chifundo adzawatsogolera
ndi kuwaperekeza ku akasupe a madzi.
11 Mapiri anga onse ndidzawasandutsa njira yoyendamo,
ndipo misewu yanga yayikulu ndidzayikweza.
12 Taonani, anthu anga adzachokera kutali,
ena kumpoto, ena kumadzulo,
enanso adzachokera ku chigawo cha Asuwani.”
13 Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga;
kondwera, iwe dziko lapansi;
imbani nyimbo inu mapiri!
Pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake,
ndipo wachitira chifundo anthu ake ovutika.
14 Koma Ziyoni anati, “Yehova wandisiya,
Ambuye wandiyiwala.”
15 “Kodi amayi angathe kuyiwala mwana wawo wakubere
ndi kusachitira chifundo mwana amene anabereka iwo eni?
Ngakhale iye angathe kuyiwala,
Ine sindidzakuyiwala iwe!
Amayi ndi Abale Ake a Yesu
46 Pamene Yesu anali kuyankhulabe ndi gulu la anthu, amayi ndi abale ake anayimirira kunja, akufuna kuyankhulana naye. 47 Wina anamuwuza Iye kuti, “Amayi ndi abale anu ayima kunjaku akufuna kuyankhulana nanu.”
48 Iye anayankha kuti, “Amayi anga ndani ndipo abale anga ndi ndani?” 49 Ndipo akuloza ophunzira ake, Iye anati, “Awa ndiwo amayi anga ndi abale anga. 50 Pakuti aliyense amene achita chifuniro cha Atate anga akumwamba ndiye mʼbale wanga, mlongo wanga ndi amayi anga.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.